Salimo 54
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”
1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;
onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.
2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu
mvetserani mawu a pakamwa panga.
3Alendo akundithira nkhondo;
anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,
anthu amene salabadira za Mulungu.
4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;
Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.
5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;
mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.
6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;
ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,
pakuti ndi labwino.
7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,
ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.
Salmo 54Sal 54 En el texto hebreo 54:1-7 se numera 54:3-9.
Al director musical. Acompáñese con instrumentos de cuerda. Masquil de David, cuando gente de Zif fue a decirle a Saúl: «¿No está David escondido entre nosotros?».
1¡Sálvame, oh Dios, por tu nombre!
¡Defiéndeme con tu poder!
2¡Escucha, oh Dios, mi oración!
¡Presta oído a las palabras de mi boca!
3Pues gente extraña se levanta contra mí;
gente violenta procura matarme,
sin tener en cuenta a Dios. Selah
4Pero Dios es mi socorro;
el Señor es quien me sostiene.
5Hará recaer el mal sobre mis enemigos.
Por tu fidelidad, Señor, ¡destrúyelos!
6Te presentaré una ofrenda voluntaria
y alabaré tu nombre, Señor, porque es bueno;
7pues me has librado de todas mis angustias
y mis ojos han visto la derrota de mis enemigos.