Masalimo 54 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 54:1-7

Salimo 54

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Ndakatulo ya Davide. Pamene anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ndipo anati, “Kodi Davide sakubisala pakati pathu.”

1Pulumutseni Inu Mulungu, mwa dzina lanu;

onetsani kuti ndine wosalakwa mwamphamvu yanu.

2Imvani pemphero langa, Inu Mulungu

mvetserani mawu a pakamwa panga.

3Alendo akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufunafuna moyo wanga,

anthu amene salabadira za Mulungu.

4Zoonadi Mulungu ndi thandizo langa;

Ambuye ndiye amene amandichirikiza ine.

5Lolani kuti choyipa chifike pa iwo amene amandichita chipongwe;

mwa kukhulupirika kwanu awonongeni.

6Ine ndidzapereka nsembe yaufulu kwa Inu;

ndidzatamanda dzina lanu, Inu Yehova,

pakuti ndi labwino.

7Pakuti Iyeyo wandipulumutsa ku masautso anga onse,

ndipo maso anga apenya kupambana kwa pa adani anga.

Nueva Versión Internacional

Salmo 54:1-7

Salmo 54Sal 54 En el texto hebreo 54:1-7 se numera 54:3-9.

Al director musical. Acompáñese con instrumentos de cuerda. Masquil de David, cuando gente de Zif fue a decirle a Saúl: «¿No está David escondido entre nosotros?».

1¡Sálvame, oh Dios, por tu nombre!

¡Defiéndeme con tu poder!

2¡Escucha, oh Dios, mi oración!

¡Presta oído a las palabras de mi boca!

3Pues gente extraña se levanta contra mí;

gente violenta procura matarme,

sin tener en cuenta a Dios. Selah

4Pero Dios es mi socorro;

el Señor es quien me sostiene.

5Hará recaer el mal sobre mis enemigos.

Por tu fidelidad, Señor, ¡destrúyelos!

6Te presentaré una ofrenda voluntaria

y alabaré tu nombre, Señor, porque es bueno;

7pues me has librado de todas mis angustias

y mis ojos han visto la derrota de mis enemigos.