Masalimo 51 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 51:1-19

Salimo 51

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu,

molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;

molingana ndi chifundo chanu chachikulu

mufafanize mphulupulu zanga.

2Munditsuke zolakwa zanga zonse

ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.

3Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga,

ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.

4Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa

ndipo ndachita zoyipa pamaso panu,

Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama

pamene muyankhula ndi pamene muweruza.

5Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa,

wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.

6Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga;

mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.

7Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera,

munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala

8Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo,

mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.

9Mufulatire machimo anga

ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.

10Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu

ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.

11Musandichotse pamaso panu

kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.

12Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu

ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.

13Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu

kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.

14Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu,

Mulungu wa chipulumutso changa,

ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.

15Inu Ambuye tsekulani milomo yanga,

ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.

16Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba.

Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.

17Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka;

mtima wosweka ndi wachisoni

Inu Mulungu simudzawunyoza.

18Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere;

mumange makoma a Yerusalemu.

19Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo,

nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu;

ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.

King James Version

Psalms 51:1-19

To the chief Musician, A Psalm of David, when Nathan the prophet came unto him, after he had gone in to Bath-sheba.

1Have mercy upon me, O God, according to thy lovingkindness: according unto the multitude of thy tender mercies blot out my transgressions.

2Wash me throughly from mine iniquity, and cleanse me from my sin.

3For I acknowledge my transgressions: and my sin is ever before me.

4Against thee, thee only, have I sinned, and done this evil in thy sight: that thou mightest be justified when thou speakest, and be clear when thou judgest.

5Behold, I was shapen in iniquity; and in sin did my mother conceive me.51.5 conceive…: Heb. warm me

6Behold, thou desirest truth in the inward parts: and in the hidden part thou shalt make me to know wisdom.

7Purge me with hyssop, and I shall be clean: wash me, and I shall be whiter than snow.

8Make me to hear joy and gladness; that the bones which thou hast broken may rejoice.

9Hide thy face from my sins, and blot out all mine iniquities.

10Create in me a clean heart, O God; and renew a right spirit within me.51.10 right: or, constant

11Cast me not away from thy presence; and take not thy holy spirit from me.

12Restore unto me the joy of thy salvation; and uphold me with thy free spirit.

13Then will I teach transgressors thy ways; and sinners shall be converted unto thee.

14Deliver me from bloodguiltiness, O God, thou God of my salvation: and my tongue shall sing aloud of thy righteousness.51.14 bloodguiltiness: Heb. bloods

15O Lord, open thou my lips; and my mouth shall shew forth thy praise.

16For thou desirest not sacrifice; else would I give it: thou delightest not in burnt offering.51.16 else…: or, that I should

17The sacrifices of God are a broken spirit: a broken and a contrite heart, O God, thou wilt not despise.

18Do good in thy good pleasure unto Zion: build thou the walls of Jerusalem.

19Then shalt thou be pleased with the sacrifices of righteousness, with burnt offering and whole burnt offering: then shall they offer bullocks upon thine altar.