Masalimo 49 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 49:1-20

Salimo 49

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Imvani izi anthu a mitundu yonse;

mvetserani, nonse amene mumakhala pa dziko lonse,

2anthu wamba pamodzi ndi anthu odziwika,

olemera pamodzinso ndi osauka:

3Pakamwa panga padzayankhula mawu anzeru;

mawu ochokera mu mtima mwanga adzapereka nzeru.

4Ndidzatchera khutu langa ku mwambo,

ndi pangwe ndidzafotokoza momveka mwambi wanga.

5Ine ndichitirenji mantha pamene masiku oyipa afika,

pamene achinyengo oyipa andizungulira.

6Iwo amene adalira kulemera kwawo

ndi kutamandira kuchuluka kwa chuma chawo?

7Palibe munthu amene angawombole moyo wa mnzake

kapena kuperekera mnzake dipo kwa Mulungu.

8Dipo la moyo ndi la mtengowapatali,

palibe malipiro amene angakwanire,

9kuti iye akhale ndi moyo mpaka muyaya

ndi kusapita ku manda.

10Pakuti onse amaona kuti anthu anzeru amamwalira;

opusa ndi opanda nzeru chimodzimodzinso amawonongeka

ndipo amasiyira chuma chawo anthu ena.

11Manda awo adzakhala nyumba zawo mpaka muyaya,

malo awo okhalako kwa nthawi yonse ya mibado yawo,

ngakhale anatchula malo mayina awo.

12Ngakhale munthu akhale wachuma chotani,

adzafa ngati nyama.

13Izi ndi zimene zimachitikira iwo amene amadzidalira okha,

ndi owatsatira awo amene amavomereza zimene amayankhula.

Sela

14Monga nkhosa iwo ayenera kupita ku manda,

ndipo imfa idzawadya.

Olungama adzawalamulira mmawa;

matupi awo adzavunda mʼmanda,

kutali ndi nyumba zawo zaufumu.

15Koma Mulungu adzawombola moyo wanga kuchoka ku manda;

ndithu Iye adzanditengera kwa Iye mwini.

16Usavutike mu mtima pamene munthu akulemera,

pamene ulemerero wa nyumba yake ukuchulukirachulukira;

17Pakuti sadzatenga kanthu pamodzi naye pamene wamwalira,

ulemerero wake sudzapita pamodzi naye.

18Ngakhale pamene munthuyo ali moyo amadziyesa wodala,

ndipo ngakhale atamandidwe pamene zinthu zikumuyendera bwino,

19iyeyo adzakakhala pamodzi ndi mʼbado wa makolo ake,

amene sadzaonanso kuwala.

20Munthu amene ali ndi chuma koma wopanda nzeru

adzafa ngati nyama yakuthengo.

Hoffnung für Alle

Psalm 49:1-21

Das Leben ist nicht käuflich!

1Ein Lied der Nachkommen von Korach.

2Hört zu, all ihr Völker!

Horcht auf, ihr Bewohner der Erde!

3Ob ihr einfache oder vornehme Leute seid,

ob arm oder reich –

4ich habe euch Wichtiges zu sagen!

Meine Worte sind die Worte eines Weisen,

und tiefe Einsicht spricht aus ihnen.

5Denn ich höre genau zu, wenn Gott mir Sprüche der Weisheit vermittelt,49,5 Wörtlich: ich neige mein Ohr zu einem Spruch.

beim Spiel auf der Laute will ich euch nun ihre Bedeutung erklären.

6Warum sollte ich mich fürchten, wenn ein Unglück naht,

wenn ich umgeben bin von boshaften und hinterhältigen Menschen?

7Sie verlassen sich auf ihren Reichtum,

mit Geld und Luxus protzen sie.

8Doch niemand kann für das Leben seines Freundes bezahlen,

niemand kann ihn bei Gott vom Tod freikaufen.

9Denn ein Menschenleben kann man nicht mit Gold aufwiegen –

aller Reichtum dieser Welt wäre noch zu wenig!

10Keiner lebt hier ewig,

niemand kann dem Grab entrinnen.

11Jeder kann es sehen: Auch die klügsten Menschen werden vom Tod ereilt,

genauso wie Tagträumer und Dummköpfe.

Ihren Besitz müssen sie zurücklassen – für andere!

12Sie bilden sich ein, dass ihre Häuser für die Ewigkeit gebaut sind

und alle Generationen überdauern.

Aber es hilft ihnen nichts,

selbst wenn sie ganze Länder besessen haben.49,12 Oder nach der griechischen Übersetzung: (Vers 12) Gräber sind auf ewig ihre Behausung, ihre Wohnung für alle Generationen, auch wenn sie ganze Länder besessen haben.

13Reichtum und Ansehen erhalten keinen Menschen am Leben;

er verendet wie das Vieh.

14Dieses Schicksal trifft alle, die auf sich selbst vertrauen

und sich in ihrem überheblichen Gerede gefallen:

15Ahnungslos wie Schafe trotten sie in die Totenwelt;

ihr Hirte dort ist niemand anderes als der Tod.

Ihr Körper verwest im Grab, und ihre vornehmen Häuser zerfallen.

Dann bricht ein neuer Morgen an –

der Tag, an dem die aufrichtigen Menschen über sie triumphieren.49,15 Der hebräische Text ist nur schwer zu deuten.

16Ich bin gewiss: Gott wird mich erlösen,

er wird mich den Klauen des Todes entreißen.

17Lass dich nicht einschüchtern, wenn einer steinreich wird

und sein Haus immer prachtvoller ausstattet!

18Nichts kann er davon mitnehmen, wenn er stirbt;

was er angehäuft hat, folgt ihm nicht ins Grab.

19Er preist sich selbst: »Ich bin meines Glückes Schmied!«,

und man schmeichelt ihm, weil er so erfolgreich ist.

20Und doch kommt auch er dorthin, wo seine Vorfahren sind,

die nie mehr das Licht sehen.

21Ein Mensch mag zu Reichtum und Ansehen kommen;

aber wenn er keine Einsicht erlangt, verendet er wie das Vieh.