Masalimo 48 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 48:1-14

Salimo 48

Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1Wamkulu ndi Yehova, ndi woyenera kwambiri matamando

mu mzinda wa Mulungu wathu, phiri lake loyera.

2Lokongola mu utali mwake,

chimwemwe cha dziko lonse lapansi.

Malo aatali kwambiri a Zafoni ndiye Phiri la Ziyoni,

mzinda wa Mfumu yayikulu.

3Mulungu ali mu malinga ake;

Iye wadzionetsa yekha kuti ndiye malinga akewo.

4Pamene mafumu anasonkhana pamodzi,

pamene anayendera pamodzi kudzalimbana nafe,

5iwo anaona mzindawo ndipo anadabwa kwambiri;

anathawa ndi mantha aakulu.

6Pomwepo anagwidwa nako kunjenjemera,

ululu wonga wa mkazi woyembekezera pa nthawi yochira.

7Inu munawawononga monga sitima zapamadzi za ku Tarisisi

zitawonongeka ndi mphepo ya kummawa.

8Monga momwe tinamvera,

kotero ife tinaona

mu mzinda wa Yehova Wamphamvuzonse,

mu mzinda wa Mulungu wathu.

Mulungu adzawuteteza kwamuyaya.

9Mʼkati mwa Nyumba yanu Mulungu,

ife timalingaliramo zachikondi chanu chosasinthika.

10Monga dzina lanu, Inu Mulungu,

matamando anu amafika ku malekezero a dziko lapansi

dzanja lanu lamanja ladzaza ndi chilungamo.

11Phiri la Ziyoni likukondwera,

midzi ya Yuda ndi yosangalala

chifukwa cha maweruzo anu.

12Yendayendani mu Ziyoni, uzungulireni mzindawo,

werengani nsanja zake.

13Yangʼanitsitsani bwino mipanda yake,

penyetsetsani malinga ake,

kuti mudzafotokoze za izo ku mʼbado wotsatira.

14Pakuti Mulungu uyu ndi Mulungu wathu ku nthawi zosatha;

Iye adzakhala mtsogoleri wathu mpaka ku mapeto.

Hoffnung für Alle

Psalm 48:1-15

Gott liebt Jerusalem

1Ein Lied der Nachkommen von Korach.

2Groß ist der Herr!

Lobt ihn in Jerusalem, der Stadt unseres Gottes,

auf seinem heiligen Berg!

3Der Berg Zion ragt im Norden auf48,3 Oder: Der Berg Zion, die Höhenzüge des Berges Zafon. – Der Zafon galt in der kanaanitischen Mythologie als heiliger Ort, an dem sich die Götter versammelten. Somit würde der Zion hier als der wahre »Götterberg« gepriesen werden.

er ist voll Schönheit und Pracht.

Die Stadt des großen Königs erfreut die ganze Welt.

4In den Palästen wissen es alle:

Gott selbst beschützt Jerusalem.

5Feindliche Könige verbündeten sich

und zogen gegen Jerusalem.

6Doch kaum erblickten sie die Stadt, blieben sie erschrocken stehen;

in panischer Angst ergriffen sie die Flucht.

7Ja, sie zitterten am ganzen Leib –

wie eine Frau, die in den Wehen liegt.

8Wie stolze Schiffe48,8 Wörtlich: Tarsis-Schiffe. – So wurden große Handelsschiffe bezeichnet, die in der Lage waren, die weite Strecke bis nach Tarsis (im heutigen Spanien) zu segeln., die im Sturm zerschellen,

so hast du sie vernichtet.

9Das alles haben wir früher nur gehört, doch nun erleben wir es selbst:

Gott ist der allmächtige Herr,

an Jerusalem sehen wir seine Größe.

Durch ihn wird die Stadt auf ewig bestehen.

10In deinem Tempel, o Gott,

denken wir über deine Güte nach.

11In jedem Land kennt man deinen Namen,

dein Ruhm reicht bis ans Ende der Welt.

Du sorgst für Recht und Gerechtigkeit,

12darum herrscht Freude auf dem Berg Zion.

Ja, was du beschließt, das ist gerecht,

darum jubelt man dir in den Städten Judas zu.

13Wandert um den Berg Zion,

geht rings um die Stadt und zählt ihre Festungstürme!

14Bestaunt die unbezwingbaren Mauern und Paläste!

Dann könnt ihr der nächsten Generation erzählen:

15»So ist Gott! Er ist unser Herr für immer und ewig;

allezeit wird er uns führen48,15 So nach vielen hebräischen Handschriften und der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: bis zum Tode wird er uns führen.