Masalimo 46 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 46:1-11

Salimo 46

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.

1Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,

thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.

2Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,

ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,

3ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,

ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.

4Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,

malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.

5Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;

Mulungu adzawuthandiza mmawa.

6Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;

Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.

7Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

8Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,

chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.

9Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;

Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;

amatentha zishango ndi moto.

10Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;

ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;

ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”

11Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,

Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.

New Russian Translation

Псалтирь 46:1-10

Псалом 46

1Дирижеру хора. Псалом потомков Кораха.

2Рукоплещите, все народы,

вознесите Богу крик радости.

3Как грозен Господь Всевышний46:3 Евр.: «ЙГВГ Эльон».,

великий Царь над всей землей!

4Он покорил нам народы,

бросил нам под ноги племена.

5Он избрал нам наследие –

гордость Иакова, которого Он возлюбил. Пауза

6Бог вознесся под крики радости;

Господь вознесся под звуки рогов.

7Пойте Богу хвалу, пойте!

Пойте хвалу нашему Царю, пойте!

8Бог – Царь над всей землей;

пойте Ему искусный псалом46:8 Евр.: «маскил». Это слово можно означать «псалом размышления/наставления» или «мастерски написанные стихи»..

9Бог царит над народами;

Бог восседает на святом престоле Своем.

10Собираются вожди народов,

вместе с народом Авраамова Бога,

ведь земные правители46:10 Букв.: «щиты». принадлежат Богу;

Он высоко превознесся.