Masalimo 41 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 41:1-13

Salimo 41

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;

Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.

2Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;

Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko

ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.

3Yehova adzamuthandiza pamene akudwala

ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

4Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;

chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”

5Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,

“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”

6Pamene wina abwera kudzandiona,

amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;

kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.

7Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,

iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,

8“Matenda owopsa amugwira;

sadzaukapo pamalo pamene wagona.”

9Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,

iye amene amadya pamodzi ndi ine

watukula chidendene chake kulimbana nane.

10Koma Yehova mundichititre chifundo,

dzutseni kuti ndiwabwezere.

11Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,

pakuti mdani wanga sandigonjetsa.

12Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga

ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.

13Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

Ameni ndi Ameni.

New International Reader’s Version

Psalm 41:1-13

Psalm 41

For the director of music. A psalm of David.

1Blessed are those who care about weak people.

When they are in trouble, the Lord saves them.

2The Lord guards them and keeps them alive.

They are counted among those who are blessed in the land.

The Lord won’t hand them over to the wishes of their enemies.

3The Lord will take care of them when they are lying sick in bed.

He will make them well again.

4I said, “Lord, have mercy on me.

Heal me, because I have sinned against you.”

5My enemies are saying bad things about me.

They say, “When will he die and his name be forgotten?”

6When one of them comes to see me,

he says things that aren’t true.

At the same time, he thinks up lies to tell against me.

Then he goes out and spreads those lies around.

7All my enemies whisper to each other about me.

They want something terrible to happen to me.

8They say, “He is sick and will die very soon.

He will never get up from his bed again.”

9Even my close friend, someone I trusted, has failed me.

I even shared my bread with him.

10But Lord, may you have mercy on me.

Make me well, so I can pay them back.

11Then I will know that you are pleased with me,

because my enemies haven’t won the battle over me.

12You will take good care of me because I’ve been honest.

You will let me be with you forever.

13Give praise to the Lord, the God of Israel,

for ever and ever.

Amen and Amen.