Masalimo 41 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 41:1-13

Salimo 41

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;

Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.

2Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;

Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko

ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.

3Yehova adzamuthandiza pamene akudwala

ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

4Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;

chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”

5Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,

“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”

6Pamene wina abwera kudzandiona,

amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;

kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.

7Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,

iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,

8“Matenda owopsa amugwira;

sadzaukapo pamalo pamene wagona.”

9Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,

iye amene amadya pamodzi ndi ine

watukula chidendene chake kulimbana nane.

10Koma Yehova mundichititre chifundo,

dzutseni kuti ndiwabwezere.

11Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,

pakuti mdani wanga sandigonjetsa.

12Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga

ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.

13Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

Ameni ndi Ameni.

Hoffnung für Alle

Psalm 41:1-14

Vom Tod gezeichnet, von Freunden verlassen

1Ein Lied von David.

2Glücklich ist, wer sich für die Schwachen einsetzt!

Wenn ihn ein Unglück trifft, hilft der Herr ihm wieder heraus.

3Der Herr wird ihn beschützen und am Leben erhalten;

im ganzen Land wird man von seinem Glück erzählen.

Gott überlässt ihn nicht der Willkür seiner Feinde.

4Und wenn er auf dem Krankenbett liegt,

steht der Herr ihm zur Seite und hilft ihm wieder auf.

5Deshalb bete ich zu dir: »Herr, ich habe gegen dich gesündigt,

aber sei mir gnädig und mach mich wieder gesund!«

6Meine Feinde wünschen mir Böses und fragen hämisch:

»Wann ist er endlich tot? Niemand soll mehr an ihn denken!«

7Wenn mich einer von ihnen besucht,

heuchelt er Mitgefühl.

In Wirklichkeit sucht er nur Stoff für seine Verleumdungen.

Kaum ist er fort, verbreitet er seine Gerüchte über mich.

8Alle, die mich hassen, tun sich zusammen

und tuscheln hinter meinem Rücken.

Sie planen Böses gegen mich und verfluchen mich.

9»Die Krankheit soll ihn auffressen!«, sagen sie.

»Wer so daniederliegt, steht nicht wieder auf!«

10Sogar mein engster Freund, mit dem ich mein Brot teilte

und dem ich vertraute, tritt mich nun mit Füßen.

11Du aber, Herr, sei mir gnädig und richte mich wieder auf,

damit ich mit meinen Feinden abrechnen kann!

12Du lässt nicht zu, dass sie über mich triumphieren;

daran erkenne ich, dass du mich liebst.

13Du hältst zu mir, weil ich unschuldig bin.

Für immer darf ich in deiner Nähe bleiben.

14Gepriesen sei der Herr, der Gott Israels,

von jetzt an bis in alle Ewigkeit!

Amen, so soll es sein!