Masalimo 40 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 40:1-17

Salimo 40

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mofatsa ndinadikira Yehova

Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.

2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,

mʼthope ndi mʼchithaphwi;

Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe

ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.

3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,

nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.

Ambiri adzaona,

nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.

4Ndi wodala munthu

amakhulupirira Yehova;

amene sayembekezera kwa odzikuza,

kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.

5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,

ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.

Zinthu zimene munazikonzera ife

palibe amene angathe kukuwerengerani.

Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,

zidzakhala zambiri kuzifotokoza.

6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,

koma makutu anga mwawatsekula;

zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo

Inu simunazipemphe.

7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.

Mʼbuku mwalembedwa za ine.

8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;

lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”

9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;

sinditseka milomo yanga

monga mukudziwa Inu Yehova.

10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;

ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.

Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu

pa msonkhano waukulu.

11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;

chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.

12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;

machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.

Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,

ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.

13Pulumutseni Yehova;

Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.

14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga

achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;

onse amene amakhumba chiwonongeko changa

abwezedwe mwamanyazi.

15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”

abwerere akuchita manyazi.

16Koma iwo amene amafunafuna Inu

akondwere ndi kusangalala mwa Inu;

iwo amene amakonda chipulumutso chanu

nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”

17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;

Ambuye andiganizire.

Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;

Inu Mulungu wanga, musachedwe.

Hoffnung für Alle

Psalm 40:1-18

Echter Gottesdienst

1Ein Lied von David.

2Voll Zuversicht hoffte ich auf den Herrn,

und er wandte sich mir zu und hörte meinen Hilfeschrei.

3Ich war in eine verzweifelte Lage geraten –

wie jemand, der bis zum Hals

in einer Grube voll Schlamm und Kot steckt!

Aber er hat mich herausgezogen und auf festen Boden gestellt.

Jetzt haben meine Füße wieder sicheren Halt.

4Er gab mir ein neues Lied in meinen Mund,

einen Lobgesang für unseren Gott.

Das werden viele Leute hören, sie werden den Herrn wieder achten

und ihm ganz neu vertrauen.

5Glücklich ist, wer sein Vertrauen auf den Herrn setzt

und sich nicht mit den Überheblichen und den Lügnern einlässt!

6Herr, mein Gott, du bist einzigartig!

Du hast so viele Wunder getan, alles hast du sorgfältig geplant!

Wollte ich das schildern und beschreiben –

niemals käme ich zum Ende!

7Dir geht es nicht um Schlachtopfer und andere Gaben;

du verlangst keine Brandopfer und Sündopfer von mir.

Sondern offene Ohren hast du mir gegeben,

um auf dich zu hören und dir zu gehorchen.

8Deshalb antworte ich: »Herr, hier bin ich!

Was im Buch des Gesetzes steht, das gilt mir.40,8 Oder: Im Buch des Gesetzes ist von mir geschrieben.

9Ich will gerne deinen Willen tun, mein Gott,

dein Gesetz ist mir ins Herz geschrieben.«

10Vor der ganzen Gemeinde erzähle ich voll Freude,

wie gerecht du bist und handelst.

Herr, du weißt: Nichts kann mich abhalten, davon zu reden!

11Nie will ich verschweigen, dass du für Recht sorgst.

Vor der ganzen Gemeinde rede ich von deiner Treue und Hilfe;

ich erzähle, wie ich deine große Liebe erfahren habe.

12Herr, du wirst mir niemals dein Erbarmen versagen,

deine Liebe und Treue werden mich stets bewahren.

13Unlösbare Schwierigkeiten türmen sich vor mir auf.

Meine Verfehlungen haben mich eingeholt,

und die Folgen sind nicht mehr zu überblicken.

Jeder Mut hat mich verlassen.

14Herr, ich bitte dich: Rette mich,

komm mir schnell zu Hilfe!

15Wer mir nach dem Leben trachtet,

der soll scheitern und öffentlich bloßgestellt werden.

Wer sich über mein Unglück hämisch freut,

den jage mit Schimpf und Schande davon!

16Alle, die schadenfroh lästern: »Haha, das geschieht dir recht!«,

sollen vor Schreck erstarren über ihre selbst verschuldete Schande!

17Aber alle, die nach dir fragen,

sollen vor Freude jubeln!

Wer dich als Retter kennt und liebt,

soll immer wieder rufen: »Groß ist der Herr

18Ich bin hilflos und ganz auf dich angewiesen;

Herr, sorge für mich, denn du bist mein Helfer und Befreier!

Mein Gott, zögere nicht länger!