Salimo 40
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.
1Mofatsa ndinadikira Yehova
Iye anatembenukira kwa ine ndipo anamva kulira kwanga.
2Ananditulutsa mʼdzenje lachitayiko,
mʼthope ndi mʼchithaphwi;
Iye anakhazikitsa mapazi anga pa thanthwe
ndipo anandipatsa malo oyimapo olimba.
3Iye anayika nyimbo yatsopano mʼkamwa mwanga,
nyimbo yamatamando kwa Mulungu wanga.
Ambiri adzaona,
nadzaopa ndipo adzakhulupirira Yehova.
4Ndi wodala munthu
amakhulupirira Yehova;
amene sayembekezera kwa odzikuza,
kapena kwa amene amatembenukira kwa milungu yabodza.
5Zambiri, Yehova Mulungu wanga,
ndi zodabwitsa zimene Inu mwachita.
Zinthu zimene munazikonzera ife
palibe amene angathe kukuwerengerani.
Nditati ndiyankhule ndi kufotokozera,
zidzakhala zambiri kuzifotokoza.
6Nsembe ndi zopereka Inu simuzifuna,
koma makutu anga mwawatsekula;
zopereka zopsereza ndi zopereka chifukwa cha tchimo
Inu simunazipemphe.
7Kotero ndinati, “Ndili pano, ndabwera.
Mʼbuku mwalembedwa za ine.
8Ndikufuna kuchita chifuniro chanu, Inu Mulungu wanga;
lamulo lanu lili mu mtima mwanga.”
9Ndikulalikira uthenga wa chilungamo chanu mu msonkhano waukulu;
sinditseka milomo yanga
monga mukudziwa Inu Yehova.
10Sindibisa chilungamo chanu mu mtima mwanga;
ndinayankhula za kukhulupirika kwanu ndi chipulumutso chanu.
Ine sindiphimba chikondi chanu ndi choonadi chanu
pa msonkhano waukulu.
11Musandichotsere chifundo chanu Yehova;
chikondi chanu ndi choonadi chanu zinditeteze nthawi zonse.
12Pakuti mavuto osawerengeka andizungulira;
machimo anga andigonjetsa, ndipo sindingathe kuona.
Alipo ambiri kuposa tsitsi la mʼmutu mwanga,
ndipo mtima wanga ukufowoka mʼkati mwanga.
13Pulumutseni Yehova;
Bwerani msanga Yehova kudzandithandiza.
14Onse amene akufunafuna kuchotsa moyo wanga
achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa;
onse amene amakhumba chiwonongeko changa
abwezedwe mwamanyazi.
15Iwo amene amanena kwa ine kuti, “Hee! Hee!”
abwerere akuchita manyazi.
16Koma iwo amene amafunafuna Inu
akondwere ndi kusangalala mwa Inu;
iwo amene amakonda chipulumutso chanu
nthawi zonse anene kuti, “Yehova akwezeke!”
17Komabe Ine ndine wosauka ndi wosowa;
Ambuye andiganizire.
Inu ndinu thandizo langa ndi wondiwombola wanga;
Inu Mulungu wanga, musachedwe.
Salmo 40
40:13-17 – Sal 70:1-5
Al director musical. Salmo de David.
1Puse en el Señor toda mi esperanza;
él se inclinó hacia mí y escuchó mi clamor.
2Me sacó de la fosa de la muerte,
del lodo y del pantano;
puso mis pies sobre una roca,
y me plantó en terreno firme.
3Puso en mis labios un cántico nuevo,
un himno de alabanza a nuestro Dios.
Al ver esto, muchos tuvieron miedo
y pusieron su confianza en el Señor.
4Dichoso el que pone su confianza en el Señor
y no recurre a los idólatras
ni a los que adoran dioses falsos.
5Muchas son, Señor mi Dios,
las maravillas que tú has hecho.
No es posible enumerar
tus bondades en favor nuestro.
Si quisiera anunciarlas y proclamarlas,
serían más de lo que puedo contar.
6A ti no te complacen sacrificios ni ofrendas,
pero has abierto mis oídos para oírte;
tú no has pedido holocaustos
ni sacrificios por el pecado.
7Por eso dije: «Aquí me tienes
—como el libro dice de mí—.
8Me agrada, Dios mío, hacer tu voluntad;
tu ley la llevo dentro de mí».
9En medio de la gran asamblea
he dado a conocer tu justicia.
Tú bien sabes, Señor,
que no he sellado mis labios.
10No escondo tu justicia en mi corazón,
sino que proclamo tu fidelidad y tu salvación.
No oculto en la gran asamblea
tu gran amor y tu verdad.
11No me niegues, Señor, tu misericordia;
que siempre me protejan tu amor y tu verdad.
12Muchos males me han rodeado;
tantos son que no puedo contarlos.
Me han alcanzado mis iniquidades,
y ya ni puedo ver.
Son más que los cabellos de mi cabeza,
y mi corazón desfallece.
13Por favor, Señor, ¡ven a librarme!
¡Ven pronto, Señor, en mi auxilio!
14Sean confundidos y avergonzados
todos los que tratan de matarme;
huyan derrotados
todos los que procuran mi mal;
15que la vergüenza de su derrota
humille a los que se burlan de mí.
16Pero que todos los que te buscan
se alegren en ti y se regocijen;
que los que aman tu salvación digan siempre:
«¡Cuán grande es el Señor!»
17Y a mí, pobre y necesitado,
quiera el Señor tomarme en cuenta.
Tú eres mi socorro y mi libertador;
¡Dios mío, no tardes!