Masalimo 39 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 39:1-13

Salmo 39

Al director musical. Para Jedutún. Salmo de David.

1Me dije a mí mismo:

«Mientras esté ante gente malvada,

vigilaré mi conducta,

me abstendré de pecar con la lengua,

me pondré una mordaza en la boca».

2Así que guardé silencio, me mantuve callado.

¡Ni aun lo bueno salía de mi boca!

Pero mi angustia iba en aumento;

3¡el corazón me ardía en el pecho!

Al meditar en esto, el fuego se inflamó

y tuve que decir:

4«Hazme saber, Señor, el límite de mis días,

y el tiempo que me queda por vivir;

hazme saber lo efímero que soy.

5Muy breve es la vida que me has dado;

ante ti, mis años no son nada.

¡Un soplo nada más es el mortal! Selah

6Es un suspiro que se pierde entre las sombras.

Ilusorias son las riquezas que amontona,39:6 Ilusorias … que amontona (lectura probable); En vano hace ruido y amontona (TM).

pues no sabe quién se quedará con ellas.

7»Y ahora, Señor, ¿qué esperanza me queda?

¡Mi esperanza he puesto en ti!

8Líbrame de todas mis transgresiones.

Que los necios no se burlen de mí.

9»He guardado silencio; no he abierto la boca,

pues tú eres quien actúa.

10Ya no me castigues,

que los golpes de tu mano me aniquilan.

11Tú reprendes a los mortales,

los castigas por su iniquidad;

como polilla, acabas con sus placeres.

¡Un soplo nada más es el mortal! Selah

12»Señor, escucha mi oración,

atiende mi clamor;

no cierres tus oídos a mi llanto.

Ante ti soy un extraño,

un peregrino, como todos mis antepasados.

13No me mires con enojo, y volveré a alegrarme

antes que me muera y deje de existir».