Masalimo 38 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 38:1-22

Salimo 38

Salimo la Davide. Kupempha.

1Yehova musandidzudzule mutapsa mtima

kapena kundilanga muli ndi ukali.

2Pakuti mivi yanu yandilasa,

ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.

3Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;

mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

4Kulakwa kwanga kwandipsinja

ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.

5Mabala anga akuwola ndipo akununkha

chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.

6Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;

tsiku lonse ndimangolira.

7Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,

mulibe thanzi mʼthupi langa.

8Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;

ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.

9Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,

kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.

10Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;

ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

11Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;

anansi anga akhala kutali nane.

12Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,

oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;

tsiku lonse amakonza zachinyengo.

13Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,

monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;

14Ndakhala ngati munthu amene samva,

amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.

15Ndikudikira Inu Yehova;

mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.

16Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere

kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”

17Pakuti ndili pafupi kugwa,

ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.

18Ndikuvomereza mphulupulu zanga;

ndipo ndavutika ndi tchimo langa.

19Ambiri ndi adani anga amphamvu;

amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.

20Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino

amandinyoza pamene nditsatira zabwino.

21Inu Yehova, musanditaye;

musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.

22Bwerani msanga kudzandithandiza,

Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.

New International Reader’s Version

Psalm 38:1-22

Psalm 38

A psalm of David. A prayer.

1Lord, don’t correct me when you are angry.

Don’t punish me when you are burning with anger.

2You have wounded me with your arrows.

You have struck me with your hand.

3Because of your anger, my whole body is sick.

Because of my sin, I’m not healthy.

4My guilt has become too much for me.

It is a load too heavy to carry.

5My wounds are ugly. They stink.

I’ve been foolish. I have sinned.

6I am bent over. I’ve been brought very low.

All day long I go around weeping.

7My back is filled with burning pain.

My whole body is sick.

8I am weak and feel as if I’ve been broken in pieces.

I groan because of the great pain in my heart.

9Lord, everything I really want is clearly known to you.

You always hear me when I sigh.

10My heart pounds, and my strength is gone.

My eyes can hardly see.

11My friends and companions avoid me because of my wounds.

My neighbors stay far away from me.

12Those who are trying to kill me set their traps.

Those who want to harm me talk about destroying me.

All day long they make their plans and tell their lies.

13Like a deaf person, I can’t hear.

Like someone who can’t speak, I can’t say a word.

14I’m like someone who doesn’t hear.

I’m like someone whose mouth can’t make any reply.

15Lord, I wait for you to help me.

Lord my God, I know you will answer.

16I said, “Don’t let my enemies have the joy of seeing me fall.

Don’t let them brag when my feet slip.”

17I am about to fall.

My pain never leaves me.

18I admit that I have done wrong.

I am troubled by my sin.

19Though I have done nothing to cause it, many people have become my enemies.

They hate me without any reason.

20They pay me back with evil, even though I was good to them.

They bring charges against me, though I try only to do what is good.

21Lord, don’t desert me.

My God, don’t be far away from me.

22Lord my Savior,

come quickly to help me.