Masalimo 39 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”

New International Reader’s Version

Psalm 39:1-13

Psalm 39

For the director of music. For Jeduthun. A psalm of David.

1I said, “I will be careful about how I live.

I will not sin by what I say.

I will keep my mouth closed

when I am near sinful people.”

2So I was completely silent.

I didn’t even say anything good.

But the pain inside me grew worse.

3My heart was deeply troubled.

As I thought about what was happening to me,

I became even more troubled.

Then I spoke out.

4I said, “Lord, show me when my life will end.

Show me how many days I have left.

Tell me how short my life will be.

5You have given me only a few days to live.

My whole life doesn’t seem like anything to you.

No one lasts any longer than a breath.

This is true even for those who feel secure.

6People are only shadows as they go here and there.

They rush around, but it doesn’t mean anything.

They pile up wealth, but they don’t know who will finally get it.

7“Lord, what can I look forward to now?

You are the only hope I have.

8Save me from all the wrong things I’ve done.

Don’t let foolish people make fun of me.

9I keep silent. I don’t open my mouth.

You are the one who has caused all this to happen.

10Please stop beating me.

I’m about to die from the blows of your hand.

11You correct and punish people for their sin.

Then, just as a moth eats cloth, you destroy their wealth.

No one lasts any longer than a breath.

12Lord, hear my prayer.

Listen to my cry for help.

Pay attention to my weeping.

I’m like an outsider in your home.

I’m just a stranger, like all my family who lived before me.

13Leave me alone.

Let me enjoy life again before I die.”