Masalimo 35 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.

Nueva Versión Internacional

Salmo 35:1-28

Salmo 35

Salmo de David.

1Ataca, Señor, a los que me atacan;

combate a los que me combaten.

2Toma tu adarga, tu escudo,

y acude en mi ayuda.

3Empuña la lanza y el hacha,

y haz frente a35:3 el hacha, y haz frente a (lectura probable); cierra contra (TM). los que me persiguen.

Quiero oírte decir:

«Yo soy tu salvación».

4Queden confundidos y avergonzados

los que procuran matarme;

retrocedan humillados

los que traman mi ruina.

5Sean como la paja que se lleva el viento,

acosados por el ángel del Señor;

6sea su senda oscura y resbalosa,

perseguidos por el ángel del Señor.

7Ya que sin motivo me tendieron una trampa

y sin motivo cavaron una fosa para mí,

8que la ruina los tome por sorpresa;

que caigan en su propia trampa,

en la fosa que ellos mismos cavaron.

9Así mi alma se alegrará en el Señor

y se deleitará en su salvación.

10Así todo mi ser exclamará:

«¿Quién como tú, Señor?

Tú libras de los poderosos a los pobres;

a los pobres y necesitados libras

de aquellos que los explotan».

11Se presentan testigos despiadados

y me preguntan cosas que yo ignoro.

12Me devuelven mal por bien

y eso me duele en el alma;

13pues cuando ellos enfermaban

yo me vestía de luto,

me afligía y ayunaba.

¡Ay, si pudiera retractarme de mis oraciones!

14Me vestía yo de luto,

como por un amigo o un hermano.

Afligido, inclinaba la cabeza,

como si llorara por mi madre.

15Pero yo tropecé y ellos se alegraron

y a una se juntaron contra mí.

Asaltantes35:15 Asaltantes (lectura probable); Gente golpeada o extraña (TM). que yo no conocía;

me calumniaban sin cesar.

16Me atormentaban, se burlaban de mí35:16 Me … mí (LXX); Como un grupo impío de burlones (TM).

y contra mí rechinaban los dientes.

17¿Hasta cuándo, Señor, vas a tolerar esto?

Libra mi vida, mi única vida,

de los ataques de esos leones.

18Yo te daré gracias en la gran asamblea;

ante una multitud te alabaré.

19No dejes que de mí se burlen

mis enemigos traicioneros;

no dejes que guiñen el ojo

los que me odian sin motivo.

20Porque no vienen en son de paz,

sino que urden mentiras

contra la gente apacible del país.

21De mí se ríen a carcajadas y exclaman:

«¡Miren en lo que vino a parar!».

22Señor, tú has visto todo esto;

no te quedes callado.

¡Señor, no te alejes de mí!

23¡Despierta! ¡Levántate en mi defensa!

¡Defiéndeme, mi Dios y Señor!

24Júzgame según tu justicia, Señor mi Dios;

no dejes que se burlen de mí.

25No permitas que piensen:

«¡Así queríamos verlo!».

No permitas que digan:

«Nos lo hemos tragado vivo».

26Queden avergonzados y confundidos

todos los que se alegran de mi desgracia;

sean cubiertos de deshonra y vergüenza

todos los que se creen más que yo.

27Pero lancen voces de alegría y regocijo

los que quieren mi vindicación

y digan siempre: «Exaltado sea el Señor,

quien se deleita en el bienestar de su siervo».

28Con mi lengua proclamaré tu justicia

y todo el día te alabaré.