Salimo 32
Salimo la Davide. Malangizo.
1Ngodala munthu
amene zolakwa zake zakhululukidwa;
amene machimo ake aphimbidwa.
2Ngodala munthu
amene machimo ake Yehova sawawerengeranso pa iye
ndipo mu mzimu mwake mulibe chinyengo.
3Pamene ndinali chete,
mafupa anga anakalamba
chifukwa cha kubuwula kwanga tsiku lonse.
4Pakuti usana ndi usiku
dzanja lanu linandipsinja;
mphamvu zanga zinatha
monga nthawi yotentha yachilimwe.
Sela
5Kotero ine ndinavomereza tchimo langa kwa Inu,
sindinabise mphulupulu zanga.
Ndinati, “Ine ndidzawulula
zolakwa zanga kwa Yehova,
ndipo Inu munandikhululukira
mlandu wa machimo anga.”
Sela
6Choncho aliyense okhulupirika apemphere kwa Inuyo
pomwe mukupezeka;
ndithu pamene madzi amphamvu auka,
sadzamupeza.
7Inu ndi malo anga obisala;
muzinditeteza ku mavuto ndipo muzindizinga
ndi nyimbo zachipulumutso.
Sela
8Ndidzakulangiza ndi kukuphunzitsa njira imene udzayendamo;
ndidzakupatsa uphungu ndi kukuyangʼanira.
9Usakhale ngati kavalo kapena bulu,
zimene zilibe nzeru,
koma ziyenera kuwongoleredwa ndi zitsulo za mʼkamwa ndi pamutu,
ukapanda kutero sizibwera kwa iwe.
10Zowawa ndi zambiri za anthu oyipa
koma chikondi chosatha cha Yehova
chimamuzinga munthu amene amadalira Iye.
11Kondwerani mwa Yehova inu olungama;
imbani, inu nonse amene muli owongoka mtima!
第 32 篇
認罪與赦免
大衛的詩。
1過犯得赦免、罪惡被饒恕的人有福了!
2心裡沒有詭詐、
不被耶和華算為有罪的人有福了!
3我默然不語、拒絕認罪的時候,
就因整日哀歎而身心疲憊。
4你晝夜管教我,
我的精力耗盡,
如水在盛夏枯竭。(細拉)
5我向你承認自己的罪,
不再隱瞞自己的惡。
我說:「我要向耶和華認罪。」
你就赦免了我。(細拉)
6因此,趁著還能尋求你的時候,
凡敬虔的人都當向你禱告;
洪水氾濫時,就沒有機會了。
7你是我的藏身之所,
你保護我免遭危難,
用得勝的凱歌四面環繞我。(細拉)
8耶和華說:「我要教導你,
引領你走正路;
我要勸導你,看顧你。
9不要像無知的騾馬,
不用嚼環轡頭就不馴服。」
10惡人必多遭禍患,
耶和華的慈愛必環繞信靠祂的人。
11義人啊,
你們要靠耶和華歡喜快樂;
心地正直的人啊,
你們都要歡呼。