Masalimo 31 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.

New Serbian Translation

Псалми 31:1-24

Псалам 31

За хоровођу. Псалам Давидов.

1У теби је уточиште моје, Господе;

о, да се никад не постидим;

избави ме по својој праведности.

2Пригни ухо своје к мени,

брзо ме избави,

буди ми стена, уточиште,

јака тврђава за моје спасење.

3Ти си моја стена и тврђава,

ради свог имена води ме, усмеравај.

4Извуци ме из мреже коју ми поставише,

јер ти си моја тврђава.

5У твоје руке предајем свој дух,

откупи ме, Господе, верни Боже.

6Мрзим служитеље безвредних идола;

поуздајем се једино у Господа.

7Клицаћу и радоваћу се по твојој милости,

јер ти си видео моју муку;

ти си знао тескобу моје душе.

8Ниси ме дао у руке душманину,

него си ми ноге поставио на пространо место.

9Смилуј ми се, Господе, јер сам у невољи,

моје око од жалости копни,

вене моја душа и нутрина.

10Живот ми се троши у жалости,

у јецању одмичу године,

снага ме издаје због моје неправде,

и кости се моје распадају.

11Поруга постадох због свих својих душмана:

суседима терет, а знанцима страшило;

беже од мене кад ме виде на улици.

12Падох у заборав, као да сам умро,

постао сам као разбијени суд.

13Јер ја чујем клевете многих,

ужас ме је опколио одасвуд.

А они се удружују против мене,

кују заверу да ми живот узму.

14Али ја се у тебе уздам, Господе,

и кажем: „Ти си Бог мој.“

15Време је моје у руци твојој;

избави ме из руку душмана,

и од оних који ме прогоне.

16Нека лице твоје обасја слугу твога,

милошћу ме својом избави.

17Не дај да се постидим, Господе,

јер теби завапих;

нека се опаки постиде,

у Свету мртвих нек умукну.

18Нека умукну уста лажљива,

која против праведника говоре

обесно, охоло и презриво.

19Како је обилна доброта твоја,

коју чуваш за оне који те се боје;

исказујеш је пред потомцима људи,

онима што у теби уточиште нађу.

20Ти их скриваш у заклону свог лица,

од завера које људи кују,

заклањаш их под своју сеницу,

од језика који оптужују.

21Благословен био Господ,

јер ми исказа дивну милост своју,

кад сам био у граду под опсадом.

22Тада рекох узнемирен:

„Одбачен сам од твог погледа.“

Али ти си чуо глас мога преклињања,

када сам завапио к теби.

23Волите Господа, сви верни његови,

Господ чува оне који верују,

а охолима плаћа пуном мером.

24Будите јаки и храбра срца,

сви ви што се надате Господу!