Masalimo 30 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 30:1-12

Salimo 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

“Sindidzagwedezekanso.”

7Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa.”

11Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

New Serbian Translation

Псалми 30:1-12

Псалам 30

Псалам Давидов. Песма за посвећење храма.

1Узвисујем те, Господе, јер си ме подигао,

ниси дао да се душмани нада мном радују.

2Теби завапих, Господе, Боже мој,

и ти си ме исцелио.

3Господе, из Света мртвих ти си ме извео,

моју си душу спасао од раке.

4Запојте Господу, верни његови,

хвалите га, спомињите светост његову.

5Јер гнев његов траје за трен,

а читав живот милост његова.

Вече доноси плач,

а јутро клицање.

6У свом спокојству рекао сам себи:

„Никада ме ништа неће уздрмати.“

7Милошћу си ме својом, Господе,

учврстио као моћну гору;

кад си лице своје сакрио,

свега ме је страх обузео.

8К теби вапим, Господе,

од свога Бога тражим милост.

9„Каква корист од моје смрти,

ако сиђем у раку?

Хоће ли те прах прослављати?

Зар ће прах о твојој верности да прича?

10Почуј, Господе, смилуј ми се,

буди моја помоћ, о, Господе!“

11Мој си плач окренуо у коло,

скинуо си с мене рухо жалости,

и у рухо ме радости обукао.

12Зато те душа моја слави без престанка.

О, Господе, Боже мој, хвалићу те вечно!