Masalimo 30 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 30:1-12

Salimo 30

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba popereka Nyumba ya Mulungu.

1Ndidzakukwezani Yehova,

chifukwa mwanditulutsa kwakuya,

ndipo simunalole kuti adani anga akondwere pa ine.

2Inu Yehova Mulungu wanga ndinapempha kwa Inu thandizo

ndipo Inu munandichiritsa.

3Inu Yehova, munanditulutsa ku manda,

munandisunga kuti ndisatsalire mʼdzenje.

4Imbirani Yehova inu anthu ake okhulupirika;

tamandani dzina lake loyera.

5Pakuti mkwiyo wake umakhala kwa kanthawi

koma kukoma mtima kwake ndi kwa moyo wonse;

utha kuchezera kulira usiku wonse,

koma chimwemwe chimabwera mmawa.

6Pamene ndinaona kuti ndili otetezedwa ndinati,

“Sindidzagwedezekanso.”

7Inu Yehova, pamene munandikomera mtima,

munachititsa phiri langa kuyima chilili;

koma pamene munabisa nkhope yanu,

ndinataya mtima.

8Kwa Inu Yehova ndinayitana;

kwa Ambuye ndinapempha chifundo;

9“Kodi pali phindu lanji powonongeka kwanga

ngati nditsikira ku dzenje?

Kodi fumbi lidzakutamandani Inu?

Kodi lidzalengeza za kukhulupirika kwanu?

10Imvani Yehova ndipo mundichitire chifundo;

Yehova mukhale thandizo langa.”

11Inu munasandutsa kulira kwanga kukhala kuvina;

munachotsa chiguduli changa ndi kundiveka ndi chimwemwe,

12kuti mtima wanga uthe kuyimbira Inu usakhale chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzapereka kwa Inu mayamiko kwamuyaya.

Hoffnung für Alle

Psalm 30:1-13

Vor dem sicheren Tod errettet

1Ein Lied von David. Es wurde zur Einweihung des Tempels gesungen.

2Ich will dich preisen, Herr,

denn du hast mich aus der Tiefe heraufgezogen!

Du hast meinen Feinden keinen Grund gegeben,

sich über mein Unglück zu freuen.

3Herr, mein Gott! Zu dir schrie ich um Hilfe,

und du hast mich geheilt.

4Ich war schon mehr tot als lebendig,

doch du hast mich dem sicheren Tod entrissen

und mir das Leben neu geschenkt.

5Singt dem Herrn eure Lieder, alle, die ihr treu zu ihm steht!

Lobt ihn und bezeugt: Er ist der heilige Gott!

6Nur einen Augenblick streift uns sein Zorn,

aber ein Leben lang währt seine Güte.

Wenn wir am Abend noch weinen und traurig sind,

so können wir am Morgen doch wieder vor Freude jubeln.

7Als es mir gut ging, dachte ich selbstzufrieden:

»Was kann mir schon passieren?«

8Denn du, Herr, hattest mir Macht und Sicherheit verliehen,

alles hatte ich deiner Güte zu verdanken.

Dann aber hast du dich von mir abgewandt,

und mich packte das Entsetzen.

9Ich flehte um Erbarmen

und schrie zu dir:

10»Was hast du davon, wenn ich jetzt sterbe

und man mich zu Grabe trägt?

Kann ein Mensch dich noch loben, wenn er zu Staub zerfallen ist?

Kann ein Toter noch von deiner Treue erzählen?

11Höre mich, Herr, und sei mir gnädig!

Herr, komm du mir zu Hilfe!«

12Du hast mein Klagelied in einen Freudentanz verwandelt.

Du hast mir die Trauerkleider ausgezogen

und mich mit einem Festgewand bekleidet.

13Nun kann ich dich mit meinen Liedern loben,

nie will ich verschweigen, was du für mich getan hast.

Immer und ewig will ich dir danken, Herr, mein Gott!