Masalimo 29 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

1Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

3Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

4Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

5Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

6Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

7Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

8Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

9Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

11Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

Hoffnung für Alle

Psalm 29:1-11

Gottes Stimme – herrlich und furchtbar zugleich!

1Ein Lied von David.

Lobt den Herrn, ihr mächtigen Engel29,1 Wörtlich: ihr Gottessöhne. – Vgl. »Gottessöhne« in den Sacherklärungen.,

preist seine Hoheit und Macht!

2Ehrt seinen wunderbaren Namen,

werft euch vor ihm nieder in seiner herrlichen Pracht29,2 Oder: werft euch vor ihm nieder in heiligem Schmuck!!

3Die Stimme des Herrn erschallt über die Meere,

der erhabene Gott lässt den Donner grollen.

Er ist der Herr, der über den Weiten des Ozeans thront.

4Wie gewaltig ist seine Stimme,

wie herrlich und furchtbar zugleich!

5Sie spaltet mächtige Bäume,

ja, der Herr zersplittert die stärksten Zedern.

6Das Libanongebirge lässt er wie ein Kalb hüpfen,

der Berg Hermon29,6 Wörtlich: Sirjon. – Ein anderer Name für den Berg Hermon. Vgl. 5. Mose 3,9. springt wie ein junger Stier.

7Die Stimme des Herrn lässt Blitze zucken,

8sie erschüttert die Wüste,

ja, die Wüste Kadesch bebt.

9Sein Donnergrollen lässt die Eichen schwanken29,9 Oder: lässt die Hirschkühe kalben.,

sein tosender Sturm reißt ganze Wälder kahl.

In seinem Tempel rufen alle: »Ihm gebührt die Ehre!«

10Der Herr thront über den Fluten,

als König herrscht er für alle Zeit.

11Der Herr wird seinem Volk Kraft geben,

er wird es segnen und ihm Frieden schenken.