Masalimo 29 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 29:1-11

Salimo 29

Salimo la Davide.

1Perekani kwa Yehova, inu anthu amphamvu,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

2Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake,

pembedzani Yehova mwa kukongola kwa chiyero chake.

3Liwu la Yehova lili pamwamba pa madzi;

Mulungu waulemerero abangula,

Yehova abangula pamwamba pa madzi amphamvu.

4Liwu la Yehova ndi lamphamvu;

liwu la Yehova ndi laulemerero.

5Liwu la Yehova limathyola mikungudza;

Yehova amathyolathyola mikungudza ya ku Lebanoni.

6Iye amachititsa Lebanoni kulumphalumpha ngati mwana wangʼombe,

Siriyoni ngati mwana wa njati:

7Liwu la Yehova limakantha

ngati kungʼanima kwa mphenzi.

8Liwu la Yehova limagwedeza chipululu;

Yehova amagwedeza chipululu cha Kadesi.

9Liwu la Yehova limapindapinda mibawa

ndi kuyeretsa nkhalango.

Ndipo mʼNyumba mwake onse amafuwula kuti, “Ulemerero!”

10Yehova amakhala pamwamba pa madzi osefukira,

Yehova ndiye mfumu kwamuyaya.

11Yehova amapereka mphamvu kwa anthu ake;

Yehova amadalitsa anthu ake ndi mtendere.

New International Version – UK

Psalms 29:1-11

Psalm 29

A psalm of David.

1Ascribe to the Lord, you heavenly beings,

ascribe to the Lord glory and strength.

2Ascribe to the Lord the glory due to his name;

worship the Lord in the splendour of his29:2 Or Lord with the splendour of holiness.

3The voice of the Lord is over the waters;

the God of glory thunders,

the Lord thunders over the mighty waters.

4The voice of the Lord is powerful;

the voice of the Lord is majestic.

5The voice of the Lord breaks the cedars;

the Lord breaks in pieces the cedars of Lebanon.

6He makes Lebanon leap like a calf,

Sirion29:6 That is, Mount Hermon like a young wild ox.

7The voice of the Lord strikes

with flashes of lightning.

8The voice of the Lord shakes the desert;

the Lord shakes the Desert of Kadesh.

9The voice of the Lord twists the oaks29:9 Or Lord makes the deer give birth

and strips the forests bare.

And in his temple all cry, ‘Glory!’

10The Lord sits enthroned over the flood;

the Lord is enthroned as King for ever.

11The Lord gives strength to his people;

the Lord blesses his people with peace.