Masalimo 28 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 28:1-9

Salimo 28

Salimo la Davide.

1Kwa Inu ine ndiyitana, Yehova ndinu Thanthwe langa;

musakhale osamva kwa ine.

Pakuti mukapitirira kukhala chete,

ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

2Imvani kupempha chifundo kwanga

pomwe ndikuyitana kwa Inu kuti mundithandize,

pomwe ndikukweza manja anga

kuloza ku malo anu oyeretsetsa.

3Musandikokere kutali pamodzi ndi anthu oyipa,

pamodzi ndi iwo amene amachita zoyipa,

amene amayankhula mwachikondi ndi anzawo

koma akusunga chiwembu mʼmitima mwawo.

4Muwabwezere chifukwa cha zochita zawo

ndi ntchito zawo zoyipa;

abwezereni chifuwa cha zimene manja awo achita

ndipo mubweretse pa iwo zimene zowayenera.

5Popeza iwowo sakhudzidwa ndi ntchito za Yehova,

ndi zimene manja ake anazichita,

Iye adzawakhadzula

ndipo sadzawathandizanso.

6Matamando apite kwa Yehova,

popeza Iye wamva kupempha chifundo kwanga.

7Yehova ndiye mphamvu yanga ndi chishango changa;

mtima wanga umadalira Iye, ndipo Ine ndathandizidwa.

Mtima wanga umalumphalumpha chifukwa cha chimwemwe

ndipo ndidzayamika Iye mʼnyimbo.

8Yehova ndi mphamvu ya anthu ake,

linga la chipulumutso kwa wodzozedwa wake.

9Pulumutsani anthu anu ndipo mudalitse cholowa chanu;

mukhale mʼbusa wawo ndipo muwakweze kwamuyaya.

Persian Contemporary Bible

مزامير 28:1-9

طلب كمک از خداوند

1ای خداوند، نزد تو فرياد برمی‌آورم؛ ای تكيه‌گاه من، دعايم را بشنو! اگر دعای مرا نشنوی به سرنوشت كسانی دچار خواهم شد كه الان در قبرها خفته‌اند. 2وقتی دستهای خود را به سوی تو بلند می‌كنم و با گريه و زاری از تو كمک می‌طلبم، مرا اجابت فرما. 3مرا جزو بدكاران و شروران محسوب نكن. آنها در ظاهر با همسايگان خود سخنان دوستانه می‌گويند، اما در دل خود قصد اذيت و آزارشان را دارند. 4آنها را برای آنچه كه كرده‌اند مجازات كن! برای كارهای زشتی كه مرتكب شده‌اند، مزدشان را كف دستشان بگذار! 5آنها را چنان بر زمين بكوب كه ديگر نتوانند بلند شوند، زيرا به آفرينش و كارهای دست تو اهميت نمی‌دهند.

6خدا را سپاس باد! او فرياد مرا كه از او كمک طلبيدم، شنيده است. 7خداوند قوت و سپر من است. از صميم قلب بر او توكل كردم و او مرا ياری كرد. از اين رو، دلم شاد است و با سرود از او تشكر می‌نمايم.

8خداوند قوم خود را حفظ می‌كند و از پادشاه برگزيدهٔ خويش حمايت می‌نمايد و او را نجات می‌بخشد. 9ای خداوند، قوم برگزيدهٔ خود را نجات ده و عزيزان خود را بركت عنايت فرما. تو شبان آنها باش و تا ابد از ايشان نگهداری كن!