Masalimo 22 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 22:1-31

Salimo 22

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa “Mbawala yayikazi ya Mmawa.” Salimo la Davide.

1Mulungu wanga, Mulungu wanga, nʼchifukwa chiyani mwandisiya?

Chifuwa chiyani simukundithandiza ndi pangʼono pomwe?

Nʼchifukwa chiyani simukumva mawu a kudandaula kwanga?

2Inu Mulungu wanga, ine ndimalira masana, koma simuyankha,

usikunso, ndipo sindikhala chete.

3Inu ndinu Woyera, wokhala pa mpando waufumu;

ndinu matamando a Israeli.

4Pa inu makolo athu anadalira;

iwo anadalira ndipo Inu munawapulumutsa.

5Analirira kwa inu ndipo munawapulumutsa.

Iwo anakhulupirira Inu ndipo simunawakhumudwitse.

6Koma ine ndine nyongolotsi osati munthu,

wosekedwa ndi wonyozedwa ndi anthu onse.

7Onse amene amandiona amandiseka;

amandiyankhulira mawu achipongwe akupukusa mitu yawo kunena kuti

8“Iyeyu amadalira Yehova,

musiyeni Yehovayo amulanditse.

Musiyeni Yehova amupulumutse

popeza amakondwera mwa Yehovayo.”

9Komabe Inu ndinu amene munandibadwitsa, munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga.

Munachititsa kuti ndizikudalirani

ngakhale pa nthawi imene ndinkayamwa.

10Chibadwire ine ndinaperekedwa kwa Inu;

kuchokera mʼmimba mwa amayi anga Inu mwakhala muli Mulungu wanga.

11Musakhale kutali ndi ine,

pakuti mavuto ali pafupi

ndipo palibe wina wondipulumutsa.

12Ngʼombe zazimuna zandizungulira;

ngʼombe zazimuna zamphamvu za ku Basani zandizinga.

13Mikango yobangula pokadzula nyama,

yatsekula kwambiri pakamwa pawo kulimbana nane.

14Ine ndatayika pansi ngati madzi

ndipo mafupa anga onse achoka mʼmalo mwake.

Mtima wanga wasanduka phula;

wasungunuka mʼkati mwanga.

15Mphamvu zanga zauma ngati phale,

ndipo lilime langa lamamatira ku nsagwada;

mwandigoneka mʼfumbi la imfa.

16Agalu andizungulira;

gulu la anthu oyipa landizinga.

Alasa manja ndi mapazi anga.

17Ine nditha kuwerenga mafupa anga onse;

anthu amandiyangʼanitsitsa ndi kundidzuma.

18Iwo agawana zovala zanga pakati pawo

ndi kuchita maere pa zovala zangazo.

19Koma Inu Yehova, musakhale kutali;

Inu mphamvu yanga, bwerani msanga kuti mudzandithandize.

20Pulumutsani moyo wanga ku lupanga,

moyo wanga wopambanawu ku mphamvu ya agalu.

21Ndilanditseni mʼkamwa mwa mikango;

pulumutseni ku nyanga za njati.

22Ine ndidzalengeza dzina lanu kwa abale anga;

ndidzakutamandani mu msonkhano.

23Inu amene mumaopa Yehova mutamandeni!

Inu zidzukulu zonse za Yakobo, mulemekezeni!

Muopeni mwaulemu, inu zidzukulu zonse za Israeli!

24Pakuti Iye sanapeputse kapena kunyoza

kuvutika kwa wosautsidwayo;

Iye sanabise nkhope yake kwa iye.

Koma anamvera kulira kwake kofuna thandizo.

25Ndidzakutamandani pa msonkhano waukulu chifukwa cha zimene mwandichitira.

Ndidzakwaniritsa lonjezo langa pamaso pa amene amaopa Inu.

26Osauka adzadya ndipo adzakhuta;

iwo amene amafunafuna Yehova adzamutamanda.

Mitima yanu ikhale ndi moyo mpaka muyaya!

27Malekezero onse a dziko lapansi

adzakumbukira Yehova ndi kutembenukira kwa Iye,

ndipo mabanja a mitundu ya anthu

adzawerama pamaso pake,

28pakuti ulamuliro ndi wake wa Yehova

ndipo Iye amalamulira anthu a mitundu yonse.

29Anthu olemera onse a dziko lapansi adzachita phwando ndi kulambira;

onse amene amapita ku fumbi adzagwada pamaso pake;

iwo amene sangathe kudzisunga okha ndi moyo.

30Zidzukulu zamʼtsogolo zidzamutumikira Iye;

mibado ya mʼtsogolo idzawuzidwa za Ambuye.

31Iwo adzalengeza za chilungamo chake

kwa anthu amene pano sanabadwe

pakuti Iye wachita zimenezi.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 22:1-31

第 22 篇

苦难中的呼求和感恩

大卫的诗,交给乐长,调用“朝鹿”。

1我的上帝,我的上帝,

你为何离弃我?

为何迟迟不来救我,

不听我的哀号呢?

2我的上帝啊,

我日夜不停地呼求,

你却没有回应。

3然而,你是圣洁的,

你的宝座设立在以色列人的颂赞之上。

4我们的祖先信靠你,

他们信靠你,

你就拯救他们。

5他们向你呼求,

就得到拯救;

他们信靠你,

就不会失望。

6但我好像不是人,只是一条虫,

受尽人的羞辱和藐视。

7看见我的人都讥笑我,

他们撇着嘴、摇着头说:

8“他信靠耶和华,

让耶和华救他吧!

既然耶和华喜悦他,

让耶和华拯救他吧!”

9耶和华啊,

是你使我从母腹中安然出生,

让我在母亲怀里便倚靠你。

10我一出生就被交托在你手中,

你从我出母胎就是我的上帝。

11求你不要远离我,

因为危难当头,无人帮我。

12我被许多仇敌围困,

他们像巴珊的公牛那样强壮。

13他们张口要吞噬我,

如同吼叫着撕食猎物的狮子。

14我的力量如水消逝,

我的骨头都脱了节,

我的心如蜡熔化。

15我的力量枯竭如焦土,

我的舌头发干紧贴上颚。

你把我放在死亡的尘土中。

16恶人包围我,犹如一群恶犬,

他们刺伤我的手脚。

17我身上的骨头历历可见,

人们都幸灾乐祸地看着我。

18他们分我的外衣,

又为我的内衣抽签。

19耶和华啊,求你不要远离我。

你是我的力量,

求你快来帮助我。

20求你救我逃脱刀剑之灾,

从这些恶犬的利爪下拯救我的生命。

21求你救我脱离狮子的口,

使我脱离野牛的角。

22我要向众弟兄传扬你的名,

在会众当中赞美你。

23敬畏耶和华的人啊,

你们都要赞美祂,

雅各的后裔都要尊崇祂的名,

以色列的后裔都要敬畏祂。

24因为祂没有藐视、厌恶苦难中的人,

也没有掩面不顾他们,

而是垂听他们的呼求。

25我要在大会中赞美你,

在敬畏你的人面前履行我的誓言。

26穷苦人必得饱足,

寻求耶和华的人必赞美祂,

他们的心要永远欢欣跳跃。

27普世都要心系耶和华,归向祂,

各国人民都要敬拜祂。

28因为耶和华是主宰,

祂统治列国。

29世上的富贵人要敬拜祂,

必归尘土的世人都要敬拜祂。

30世世代代的人都要事奉祂,

传扬主所行的奇事。

31他们也要向未来的世代传讲祂的公义作为。