Masalimo 150 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 150:1-6

Salimo 150

1Tamandani Yehova.

Tamandani Mulungu mʼmalo ake opatulika;

mutamandeni ku thambo lake lamphamvu.

2Mutamandeni chifukwa cha machitidwe ake amphamvu;

mutamandeni chifukwa cha ukulu wake wopambana.

3Mutamandeni poyimba malipenga,

mutamandeni ndi pangwe ndi zeze.

4Mutamandeni ndi matambolini ndi kuvina,

mutamandeni ndi zingwe ndi zitoliro.

5Mutamandeni ndi ziwaya zolira za malipenga,

mutamandeni ndi ziwaya zolira kwambiri.

6Chamoyo chilichonse chopuma chitamande Yehova.

Tamandani Yehova.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 150:1-6

Salmo 150

1¡Aleluya! ¡Alabado sea el Señor!

Alabad a Dios en su santuario,

alabadle en su poderoso firmamento.

2Alabadle por sus proezas,

alabadle por su inmensa grandeza.

3Alabadle con sonido de trompeta,

alabadle con el arpa y la lira.

4Alabadle con panderos y danzas,

alabadle con cuerdas y flautas.

5Alabadle con címbalos sonoros,

alabadle con címbalos resonantes.

6¡Que todo lo que respira alabe al Señor!

¡Aleluya! ¡Alabado sea el Señor!