Masalimo 146 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 146:1-10

Salimo 146

1Tamandani Yehova.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

2Ndidzatamanda Yehova ndi moyo wanga wonse;

ndidzayimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wanga nthawi yonse ya moyo wanga.

3Musamadalire mafumu,

anthu osakhalitsa, amene sangathe kupulumutsa.

4Pamene mizimu yawo yachoka, iwo amabwerera ku dothi;

zimene ankafuna kuchita zimatha tsiku lomwelo.

5Wodala ndi amene thandizo lake ndi

Mulungu wa Yakobo.

6Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi,

nyanja ndi zonse zili mʼmenemo;

Yehova, amene ndi wokhulupirika kwamuyaya.

7Iye amachitira chilungamo anthu oponderezedwa

ndipo amapereka chakudya kwa anthu anjala.

Yehova amamasula amʼndende,

8Yehova amatsekula maso anthu osaona,

Yehova amadzutsa onse amene awerama pansi,

Yehova amakonda anthu olungama.

9Yehova amasamalira alendo

ndipo amathandiza ana ndi akazi amasiye,

koma amasokoneza njira za anthu oyipa.

10Yehova ndiye Mfumu mpaka muyaya,

Mulungu wako iwe Ziyoni, pa mibado yonse.

Tamandani Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 146:1-10

Gott schützt die Schwachen

1Halleluja – lobt den Herrn!

Ich will den Herrn loben mit ganzer Hingabe,

2ja, ich will ihn loben, solange ich bin!

Zur Ehre meines Gottes will ich singen mein Leben lang.

3Setzt euer Vertrauen nicht auf Leute,

die Einfluss haben und Macht ausüben!

Sie sind doch bloß vergängliche Menschen

und können euch nicht retten.

4Sie werden sterben und zu Staub zerfallen;

und wenn ihr Lebensgeist sie verlässt,

dann vergehen auch all ihre Pläne.

5Glücklich aber ist der Mensch,

der seine Hilfe von dem Gott Jakobs erwartet!

Glücklich ist, wer seine Hoffnung auf den Herrn setzt!

6Denn er hat Himmel und Erde geschaffen,

das Meer und alles, was es dort gibt.

Für immer wird er zu seinem Wort stehen!

7Den Unterdrückten verschafft er Recht,

den Hungernden gibt er zu essen, und die Gefangenen befreit er.

8-9Der Herr macht die Blinden wieder sehend

und richtet die Niedergeschlagenen auf.

Er bietet den Ausländern Schutz und sorgt für die Witwen und Waisen.

Er liebt alle, die seinen Willen tun,

aber diejenigen, die ihn missachten, führt er in die Irre.

10Der Herr regiert für immer und ewig.

Zion, dein Gott herrscht für alle Zeit!

Lobt den Herrn – halleluja!