Masalimo 147 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 147:1-20

Salimo 147

1Tamandani Yehova.

Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,

nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!

2Yehova akumanga Yerusalemu;

Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.

3Akutsogolera anthu osweka mtima

ndi kumanga mabala awo.

4Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,

ndipo iliyonse amayitchula dzina.

5Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;

nzeru zake zilibe malire.

6Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,

koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

7Imbirani Yehova ndi mayamiko;

imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.

8Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;

amapereka mvula ku dziko lapansi

ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.

9Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe

ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.

10Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,

kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.

11Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.

12Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;

tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,

13pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako

ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.

14Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako

ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

15Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;

mawu ake amayenda mwaliwiro.

16Amagwetsa chisanu ngati ubweya

ndi kumwaza chipale ngati phulusa.

17Amagwetsa matalala ngati miyala.

Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?

18Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;

amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

19Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,

malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.

20Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;

anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.

Hoffnung für Alle

Psalm 147:1-20

Gottes Macht ist einzigartig

1Halleluja – lobt den Herrn!

Es ist gut, unserem Gott Loblieder zu singen;

ja, es macht Freude, ihn mit unserer Musik zu preisen.

2Der Herr baut Jerusalem wieder auf

und bringt die Israeliten zurück,

die man aus ihrem Land verschleppt hat.

3Er heilt die Menschen, die innerlich zerbrochen sind,

und verbindet ihre Wunden.

4Er hat die Zahl der Sterne festgelegt

und gab jedem einzelnen einen Namen.

5Wie groß ist unser Herr und wie gewaltig seine Macht!

Unermesslich ist seine Weisheit.

6Der Herr richtet die Erniedrigten auf

und tritt alle Gottlosen in den Staub.

7Singt dem Herrn Danklieder!

Spielt für unseren Gott auf der Harfe!

8Er überzieht den Himmel mit Wolken

und lässt es auf der Erde regnen.

Er sorgt dafür, dass Gras auf den Weiden wächst,

9und gibt den Tieren ihr Futter –

auch den jungen Raben, wenn sie danach krächzen.

10Viele Menschen erwarten ihre Sicherheit

von schnellen Pferden und guten Soldaten.

Gott aber lässt sich davon nicht beeindrucken.147,10 Wörtlich: Er hat nicht Lust an der Stärke des Rosses, er findet nicht Gefallen an den Schenkeln des Mannes.

11Der Herr freut sich über alle, die ihm in Ehrfurcht begegnen

und von seiner Gnade alles erwarten.

12Jerusalem, lobe den Herrn!

Du Stadt auf dem Berg Zion, rühme deinen Gott!

13Er gewährt dir Schutz in deinen Mauern147,13 Wörtlich: Er hat die Riegel deiner Tore stark gemacht.

und segnet die Menschen, die darin wohnen.

14Er gibt deinem Land Frieden und Wohlstand

und versorgt dich reichlich mit dem besten Getreide.

15Er sendet seine Befehle hinunter zur Erde,

und in Windeseile erreichen sie ihr Ziel.

16Er lässt es in dichten Flocken schneien

und überzieht alles mit feinem Reif.

17Dicke Hagelkörner lässt er auf die Erde prasseln,

er schickt klirrende Kälte, die kein Mensch erträgt.

18Er gibt einen Befehl, und schon schmilzt der Schnee;

er haucht das Eis an, und schon taut es.

19Den Nachkommen Jakobs hat er sein Wort verkündet,

damit sie nach seinen Gesetzen und Ordnungen leben.

20An keinem anderen Volk hat Gott je so gehandelt,

kein anderes kennt seine Ordnungen.

Lobt den Herrn – halleluja!