Masalimo 145 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 145:1-21

Salimo 145

Salimo la matamando la Davide.

1Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga;

ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.

2Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku

ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.

3Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse;

ukulu wake palibe angawumvetsetse.

4Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina;

Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.

5Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu,

ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.

6Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri,

ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.

7Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu,

ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.

8Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo,

wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.

9Yehova ndi wabwino kwa onse;

amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.

10Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova;

oyera mtima adzakulemekezani.

11Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu

ndi kuyankhula za mphamvu yanu,

12kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu

ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.

13Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya,

ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse.

Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse

ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.

14Yehova amagwiriziza onse amene akugwa

ndipo amakweza onse otsitsidwa.

15Maso a onse amayangʼana kwa Inu,

ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.

16Mumatsekula dzanja lanu

ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.

17Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse,

ndi wokonda zonse zimene anazipanga.

18Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana,

onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.

19Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa;

amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.

20Yehova amayangʼana onse amene amamukonda

koma adzawononga anthu onse oyipa.

21Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova.

Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera

ku nthawi za nthawi.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 145:1-21

Dwom 145

Ayɛyie dwom. Dawid deɛ.

1Mɛma wo so, me Onyankopɔn, me Ɔhene;

mɛkamfo wo din daa daa.

2Ɛda biara, mɛkamfo wo;

na mama wo din so daa daa.

3Awurade so, na ɔsɛ nkamfo kɛseɛ;

obiara rentumi nsusu ne kɛseyɛ.

4Awoɔ ntoatoasoɔ baako bɛkamfo wo nnwuma akyerɛ ɔfoforɔ;

wɔbɛka wo nnwuma akɛseɛ ho asɛm.

5Wɔbɛka wʼanimuonyam ne wo tumi a ɛhran no ho asɛm,

na mɛdwene wʼanwanwadwuma ho.

6Wɔbɛka wo nnwuma a ɛyɛ hu no mu tumi ho asɛm;

na mapae mu aka wo nneyɛɛ akɛseɛ no akyerɛ.

7Wɔbɛhyɛ wo papayɛ mmorosoɔ no ho fa,

na wɔde anigyeɛ ato wo tenenee ho dwom.

8Awurade yɛ ɔdomfoɔ ne mmɔborɔhunufoɔ;

ne bo kyɛre fu na nʼadɔeɛ dɔɔso.

9Awurade yɛ ma obiara;

na ɔwɔ ahummɔborɔ ma nʼabɔdeɛ nyinaa.

10Ao Awurade, wʼabɔdeɛ nyinaa bɛkamfo wo;

na wʼahotefoɔ bɛma wo so.

11Wɔbɛka wʼahennie no animuonyam ho asɛm

na wɔaka wo mmaninyɛ ho asɛm,

12sɛ ɛbɛyɛ a nnipa bɛhunu wo nnwuma akɛseɛ

ne wʼahennie animuonyam a ɛhran no.

13Wʼahennie yɛ daa ahennie,

na wo tumidie wɔ hɔ ma awoɔ ntoantoasoɔ nyinaa.

Awurade di ne bɔhyɛ nyinaa so,

na ɔwɔ ɔdɔ ma biribiara a wayɛ.

14Awurade wowa wɔn a wɔhwe ase

na ɔpagya wɔn a wɔn nnesoa ama wɔakom.

15Ani nyinaa hwɛ wo ɛkwan,

na woma wɔn wɔn aduane wɔ ne berɛ mu.

16Wobue wo nsam

na woma biribiara a ɛwɔ nkwa no nʼapɛdeɛ.

17Awurade tene wɔ nʼakwan nyinaa mu;

na ɔyɛ adɔeɛ ma deɛ wayɛ nyinaa.

18Awurade bɛn wɔn a wɔfrɛ no nyinaa,

wɔn a wɔfrɛ no nokorɛ mu nyinaa.

19Ɔyɛ wɔn a wɔsuro no no apɛdeɛ ma wɔn;

ɔtie wɔn sufrɛ na ɔgye wɔn.

20Awurade hwɛ wɔn a wɔdɔ no nyinaa so,

nanso amumuyɛfoɔ deɛ, ɔbɛsɛe wɔn nyinaa.

21Mʼano bɛkamfo Awurade.

Ma abɔdeɛ nyinaa nkamfo ne din kronkron no

daa daa.