Masalimo 144 – CCL & ASCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 144:1-15

Salimo 144

Salimo la Davide.

1Atamandike Yehova Thanthwe langa,

amene amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

zala zanga kumenya nkhondo.

2Iye ndiye Mulungu wanga wachikondi ndi malo anga otetezedwa,

linga langa ndi mpulumutsi wanga,

chishango changa mmene ine ndimathawiramo,

amene amagonjetsa mitundu ya anthu pansi panga.

3Inu Yehova, munthu nʼchiyani kuti mumamusamalira,

mwana wa munthu kuti muzimuganizira?

4Munthu ali ngati mpweya;

masiku ake ali ngati mthunzi wosakhalitsa.

5Ngʼambani mayiko akumwamba, Inu Yehova, ndipo tsikani pansi;

khudzani mapiri kuti atulutse utsi.

6Tumizani zingʼaningʼani ndi kubalalitsa adani;

ponyani mivi yanu ndi kuwathamangitsa.

7Tambasulani dzanja lanu kuchokera kumwamba;

landitseni ndi kundipulumutsa,

ku madzi amphamvu,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

8amene pakamwa pawo ndi podzala ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

9Ndidzakuyimbirani nyimbo yatsopano Inu Mulungu;

ndidzakuyimbirani nyimbo pa zeze wa nsambo khumi,

10kwa Iye amene amapambanitsa mafumu,

amene amapulumutsa Davide mtumiki wake ku lupanga loopsa.

11Landitseni ndi kundipulumutsa,

mʼmanja mwa anthu achilendo,

amene pakamwa pawo ndi podzaza ndi mabodza,

amene dzanja lawo lamanja ndi lachinyengo.

12Ndipo ana aamuna pa chinyamata chawo

adzakhala ngati mbewu yosamalidwa bwino,

ana athu aakazi adzakhala ngati zipilala

zosemedwa bwino, zokongoletsera nyumba yaufumu.

13Nkhokwe zathu zidzakhala zodzaza

ndi zokolola za mtundu uliwonse.

Nkhosa zathu zidzaswana miyandamiyanda

pa mabusa athu.

14Ngʼombe zathu zidzanyamula katundu wolemera.

Sipadzakhala mingʼalu pa makoma,

sipadzakhalanso kupita ku ukapolo,

mʼmisewu mwathu simudzakhala kulira chifukwa cha mavuto.

15Odala anthu amene adzalandira madalitso awa;

odala anthu amene Mulungu wawo ndi Yehova.

Asante Twi Contemporary Bible

Nnwom 144:1-15

Dwom 144

Dawid deɛ.

1Nkamfoɔ nka Awurade, me Botan,

deɛ ɔkyerɛkyerɛ me nsa akodie,

na ɔkyerɛkyerɛ me nsateaa akodie.

2Ɔyɛ mʼadɔeɛ Onyankopɔn ne mʼaban,

mʼabandenden ne me ɔgyefoɔ,

me kyɛm a mewɔ dwanekɔbea wɔ ne mu;

ɔno na ɔka nnipa hyɛ mʼase.

3Ao Awurade, hwan ne onipa, a wʼani ku ne ho?

Hwan ne onipa ba, a wodwene ne ho yi?

4Onipa te sɛ ahomeɛ;

ne nna te sɛ sunsum a ɛretwam.

5Ao Awurade, firi ɔsoro hɔ na siane bra fam;

fa wo nsa ka mmepɔ, na ɛmfiri wisie.

6Soma anyinam na bɔ atamfoɔ no hwete;

to wo mmemma no ma wɔn nnwane.

7Tene wo nsa firi soro bra fam;

gye me na yi me

firi nsuo akɛseɛ ho,

firi ananafoɔ nsam,

8wɔn a atorɔ ayɛ wɔn anomu ma,

na wɔn nsa nifa yɛ nnaadaa.

9Ao Onyankopɔn, mɛto dwom foforɔ ama wo;

mɛto dwom wɔ sankuo a nhoma edu gu soɔ so ama wo,

10ama Ɔbaako a ɔde nkonimdie ma ahemfo,

na ɔgye ne ɔsomfoɔ Dawid firi akofena kɔdiawuo ano.

11Gye me na yi me firi

ananafoɔ nsam,

wɔn a atorɔ ayɛ wɔn anomu ma

na wɔn nsa nifa yɛ nnaadaa.

12Afei yɛn mmammarima mmeranteberɛ

bɛyɛ sɛ afifideɛ a wɔahwɛ so yie,

na yɛn mmammaa bɛyɛ sɛ adum

a wɔasene de asiesie ahemfie.

13Yɛn asan bɛyɛ ma.

Aduane ahodoɔ biara bɛba mu bi.

Yɛn nnwan bɛdɔɔso ayɛ mpem mpem,

ayɛ mpemdu du wɔ yɛn mfuo so;

14yɛn anantwie bɛtwe nnuane a ɛdɔɔso na emu yɛ duru.

Obiara rentumi nnwiri yɛn afasuo ngu;

yɛrenkɔ nkoasom mu,

na agyaadwotwa remma yɛn mmɔntene so.

15Nhyira nka nnipa a ɛbɛba mu saa ama wɔn.

Nhyira nka nnipa a wɔn Onyankopɔn ne Awurade.