Masalimo 143 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 143:1-12

Salimo 143

Salimo la Davide.

1Yehova imvani pemphero langa,

mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo;

mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu

bwerani kudzandithandiza.

2Musazenge mlandu mtumiki wanu,

pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.

3Mdani akundithamangitsa,

iye wandipondereza pansi;

wachititsa kuti ndikhale mu mdima

ngati munthu amene anafa kale.

4Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga;

mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.

5Ndimakumbukira masiku amakedzana;

ndimalingalira za ntchito yanu yonse,

ndimaganizira zimene manja anu anachita.

6Ndatambalitsa manja anga kwa Inu;

moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma.

Sela

7Yehova ndiyankheni msanga;

mzimu wanga ukufowoka.

Musandibisire nkhope yanu,

mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.

8Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika,

pakuti ine ndimadalira Inu.

Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo,

pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.

9Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova,

pakuti ndimabisala mwa Inu.

10Phunzitseni kuchita chifuniro chanu,

popeza ndinu Mulungu wanga;

Mzimu wanu wabwino unditsogolere

pa njira yanu yosalala.

11Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu;

mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.

12Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga;

wonongani adani anga,

pakuti ndine mtumiki wanu.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 143:1-12

Zabbuli 143

Zabbuli Ya Dawudi.

1143:1 a Zab 140:6 b Zab 89:1-2 c Zab 71:2Wulira okusaba kwange, Ayi Mukama,

wulira okwegayirira kwange!

Ggwe omwesigwa

era omutuukirivu jjangu ombeere.

2143:2 Zab 14:3; Mub 7:20; Bar 3:20Tonsalira musango,

kubanga mu maaso go tewali n’omu atuukiridde.

3Omulabe wange angoba n’ankwata n’ansuula wansi;

anteeka mu kizikiza ne nfaanana ng’abaafa edda.

4143:4 Zab 142:3Noolwekyo omwoyo gwange guweddemu endasi,

n’omutima gwange gwennyise.

5143:5 Zab 77:6Nzijukira ennaku ez’edda,

ne nfumiitiriza ku ebyo bye wakola byonna,

ne ndowooza ku mirimu gy’emikono gyo.

6143:6 Zab 63:1; 88:9Ngolola emikono gyange gy’oli,

ne nkuyaayaanira ng’ettaka ekkalu bwe liyaayaanira enkuba.

7143:7 a Zab 69:17 b Zab 27:9; 28:1Yanguwa okunziramu, Ayi Mukama,

kubanga omwoyo gwange guggwaamu amaanyi.

Tonkisa maaso go,

nneme okufaanana ng’abafu.

8143:8 a Zab 46:5; 90:14 b Zab 27:11 c Zab 25:1-2Obudde nga bukedde, nsaba ondage okwagala kwo okutaggwaawo;

kubanga ggwe gwe neesiga.

Njigiriza ekkubo lye nsaana okutambuliramu,

kubanga omwoyo gwange gwonna guli gy’oli.

9143:9 Zab 31:15Mponya, Ayi Mukama, abalabe bange,

kubanga ggwe kiddukiro kyange.

10143:10 Nek 9:20; Zab 23:3; 25:4-5Njigiriza okukola by’oyagala,

kubanga ggwe Katonda wange!

Omwoyo wo omulungi ankulembere,

antambulize mu kkubo eddungi ery’omuseetwe.

11143:11 a Zab 119:25 b Zab 31:1Olw’erinnya lyo, Ayi Mukama, onkuume,

mu butuukirivu bwo onzigye mu kabi.

12143:12 a Zab 52:5; 54:5 b Zab 116:16Omalewo abalabe bange olw’okwagala kwo,

ozikirize n’abanjigganya bonna,

kubanga nze ndi muddu wo.