Masalimo 142 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 142:1-7

Salimo 142

Ndakatulo ya Davide, pamene iyeyo anali mʼphanga. Pemphero.

1Ndikulirira Yehova mofuwula;

ndikukweza mawu anga kwa Yehova kupempha chifundo.

2Ndikukhuthula madandawulo anga pamaso pake;

ndikufotokoza za masautso anga pamaso pake.

3Pamene mzimu wanga walefuka mʼkati mwanga,

ndinu amene mudziwa njira yanga.

Mʼnjira imene ndimayendamo

anthu anditchera msampha mobisa.

4Yangʼanani kumanja kwanga ndipo onani;

palibe amene akukhudzika nane.

Ndilibe pothawira;

palibe amene amasamala za moyo wanga.

5Ndilirira Inu Yehova;

ndikuti, “Ndinu pothawirapo panga,

gawo langa mʼdziko la anthu amoyo.”

6Mverani kulira kwanga

pakuti ndathedwa nzeru;

pulumutseni kwa amene akundithamangitsa

pakuti ndi amphamvu kuposa ine.

7Tulutseni mʼndende yanga

kuti nditamande dzina lanu.

Ndipo anthu olungama adzandizungulira

chifukwa cha zabwino zanu pa ine.

Luganda Contemporary Bible

Zabbuli 142:1-7

Zabbuli 142

Okusaba kwa Dawudi bwe yali mu mpuku.

1142:1 Zab 30:8Nkaabirira Mukama n’eddoboozi ery’omwanguka;

neegayirira Mukama ansaasire.

2142:2 Is 26:16Mmutegeeza byonna ebinneemulugunyisa,

ne mmwanjulira ebinteganya byonna.

3142:3 Zab 140:5; 143:4, 7Omwoyo gwange bwe gunnennyika,

gw’omanyi eky’okunkolera.

Banteze omutego mu kkubo lyange mwe mpita.

4142:4 Zab 31:11; Yer 30:17Bwe ntunula ku mukono gwange ogwa ddyo, sirabayo anambeera;

sirina wa kwekweka, era tewali n’omu anfaako.

5142:5 a Zab 46:1 b Zab 16:5 c Zab 27:13Nkaabirira ggwe, Ayi Mukama,

nga ŋŋamba nti, “Ggwe kiddukiro kyange,

ggwe mugabo gwange mu nsi muno.”

6142:6 a Zab 17:1 b Zab 79:8; 116:6Owulire okukaaba kwange,

kubanga njeezebwa nnyo!

Mponya abanjigganya,

kubanga bansinza nnyo amaanyi.

7142:7 a Zab 146:7 b Zab 13:6Nziggya mu kkomera,

ndyoke nkwebaze nga ntendereza erinnya lyo.

Abatuukirivu balinneetooloola,

ng’onkoledde ebyekisa ekingi ebingi.