Masalimo 141 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

Nueva Versión Internacional

Salmo 141:1-10

Salmo 141

Salmo de David.

1A ti clamo, Señor, ven pronto a mí.

Escucha mi voz cuando a ti clamo.

2Que suba a tu presencia mi oración

como una ofrenda de incienso,

mis manos levantadas

como el sacrificio de la tarde.

3Señor, ponme en la boca un centinela;

un guardia a la puerta de mis labios.

4No permitas que mi corazón se incline a la maldad

ni que sea yo cómplice de iniquidades;

no me dejes participar de banquetes

en compañía de malhechores.

5Que cuando el justo me castigue,

sea una muestra de amor;

que su reprensión sea bálsamo que mi cabeza no rechace,

pues mi oración siempre está en contra de las malas obras.

6Cuando sus gobernantes sean arrojados desde los despeñaderos,

sabrán que mis palabras eran bien intencionadas.

7Y dirán: «Así como se esparce la tierra

cuando en ella se abren surcos con el arado,

así se han esparcido nuestros huesos

a la orilla del sepulcro».141:7 sepulcro. Lit. Seol.

8Por eso tengo los ojos puestos en ti, mi Señor y Dios,

en ti busco refugio; no me dejes morir.

9Protégeme de las trampas que me tienden,

de las trampas que me tienden los malhechores.

10Que caigan los malvados en sus propias redes,

mientras yo salgo bien librado.