Masalimo 141 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 141:1-10

Salimo 141

Salimo la Davide.

1Inu Yehova ndikukuyitanani; bwerani msanga kwa ine.

Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu.

2Pemphero langa lifike kwa Inu ngati lubani;

kukweza manja kwanga kukhale ngati nsembe yamadzulo.

3Yehova ikani mlonda pakamwa panga;

londerani khomo la pa milomo yanga.

4Musalole kuti mtima wanga ukokedwere ku zoyipa;

kuchita ntchito zonyansa

pamodzi ndi anthu amene amachita zoyipa;

musalole kuti ndidye nawo zokoma zawo.

5Munthu wolungama andikanthe, chimenecho ndiye chifundo;

andidzudzule ndiye mafuta pa mutu wanga.

Mutu wanga sudzakana zimenezi.

Komabe pemphero langa nthawi zonse ndi lotsutsana ndi ntchito za anthu ochita zoyipa.

6Olamulira awo adzaponyedwa pansi kuchokera pa malo okwera kwambiri,

ndipo anthu oyipa adzaphunzira kuti mawu anga anayankhulidwa bwino.

7Iwo adzati, “Monga momwe nkhuni zimamwazikira akaziwaza,

ndi momwenso mafupa athu amwazikira pa khomo la manda.”

8Koma maso anga akupenyetsetsa Inu Ambuye Wamphamvuzonse;

ndimathawira kwa Inu, musandipereke ku imfa.

9Mundipulumutse ku misampha imene anditchera,

ku makhwekhwe amene anthu oyipa andikonzera.

10Anthu oyipa akodwe mʼmaukonde awo,

mpaka ine nditadutsa mwamtendere.

New Russian Translation

Псалтирь 141:1-7

Псалом 141

1Наставление Давида. Его молитва, когда он находился в пещере141:1 См. 1 Цар. 22:1-2..

Громко взываю я к Господу,

громко Господа умоляю.

2Перед Ним я излил свою жалобу

и открыл Ему свою скорбь.

3Когда изнемогал во мне дух,

Ты знал мой путь.

На дороге, по которой я шел,

тайно поставили для меня сеть.

4Я смотрю вокруг, ища своего защитника,

но вижу, что никому нет до меня дела.

Нет у меня убежища,

никто не заботится о моей жизни.

5Взываю я к Тебе, Господи,

и говорю: «Ты – мое убежище

и мой удел в земле живых».

6Прислушайся к моему молению,

потому что я сильно изнемог;

избавь меня от преследователей,

потому что они сильнее меня.

7Освободи меня из темницы,

чтобы я вознес хвалу имени Твоему.

Меня обступят праведники,

когда Ты воздашь мне добром.