Masalimo 137 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.

Korean Living Bible

시편 137:1-9

시온을 그리워하는 포로들

1우리는

바빌론 강변에 앉아서

시온을 기억하며 울었다.

2우리가 수금을

버드나무 가지에 걸었으니

3우리를 사로잡은 자들이

우리에게 노래를 청하고

우리를 괴롭히는 자들이

즐거운 노래를 요구하며

“시온의 노래 중 하나를 불러라”

하고 말하였음이라.

4우리가 외국 땅에서 어떻게

여호와의 노래를 부를 수 있겠는가?

5예루살렘아,

내가 너를 잊는다면

내 오른손이 수금 타는 법도

잊어버리기를 원하노라.

6내가 너를 기억하지 않거나

내가 너를 가장 큰 기쁨으로

여기지 않는다면

137:6 또는 ‘내 혀가 내 입천장에 붙을지로다’내가 다시는 노래를

부르지 못하게 하라.

7여호와여, 예루살렘이

함락되던 날에

에돔 사람들이 한 짓을 기억하소서.

그들이 “예루살렘성을 헐어라!

그 기초까지 헐어 버려라!”

하였습니다.

8바빌론아, 너는 멸망할 것이다.

네가 우리에게 행한 대로

갚아 주는 자가 복이 있으리라.

9네 아이들을 잡아다가 바위에

메어치는 자가 복이 있으리라.