Masalimo 132 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 132:1-18

Salimo 132

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Inu Yehova, kumbukirani Davide

ndi mavuto onse anapirira.

2Iye analumbira kwa Yehova

ndi kulonjeza kwa Wamphamvu wa Yakobo kuti,

3“Sindidzalowa mʼnyumba mwanga

kapena kugona pa bedi langa:

4sindidzalola kuti maso anga agone,

kapena zikope zanga ziwodzere,

5mpaka nditamupezera malo Yehova,

malo okhala a Wamphamvu wa Yakobo.”

6Zoonadi, tinamva za Bokosi la Chipangano ku Efurata,

tinalipeza mʼminda ya ku Yaara:

7“Tiyeni tipite ku malo ake okhalamo;

tiyeni tikamulambire pa mapazi ake.

8‘Dzukani Yehova, ndipo bwerani ku malo anu opumulira,

Inuyo ndi Bokosi la Chipangano limene limafanizira mphamvu zanu.

9Ansembe anu avekedwe chilungamo;

anthu anu oyera mtima ayimbe nyimbo mwachimwemwe.’ ”

10Chifukwa cha Davide mtumiki wanu,

musakane wodzozedwa wanu.

11Yehova analumbira kwa Davide,

lumbiro lotsimikizika kuti Iye sadzasintha:

“Mmodzi wa ana ako

ndidzamuyika pa mpando waufumu;

12ngati ana ako azisunga pangano langa

ndi malamulo amene ndiwaphunzitsa,

pamenepo ana awo adzakhala pa mpando

wako waufumu kwamuyaya ndi muyaya.”

13Pakuti Yehova wasankha Ziyoni,

Iye wakhumba kuti akhale malo ake okhalamo:

14“Awa ndi malo anga opumapo ku nthawi za nthawi;

ndidzakhala pano pa mpando waufumu, pakuti ndakhumba zimenezi.

15Ndidzadalitsa mzindawu ndi zinthu zambiri;

anthu ake osauka ndidzawakhutitsa ndi chakudya.

16Ndidzaveka ansembe ake chipulumutso,

ndipo anthu ake oyera mtima adzayimba nthawi zonse nyimbo zachimwemwe.

17“Pano ndidzachulukitsa mphamvu za Davide

ndi kuyikapo nyale ya wodzozedwa wanga.

18Ndidzaveka adani ake manyazi,

koma chipewa chaufumu pamutu pake chidzakhala chowala.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 132:1-18

第 132 篇

求上帝赐福圣殿

上圣殿朝圣之诗。

1耶和华啊,

求你顾念大卫和他所受的一切苦难。

2他曾向你起誓,

雅各的大能者许愿说:

3-5“我不为耶和华找到居所,

不为雅各的大能者找到安居之处,

必不进家门,

不沾床,不睡觉,不打盹。”

6我们在以法他听到约柜的消息,

基列·耶琳找到了它。

7让我们进入耶和华的居所,

在祂脚前俯伏敬拜。

8耶和华啊,

求你起来和你大能的约柜一同进入圣所。

9愿你的祭司身披公义,

愿你忠心的子民高声欢唱。

10为了你仆人大卫的缘故,

求你不要弃绝你所膏立的人。

11耶和华曾向大卫起了永不废弃的誓说:

“我必使你的后代继承你的王位。

12你的后代若守我的约,

遵行我教导他们的法度,

他们的子孙必永远坐在你的宝座上。”

13因为耶和华已经拣选了锡安

愿意将锡安作为祂的居所。

14祂说:“这是我永远的居所;

我要住在这里,

因为我喜爱这地方。

15我要使她粮食充足,

使她里面的穷人饮食无忧。

16我要用救恩作她祭司的衣裳,

城里忠心的子民必高声欢唱。

17我必使大卫的后裔在那里做王,

我必为我所膏立的预备明灯。

18我必使他的仇敌满面羞愧,

但他头上的王冠必光芒四射。”