Salimo 129
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
anene tsono Israeli;
2“Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
koma sanandipambane.
3Anthu otipula analima pa msana panga
ndipo anapangapo mizere yayitali:
4Koma Yehova ndi wolungama;
Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5Onse amene amadana ndi Ziyoni
abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
umene umafota usanakule;
7sungadzaze manja a owumweta
kapena manja a omanga mitolo.
8Odutsa pafupi asanene kuti,
“Dalitso la Yehova lili pa inu;
tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
الْمَزْمُورُ الْمِئَةُ وَالتَّاسِعُ وَالْعِشْرُونَ
تَرْنِيمَةُ الْمَصَاعِدِ
1مَا أَكْثَرَ مَا ضَايَقُونِي فِي حَدَاثَتِي يَقُولُ إِسْرَائِيلُ. 2مَا أَكْثَرَ مَا ضَايَقُونِي فِي حَدَاثَتِي، لَكِنَّهُمْ لَمْ يَتَغَلَّبُوا عَلَيَّ. 3جَرَحُوا ظَهْرِي جُرُوحاً عَمِيقَةً، فَصَارَ كَالأَتْلامِ (خُطُوطِ الْمِحْرَاثِ) الطَّوِيلَةِ فِي حَقْلٍ مَحْرُوثٍ. 4الرَّبُّ عَادِلٌ، كَسَرَ أَغْلالَ عُبُودِيَّةِ الأَشْرَارِ. 5فَلْيَخْزَ وَلْيُدْبِرْ جَمِيعُ مُبْغِضِي صِهْيَوْنَ. 6لِيَكُونُوا كَالْعُشْبِ النَّابِتِ عَلَى السُّطُوحِ، الَّذِي يَجِفُّ قَبْلَ أَنْ يَنْمُوَ، 7فَلَا يَمْلأُ الْحَاصِدُ مِنْهُ يَدَهُ، وَلَا الْحَازِمُ حِضْنَهُ. 8وَلَا يَقُولُ عَابِرُو السَّبِيلِ لَهُمْ: «لِتَكُنْ عَلَيْكُمْ بَرَكَةُ الرَّبِّ: نُبَارِكُكُمْ بِاسْمِ الرَّبِّ».