Masalimo 128 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 128:1-6

Salimo 128

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Odala ndi onse amene amaopa Yehova,

amene amayenda mʼnjira zake.

2Udzadya chipatso cha ntchito yako;

madalitso ndi chuma zidzakhala zako.

3Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka

mʼkati mwa nyumba yako;

ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi

kuzungulira tebulo lako.

4Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa

amene amaopa Yehova.

5Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni

masiku onse a moyo wako;

uwone zokoma za Yerusalemu,

6ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako.

Mtendere ukhale ndi Israeli.

Ketab El Hayat

مزمور 128:1-6

الْمَزْمُورُ الْمِئَةُ وَالثَّامِنُ وَالْعِشْرُونَ

تَرْنِيمَةُ الْمَصَاعِدِ

1طُوبَاكَ يَا مَنْ تَتَّقِي الرَّبَّ وَتَسْلُكُ فِي طُرُقِهِ. 2لأَنَّكَ تَأْكُلُ مِنْ تَعَبِ يَدَيْكَ وَتَتَمَتَّعُ بِالسَّعَادَةِ وَالْخَيْرِ. 3تَكُونُ امْرَأَتُكَ كَكَرْمَةٍ مُثْمِرَةٍ فِي جَوَانِبِ بَيْتِكَ، وَأَبْنَاؤُكَ كَأَغْرَاسِ الزَّيْتُونِ حَوْلَ مَائِدَتِكَ. 4هَكَذَا يُبَارَكُ الرَّجُلُ الَّذِي يَتَّقِي الرَّبَّ. 5يُبَارِكُكَ الرَّبُّ مِنْ صِهْيَوْنَ، حَتَّى تَشْهَدَ خَيْرَ أُورُشَلِيمَ كُلَّ أَيَّامِ حَيَاتِكَ، 6وَتَعِيشَ لِتَرَى أَحْفَادَكَ. وَلْيَكُنْ لِشَعْبِ إِسْرَائِيلَ سَلامٌ.