Masalimo 126 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.

King James Version

Psalms 126:1-6

A Song of degrees.

1When the LORD turned again the captivity of Zion, we were like them that dream.126.1 turned…: Heb. returned the returning

2Then was our mouth filled with laughter, and our tongue with singing: then said they among the heathen, The LORD hath done great things for them.126.2 hath…: Heb. hath magnified to do with them

3The LORD hath done great things for us; whereof we are glad.

4Turn again our captivity, O LORD, as the streams in the south.

5They that sow in tears shall reap in joy.126.5 joy: or, singing

6He that goeth forth and weepeth, bearing precious seed, shall doubtless come again with rejoicing, bringing his sheaves with him.126.6 precious…: or, seed basket