Masalimo 125 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 125:1-5

Salimo 125

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Amene amadalira Yehova ali ngati phiri la Ziyoni,

limene silingagwedezeke koma ndi lokhala mpaka muyaya.

2Monga mapiri azungulira Yerusalemu,

momwemonso Yehova azungulira anthu ake

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

3Ndodo yaufumu ya anthu oyipa sidzakhala

pa dziko limene lapatsidwa kwa anthu olungama,

kuti anthu olungamawo

angachite nawonso zoyipa.

4Yehova chitirani zabwino amene ndi abwino,

amene ndi olungama mtima

5Koma amene amatembenukira ku njira zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi anthu ochita zoyipa.

Mtendere ukhale pa Israeli.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 125:1-5

第 125 篇

上帝保护祂的子民

上圣殿朝圣之诗。

1信靠耶和华的人就像锡安山永不动摇。

2群山怎样环绕耶路撒冷

耶和华也怎样保护祂的子民,

从现在直到永远。

3恶人必不能长久统治义人的土地,

免得义人也去行恶。

4耶和华啊,求你善待行善的人,

善待心地正直的人。

5耶和华必把那些偏行恶道的人与作恶的人一同赶走。

愿平安临到以色列