Masalimo 121 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 121:1-8

Salimo 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

Nueva Versión Internacional

Salmo 121:1-8

Salmo 121

Cántico de los peregrinos.

1A las montañas levanto mis ojos;

¿de dónde ha de venir mi ayuda?

2Mi ayuda proviene del Señor,

que hizo el cielo y la tierra.

3No permitirá que tu pie resbale;

jamás duerme el que te cuida.

4Jamás duerme ni se adormece

el que cuida de Israel.

5El Señor es quien te cuida;

el Señor es tu sombra a tu mano derecha.

6De día el sol no te hará daño

ni la luna de noche.

7El Señor te cuidará;

de todo mal guardará tu vida.

8El Señor cuidará tu salida y tu entrada,

desde ahora y para siempre.