Salimo 121
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
1Ndikweza maso anga ku mapiri;
kodi thandizo langa limachokera kuti?
2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3Sadzalola kuti phazi lako literereke;
Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4Taonani, Iye amene amasunga Israeli
sadzawodzera kapena kugona.
5Yehova ndiye amene amakusunga;
Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,
kapena mwezi nthawi ya usiku.
7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;
adzasunga moyo wako.
8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;
kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Mon secours vient de l’Eternel
1Cantique pour la route vers la demeure de l’Eternel121.1 Voir note 120.1..
Je lève les yeux vers les monts :
d’où le secours me viendra-t-il ?
2Mon secours vient de l’Eternel
qui a fait le ciel et la terre.
3Il te gardera des faux pas,
celui qui te protège ╵ne sommeillera pas.
4Non, jamais il ne dort, ╵jamais il ne sommeille,
celui qui protège Israël.
5L’Eternel est ton protecteur,
l’Eternel est à ton côté ╵comme une ombre qui te protège.
6Le soleil ne te frappera donc pas le jour,
ni la lune pendant la nuit.
7L’Eternel te gardera de tout mal :
il gardera ta vie.
8L’Eternel veillera sur toi ╵pendant tes allées et venues,
dès maintenant et à jamais.