Masalimo 121 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 121:1-8

Salimo 121

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndikweza maso anga ku mapiri;

kodi thandizo langa limachokera kuti?

2Thandizo langa limachokera kwa Yehova,

wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3Sadzalola kuti phazi lako literereke;

Iye amene amakusunga sadzawodzera.

4Taonani, Iye amene amasunga Israeli

sadzawodzera kapena kugona.

5Yehova ndiye amene amakusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.

6Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana,

kapena mwezi nthawi ya usiku.

7Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse;

adzasunga moyo wako.

8Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako;

kuyambira tsopano mpaka muyaya.

La Bible du Semeur

Psaumes 121:1-8

Mon secours vient de l’Eternel

1Cantique pour la route vers la demeure de l’Eternel121.1 Voir note 120.1..

Je lève les yeux vers les monts :

d’où le secours me viendra-t-il ?

2Mon secours vient de l’Eternel

qui a fait le ciel et la terre.

3Il te gardera des faux pas,

celui qui te protège ╵ne sommeillera pas.

4Non, jamais il ne dort, ╵jamais il ne sommeille,

celui qui protège Israël.

5L’Eternel est ton protecteur,

l’Eternel est à ton côté ╵comme une ombre qui te protège.

6Le soleil ne te frappera donc pas le jour,

ni la lune pendant la nuit.

7L’Eternel te gardera de tout mal :

il gardera ta vie.

8L’Eternel veillera sur toi ╵pendant tes allées et venues,

dès maintenant et à jamais.