Salimo 119
Alefu
1Odala ndi amene moyo wawo ulibe cholakwa,
amene amayenda monga mwa malamulo a Yehova.
2Odala ndi amene amasunga malamulo ake,
amene amafunafuna Iyeyo ndi mtima wawo wonse.
3Sachita cholakwa chilichonse;
amayenda mʼnjira zake.
4Inu mwapereka malangizo
ndipo ayenera kutsatidwa kwathunthu.
5Aa! Ndikanakonda njira zanga zikanakhala zokhazikika
pa kumvera zophunzitsa zanu!
6Pamenepo ine sindikanachititsidwa manyazi,
poganizira malamulo anu onse.
7Ndidzakutamandani ndi mtima wolungama,
pamene ndikuphunzira malamulo anu olungama.
8Ndidzamvera zophunzitsa zanu;
musanditaye kwathunthu.
Beti
9Kodi mnyamata angathe bwanji kuyeretsa mayendedwe ake?
Akawasamala potsata mawu anu.
10Ndimakufunafunani ndi mtima wanga wonse;
musalole kuti ndisochere kuchoka pa malamulo anu.
11Ndasunga mawu anu mu mtima mwanga
kuti ndisakuchimwireni.
12Mutamandike Inu Yehova;
phunzitseni malamulo anu.
13Ndi milomo yanga ndimafotokoza malamulo anu onse
amene amachokera pakamwa panu.
14Ndimakondwera potsatira malamulo anu
monga momwe munthu amakondwera akakhala ndi chuma chambiri.
15Ndimalingalira malangizo anu
ndipo ndimaganizira njira zanu.
16Ndimakondwera ndi malamulo anu;
sindidzayiwala konse mawu anu.
Gimeli
17Chitirani zokoma mtumiki wanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
kuti tsono ndisunge mawu anu.
18Tsekulani maso anga kuti ndithe kuona
zinthu zodabwitsa mʼmalamulo anu.
19Ine ndine mlendo pa dziko lapansi;
musandibisire malamulo anu.
20Moyo wanga wafowoka polakalaka
malamulo anu nthawi zonse.
21Inu mumadzudzula onyada, otembereredwa,
amene achoka pa malamulo anu.
22Mundichotsere chitonzo ndi mnyozo
pakuti ndimasunga malamulo anu.
23Ngakhale mafumu akhale pamodzi kundinyoza,
mtumiki wanu adzalingalirabe zophunzitsa zanu.
24Malamulo anu amandikondweretsa;
ndiwo amene amandilangiza.
Daleti
25Moyo wanga wakangamira fumbi;
tsitsimutseni molingana ndi mawu anu.
26Ndinafotokoza njira zanga ndipo Inu munandiyankha;
phunzitseni malamulo anu.
27Mundidziwitse chiphunzitso cha malangizo anu;
pamenepo ndidzalingalira zodabwitsa zanu.
28Moyo wanga wafowoka ndi chisoni;
limbikitseni monga mwa mawu anu.
29Mundichotse mʼnjira zachinyengo;
mundikomere mtima pondiphunzitsa malamulo anu.
30Ndasankha njira ya choonadi;
ndayika malamulo anu pa mtima panga.
31Ndagwiritsitsa umboni wanu, Inu Yehova;
musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
32Ndimathamanga mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti Inu mwamasula mtima wanga.
He
33Yehova, phunzitseni kutsatira zophunzitsa zanu;
ndipo ndidzazisunga mpaka kumapeto.
34Mundipatse mtima womvetsa zinthu ndipo ndidzasunga malamulo anu
ndi kuwamvera ndi mtima wanga wonse.
35Munditsogolere mʼnjira ya malamulo anu,
pakuti mʼmenemo ndimapezamo chikondwerero changa.
36Tembenuzani mtima wanga kuti uzikonda malamulo anu,
osati chuma.
37Tembenuzani maso anga kuchoka ku zinthu zachabechabe;
sungani moyo wanga monga mwa mawu anu.
38Kwaniritsani lonjezo lanu kwa mtumiki wanu,
kuti Inu muopedwe.
39Mundichotsere chipongwe chimene ndikuchiopa,
pakuti malamulo anu ndi abwino.
40Taonani, ndimalakalakatu malangizo anu!
Sungani moyo wanga mʼchilungamo chanu.
Wawi
41Chikondi chanu chosasinthika chibwere kwa ine, Inu Yehova,
chipulumutso chanu monga mwa lonjezo lanu;
42ndipo ndidzayankha amene amandinyoza,
popeza ndimadalira mawu anu.
43Musakwatule mawu a choonadi mʼkamwa mwanga,
pakuti ndakhazikitsa chiyembekezo changa mʼmalamulo anu.
44Ndidzasunga malamulo anu nthawi zonse,
ku nthawi za nthawi.
45Ndidzayendayenda mwaufulu,
chifukwa ndinafunafuna malangizo anu.
46Ndidzayankhula za umboni wanu pamaso pa mfumu
ndipo sindidzachititsidwa manyazi,
47popeza ndimakondwera ndi malamulo anu
chifukwa ndimawakonda.
48Ndikweza manja anga ku malamulo anu, ku malamulo amene ndimawakonda,
ndipo ndimalingalira malangizo anu.
Zayini
49Kumbukirani mawu anu kwa mtumiki wanu,
popeza mwandipatsa chiyembekezo.
50Chitonthozo changa pa masautso anga ndi ichi:
lonjezo lanu limasunga moyo wanga.
51Odzikuza amandinyoza popanda chowaletsa,
koma sindichoka pa malamulo anu.
52Ndimakumbukira malamulo anu Yehova akalekale,
ndipo mwa iwo ndimapeza chitonthozo.
53Ndayipidwa kwambiri chifukwa cha oyipa
amene ataya malamulo anu.
54Zophunzitsa zanu ndi mitu ya nyimbo yanga
kulikonse kumene ndigonako.
55Usiku ndimakumbukira dzina lanu Yehova,
ndipo ndidzasunga malamulo anu.
56Ichi ndicho ndakhala ndikuchita:
ndimasunga malangizo anu.
Heti
57Yehova, Inu ndiye gawo langa;
ndalonjeza kumvera mawu anu.
58Ndimafunafuna nkhope yanu ndi mtima wanga wonse;
mundikomere mtima monga mwa lonjezo lanu.
59Ndinalingalira za njira zanga
ndipo ndatembenuza mayendedwe anga kutsatira umboni wanu.
60Ndidzafulumira ndipo sindidzazengereza
kumvera malamulo anu.
61Ngakhale oyipa andimange ndi zingwe,
sindidzayiwala lamulo lanu.
62Ndimadzuka pakati pa usiku kuyamika Inu
chifukwa cha malamulo anu olungama.
63Ine ndine bwenzi la onse amene amakukondani,
kwa onse amene amatsatira malangizo anu.
64Dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chanu chosasinthika,
phunzitseni malamulo anu.
Teti
65Inu Yehova, chitirani chabwino mtumiki wanu
molingana ndi mawu anu.
66Phunzitseni nzeru ndi chiweruzo chabwino,
pakuti ndimakhulupirira malamulo anu.
67Ndisanayambe kuzunzika ndinasochera,
koma tsopano ndimamvera mawu anu.
68Inu ndinu abwino ndipo zimene mumachita ndi zabwino;
phunzitseni malamulo anu.
69Ngakhale odzikuza andipaka mabodza,
ine ndimasunga malangizo anu ndi mtima wanga wonse.
70Mitima yawo ndi yowuma ndi yosakhudzidwa,
koma ine ndimakondwera ndi malamulo anu.
71Ndi bwino kuti ndinasautsidwa
kuti ndithe kuphunzira malamulo anu.
72Lamulo lochokera mʼkamwa mwanu limandikomera kwambiri
kuposa ndalama zambirimbiri za siliva ndi golide.
Yodi
73Manja anu anandilenga ndi kundiwumba;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ndiphunzire malamulo anu.
74Iwo amene amakuopani akondwere akandiona,
chifukwa chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
75Ine ndikudziwa, Inu Yehova, kuti malamulo anu ndi olungama
ndipo mwandizunza chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
76Chikondi chanu chosasinthika chikhale chitonthozo changa,
molingana ndi lonjezo lanu kwa mtumiki wanu.
77Chifundo chanu chindifikire kuti ndikhale ndi moyo,
popeza malamulo anu ndiye chikondwerero changa.
78Odzikuza achititsidwe manyazi chifukwa cha kundilakwira popanda chifukwa;
koma ine ndidzalingalira malangizo anu.
79Iwo amene amakuopani atembenukire kwa ine,
iwo amene amamvetsetsa umboni wanu.
80Mtima wanga ukhale wopanda cholakwa pa chiphunzitso chanu
kuti ndisachititsidwe manyazi.
Kafu
81Moyo wanga wafowoka ndi kufunafuna chipulumutso chanu,
koma chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
82Maso anga alefuka pofunafuna lonjezo lanu;
Ine ndikuti, “Kodi mudzanditonthoza liti?”
83Ngakhale ndili ngati thumba lachikopa la vinyo pa utsi
sindiyiwala zophunzitsa zanu.
84Kodi mtumiki wanu ayenera kudikira mpaka liti?
Kodi mudzawalanga liti amene amandizunza?
85Anthu osalabadira za Mulungu,
odzikuza amandikumbira dzenje motsutsana ndi malamulo anu.
86Malamulo anu onse ndi odalirika;
thandizeni, pakuti anthu akundizunza popanda chifukwa.
87Iwo anatsala pangʼono kundichotsa pa dziko lapansi
koma sindinataye malangizo anu.
88Sungani moyo wanga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo ndidzamvera umboni wa pakamwa panu.
Lamedi
89Mawu anu Yehova ndi amuyaya;
akhazikika kumwambako.
90Kukhulupirika kwanu kumakhala mpaka ku mibado yonse;
Inu munakhazikitsa dziko lapansi ndipo lilipobe.
91Malamulo anu alipobe mpaka lero lino,
pakuti zinthu zonse zimatumikira Inu.
92Malamulo anu akanapanda kukhala chikondwerero changa,
ndikanawonongeka mʼmasautso anga.
93Ine sindidzayiwala konse malangizo anu,
pakuti ndi malangizo anuwo munasunga moyo wanga.
94Ndine wanu, ndipulumutseni;
pakuti ndasamala malangizo anu.
95Anthu oyipa akudikira kuti andiwononge,
koma ndidzalingalira umboni wanu.
96Ndadziwa kuti zinthu zonse zili ndi malire,
koma malamulo anu alibe malire konse.
Memu
97Ndithu, ine ndimakonda malamulo anu!
Ndimalingaliramo tsiku lonse.
98Malamulo anu amachititsa kuti ndikhale wanzeru kuposa adani anga,
popeza malamulowo ali ndi ine nthawi zonse.
99Ndimamvetsa zinthu kwambiri kuposa aphunzitsi anga onse
popeza ndimalingalira umboni wanu.
100Ndili ndi nzeru zochuluka zomvetsera zinthu kuposa anthu okalamba,
popeza ndimamvera malangizo anu.
101Ndimaletsa miyendo yanga kuyenda mʼnjira iliyonse yoyipa
kuti ndithe kumvera mawu anu.
102Sindinapatuke kuchoka pa malamulo anu,
pakuti Inu mwini munandiphunzitsa.
103Mawu anu ndi otsekemera ndikawalawa,
otsekemera kuposa uchi mʼkamwa mwanga!
104Ndimapeza nzeru zodziwira zinthu kuchokera mʼmalangizo anu;
kotero ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Nuni
105Mawu anu ndi nyale ya kumapazi kwanga
ndi kuwunika kwa pa njira yanga.
106Ndalumbira ndipo ndatsimikiza,
kuti ndidzatsatira malamulo anu olungama.
107Ndazunzika kwambiri;
Inu Yehova, sungani moyo wanga molingana ndi mawu anu.
108Inu Yehova, landirani matamando aufulu ochokera pakamwa panga,
ndipo ndiphunzitseni malamulo anu.
109Ngakhale moyo wanga umakhala mʼzoopsa nthawi ndi nthawi,
sindidzayiwala malamulo anu.
110Anthu oyipa anditchera msampha,
koma sindinasochere kuchoka pa malangizo anu.
111Umboni wanu ndiye cholowa changa kwamuyaya;
Iwo ndiye chimwemwe cha mtima wanga.
112Mtima wanga wakhazikika pa kusunga zophunzitsa zanu
mpaka kumapeto kwenikweni.
Samekhi
113Ndimadana ndi anthu apawiripawiri,
koma ndimakonda malamulo anu.
114Inu ndinu pothawirapo panga ndi chishango changa;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
115Chokani kwa ine, inu anthu ochita zoyipa,
kuti ndisunge malamulo a Mulungu wanga!
116Mundichirikize molingana ndi lonjezo lanu, ndipo ndidzakhala ndi moyo;
musalole kuti chiyembekezo changa chipite pachabe.
117Gwirizizeni, ndipo ndidzapulumutsidwa;
nthawi zonse ndidzasamalira zophunzitsa zanu.
118Inu mumakana onse amene amasochera kuchoka pa zophunzitsa zanu,
pakuti chinyengo chawo ndi chopanda phindu.
119Anthu onse oyipa a pa dziko lapansi mumawayesa ngati zinthu zakudzala;
nʼchifukwa chake ndimakonda umboni wanu.
120Thupi langa limanjenjemera chifukwa cha kuopa Inu;
ndimachita mantha ndi malamulo anu.
Ayini
121Ndachita zolungama ndi zabwino;
musandisiye mʼmanja mwa ondizunza.
122Onetsetsani kuti mtumiki wanu akukhala bwino,
musalole kuti anthu odzikuza andipondereze.
123Maso anga alefuka, kufunafuna chipulumutso chanu,
kufunafuna lonjezo lanu lolungama.
124Muchite naye mtumiki wanu molingana ndi chikondi chanu chosasinthika,
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
125Ine ndine mtumiki wanu; patseni mzimu wondizindikiritsa,
kuti ndimvetsetse umboni wanu.
126Yehova, ndi nthawi yoti muchitepo kanthu;
malamulo anu akuswedwa.
127Chifukwa choti ndimakonda malamulo anu
kuposa golide, kuposa golide woyengeka bwino,
128ndiponso chifukwa choti ndimaona kuti malangizo anu onse ndi wowongoka,
ndimadana ndi njira iliyonse yoyipa.
Pe
129Maumboni anu ndi odabwitsa
nʼchifukwa chake ndimawamvera.
130Mawu anu akamaphunzitsidwa amapereka kuwunika;
ngakhale anthu wamba amamvetsetsa.
131Ndimatsekula pakamwa panga ndi kupuma wefuwefu,
kufunafuna malamulo anu.
132Tembenukirani kwa ine ndipo mundichitire chifundo,
monga mumachitira nthawi zonse kwa iwo amene amakonda dzina lanu.
133Tsogolerani mayendedwe anga molingana ndi mawu anu;
musalole kuti tchimo lizindilamulira.
134Ndiwomboleni mʼdzanja la anthu ondizunza,
kuti ndithe kumvera malangizo anu.
135Nkhope yanu iwalire mtumiki wanu
ndipo mundiphunzitse malamulo anu.
136Mitsinje ya misozi ikuyenda kuchoka mʼmaso mwanga,
chifukwa anthu sakumvera malamulo anu.
Tsade
137Yehova ndinu wolungama,
ndipo malamulo anu ndi abwino.
138Maumboni amene munatipatsa ndi olungama;
ndi odalirika ndithu.
139Ndikusautsidwa kwambiri mʼkati mwanga
chifukwa adani anu amanyalanyaza mawu anu.
140Mawu anu ndi woyera kwambiri
nʼchifukwa chake mtumiki wanune ndimawakonda.
141Ngakhale ndili wamngʼono ndi wonyozeka,
sindiyiwala malangizo anu.
142Chilungamo chanu nʼchamuyaya,
ndipo malamulo anu nʼchoona.
143Mavuto ndi masautso zandigwera,
koma ndimakondwera ndi malamulo anu.
144Umboni wanu ndi wabwino nthawi zonse;
patseni nzeru zomvetsa zinthu kuti ine ndikhale ndi moyo.
Kofu
145Ndimayitana ndi mtima wanga wonse; ndiyankheni Inu Yehova,
ndipo ndidzamvera zophunzitsa zanu.
146Ndikuyitana kwa Inu; pulumutseni
ndipo ndidzasunga umboni wanu.
147Ndimadzuka tambala asanalire kuti ndipemphe thandizo;
chiyembekezo changa chili mʼmawu anu.
148Maso anga amakhala chipenyere nthawi yonse ya usiku,
kuti ndithe kulingalira malonjezo anu.
149Imvani mawu anga molingana ndi chikondi chanu chosasinthika;
Yehova sungani moyo wanga, molingana ndi malamulo anu.
150Iwo amene amakonza njira zoyipa andiyandikira,
koma ali kutali ndi malamulo anu.
151Koma Inu Yehova muli pafupi,
malamulo anu onse ndi woona.
152Ndinaphunzira kalekale kuchokera mʼmaumboni anu
kuti maumboni amene munakhazikitsawo ndi amuyaya.
Reshi
153Yangʼanani masautso anga ndipo mundipulumutse,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
154Mundiyimirire pa mlandu wanga ndi kundiwombola;
sungani moyo wanga molingana ndi lonjezo lanu.
155Chipulumutso chili kutali ndi anthu oyipa,
pakuti iwowo safunafuna zophunzitsa zanu.
156Chifundo chanu Yehova nʼchachikulu;
sungani moyo wanga molingana ndi malamulo anu.
157Adani amene akundizunza ndi ambiri,
koma ine sindinatembenuke kuchoka pa umboni wanu.
158Ndimawayangʼana monyansidwa anthu opanda chikhulupiriro,
popeza samvera mawu anu.
159Onani momwe ndimakondera malangizo anu;
sungani moyo wanga, Inu Yehova, molingana ndi chikondi chanu chosanthika.
160Mawu anu onse ndi owona;
malamulo anu onse olungama ndi amuyaya.
Sini ndi Shini
161Olamulira amandizunza popanda chifukwa,
koma mtima wanga umanjenjemera ndi mawu anu.
162Ine ndimakondwa ndi lonjezo lanu,
ngati munthu amene wapeza chuma chambiri.
163Ndimadana ndi chinyengo, kwambiri ndimanyansidwa nacho,
koma ndimakonda malamulo anu.
164Ndimakutamandani kasanu ndi kawiri pa tsiku
pakuti malamulo anu ndi olungama.
165Amene amakonda malamulo anu ali ndi mtendere waukulu,
ndipo palibe chimene chingawapunthwitse
166Ndikudikira chipulumutso chanu, Inu Yehova,
ndipo ndimatsatira malamulo anu.
167Ndimamvera umboni wanu
pakuti ndimawukonda kwambiri.
168Ndimamvera malangizo anu ndi umboni wanu,
pakuti njira zanga zonse ndi zodziwika pamaso panu.
Tawu
169Kulira kwanga kufike pamaso panu Yehova;
patseni nzeru zomvetsa zinthu molingana ndi mawu anu.
170Kupempha kwanga kufike pamaso panu;
pulumutseni molingana ndi lonjezo lanu.
171Matamando asefukire pa milomo yanga,
pakuti Inu mumandiphunzitsa malamulo anu.
172Lilime langa liyimbe mawu anu,
popeza malamulo anu onse ndi olungama.
173Dzanja lanu likhale lokonzeka kundithandiza
pakuti ndasankha malangizo anu.
174Ndikufunitsitsa chipulumutso chanu Yehova,
ndipo ndimakondwera ndi malamulo anu.
175Loleni kuti ndikhale ndi moyo kuti ndikutamandeni,
ndipo malamulo anu andichirikize.
176Ndasochera ngati nkhosa yotayika,
funafunani mtumiki wanu,
pakuti sindinayiwale malamulo anu.
Psalm 119119 This psalm is an acrostic poem, the stanzas of which begin with successive letters of the Hebrew alphabet; moreover, the verses of each stanza begin with the same letter of the Hebrew alphabet.
א Aleph
1Blessed are those whose ways are blameless,
who walk according to the law of the Lord.
2Blessed are those who keep his statutes
and seek him with all their heart—
3they do no wrong
but follow his ways.
4You have laid down precepts
that are to be fully obeyed.
5Oh, that my ways were steadfast
in obeying your decrees!
6Then I would not be put to shame
when I consider all your commands.
7I will praise you with an upright heart
as I learn your righteous laws.
8I will obey your decrees;
do not utterly forsake me.
ב Beth
9How can a young person stay on the path of purity?
By living according to your word.
10I seek you with all my heart;
do not let me stray from your commands.
11I have hidden your word in my heart
that I might not sin against you.
12Praise be to you, Lord;
teach me your decrees.
13With my lips I recount
all the laws that come from your mouth.
14I rejoice in following your statutes
as one rejoices in great riches.
15I meditate on your precepts
and consider your ways.
16I delight in your decrees;
I will not neglect your word.
ג Gimel
17Be good to your servant while I live,
that I may obey your word.
18Open my eyes that I may see
wonderful things in your law.
19I am a stranger on earth;
do not hide your commands from me.
20My soul is consumed with longing
for your laws at all times.
21You rebuke the arrogant, who are accursed,
those who stray from your commands.
22Remove from me their scorn and contempt,
for I keep your statutes.
23Though rulers sit together and slander me,
your servant will meditate on your decrees.
24Your statutes are my delight;
they are my counselors.
ד Daleth
25I am laid low in the dust;
preserve my life according to your word.
26I gave an account of my ways and you answered me;
teach me your decrees.
27Cause me to understand the way of your precepts,
that I may meditate on your wonderful deeds.
28My soul is weary with sorrow;
strengthen me according to your word.
29Keep me from deceitful ways;
be gracious to me and teach me your law.
30I have chosen the way of faithfulness;
I have set my heart on your laws.
31I hold fast to your statutes, Lord;
do not let me be put to shame.
32I run in the path of your commands,
for you have broadened my understanding.
ה He
33Teach me, Lord, the way of your decrees,
that I may follow it to the end.119:33 Or follow it for its reward
34Give me understanding, so that I may keep your law
and obey it with all my heart.
35Direct me in the path of your commands,
for there I find delight.
36Turn my heart toward your statutes
and not toward selfish gain.
37Turn my eyes away from worthless things;
preserve my life according to your word.119:37 Two manuscripts of the Masoretic Text and Dead Sea Scrolls; most manuscripts of the Masoretic Text life in your way
38Fulfill your promise to your servant,
so that you may be feared.
39Take away the disgrace I dread,
for your laws are good.
40How I long for your precepts!
In your righteousness preserve my life.
ו Waw
41May your unfailing love come to me, Lord,
your salvation, according to your promise;
42then I can answer anyone who taunts me,
for I trust in your word.
43Never take your word of truth from my mouth,
for I have put my hope in your laws.
44I will always obey your law,
for ever and ever.
45I will walk about in freedom,
for I have sought out your precepts.
46I will speak of your statutes before kings
and will not be put to shame,
47for I delight in your commands
because I love them.
48I reach out for your commands, which I love,
that I may meditate on your decrees.
ז Zayin
49Remember your word to your servant,
for you have given me hope.
50My comfort in my suffering is this:
Your promise preserves my life.
51The arrogant mock me unmercifully,
but I do not turn from your law.
52I remember, Lord, your ancient laws,
and I find comfort in them.
53Indignation grips me because of the wicked,
who have forsaken your law.
54Your decrees are the theme of my song
wherever I lodge.
55In the night, Lord, I remember your name,
that I may keep your law.
56This has been my practice:
I obey your precepts.
ח Heth
57You are my portion, Lord;
I have promised to obey your words.
58I have sought your face with all my heart;
be gracious to me according to your promise.
59I have considered my ways
and have turned my steps to your statutes.
60I will hasten and not delay
to obey your commands.
61Though the wicked bind me with ropes,
I will not forget your law.
62At midnight I rise to give you thanks
for your righteous laws.
63I am a friend to all who fear you,
to all who follow your precepts.
64The earth is filled with your love, Lord;
teach me your decrees.
ט Teth
65Do good to your servant
according to your word, Lord.
66Teach me knowledge and good judgment,
for I trust your commands.
67Before I was afflicted I went astray,
but now I obey your word.
68You are good, and what you do is good;
teach me your decrees.
69Though the arrogant have smeared me with lies,
I keep your precepts with all my heart.
70Their hearts are callous and unfeeling,
but I delight in your law.
71It was good for me to be afflicted
so that I might learn your decrees.
72The law from your mouth is more precious to me
than thousands of pieces of silver and gold.
י Yodh
73Your hands made me and formed me;
give me understanding to learn your commands.
74May those who fear you rejoice when they see me,
for I have put my hope in your word.
75I know, Lord, that your laws are righteous,
and that in faithfulness you have afflicted me.
76May your unfailing love be my comfort,
according to your promise to your servant.
77Let your compassion come to me that I may live,
for your law is my delight.
78May the arrogant be put to shame for wronging me without cause;
but I will meditate on your precepts.
79May those who fear you turn to me,
those who understand your statutes.
80May I wholeheartedly follow your decrees,
that I may not be put to shame.
כ Kaph
81My soul faints with longing for your salvation,
but I have put my hope in your word.
82My eyes fail, looking for your promise;
I say, “When will you comfort me?”
83Though I am like a wineskin in the smoke,
I do not forget your decrees.
84How long must your servant wait?
When will you punish my persecutors?
85The arrogant dig pits to trap me,
contrary to your law.
86All your commands are trustworthy;
help me, for I am being persecuted without cause.
87They almost wiped me from the earth,
but I have not forsaken your precepts.
88In your unfailing love preserve my life,
that I may obey the statutes of your mouth.
ל Lamedh
89Your word, Lord, is eternal;
it stands firm in the heavens.
90Your faithfulness continues through all generations;
you established the earth, and it endures.
91Your laws endure to this day,
for all things serve you.
92If your law had not been my delight,
I would have perished in my affliction.
93I will never forget your precepts,
for by them you have preserved my life.
94Save me, for I am yours;
I have sought out your precepts.
95The wicked are waiting to destroy me,
but I will ponder your statutes.
96To all perfection I see a limit,
but your commands are boundless.
מ Mem
97Oh, how I love your law!
I meditate on it all day long.
98Your commands are always with me
and make me wiser than my enemies.
99I have more insight than all my teachers,
for I meditate on your statutes.
100I have more understanding than the elders,
for I obey your precepts.
101I have kept my feet from every evil path
so that I might obey your word.
102I have not departed from your laws,
for you yourself have taught me.
103How sweet are your words to my taste,
sweeter than honey to my mouth!
104I gain understanding from your precepts;
therefore I hate every wrong path.
נ Nun
105Your word is a lamp for my feet,
a light on my path.
106I have taken an oath and confirmed it,
that I will follow your righteous laws.
107I have suffered much;
preserve my life, Lord, according to your word.
108Accept, Lord, the willing praise of my mouth,
and teach me your laws.
109Though I constantly take my life in my hands,
I will not forget your law.
110The wicked have set a snare for me,
but I have not strayed from your precepts.
111Your statutes are my heritage forever;
they are the joy of my heart.
112My heart is set on keeping your decrees
to the very end.119:112 Or decrees / for their enduring reward
ס Samekh
113I hate double-minded people,
but I love your law.
114You are my refuge and my shield;
I have put my hope in your word.
115Away from me, you evildoers,
that I may keep the commands of my God!
116Sustain me, my God, according to your promise, and I will live;
do not let my hopes be dashed.
117Uphold me, and I will be delivered;
I will always have regard for your decrees.
118You reject all who stray from your decrees,
for their delusions come to nothing.
119All the wicked of the earth you discard like dross;
therefore I love your statutes.
120My flesh trembles in fear of you;
I stand in awe of your laws.
ע Ayin
121I have done what is righteous and just;
do not leave me to my oppressors.
122Ensure your servant’s well-being;
do not let the arrogant oppress me.
123My eyes fail, looking for your salvation,
looking for your righteous promise.
124Deal with your servant according to your love
and teach me your decrees.
125I am your servant; give me discernment
that I may understand your statutes.
126It is time for you to act, Lord;
your law is being broken.
127Because I love your commands
more than gold, more than pure gold,
128and because I consider all your precepts right,
I hate every wrong path.
פ Pe
129Your statutes are wonderful;
therefore I obey them.
130The unfolding of your words gives light;
it gives understanding to the simple.
131I open my mouth and pant,
longing for your commands.
132Turn to me and have mercy on me,
as you always do to those who love your name.
133Direct my footsteps according to your word;
let no sin rule over me.
134Redeem me from human oppression,
that I may obey your precepts.
135Make your face shine on your servant
and teach me your decrees.
136Streams of tears flow from my eyes,
for your law is not obeyed.
צ Tsadhe
137You are righteous, Lord,
and your laws are right.
138The statutes you have laid down are righteous;
they are fully trustworthy.
139My zeal wears me out,
for my enemies ignore your words.
140Your promises have been thoroughly tested,
and your servant loves them.
141Though I am lowly and despised,
I do not forget your precepts.
142Your righteousness is everlasting
and your law is true.
143Trouble and distress have come upon me,
but your commands give me delight.
144Your statutes are always righteous;
give me understanding that I may live.
ק Qoph
145I call with all my heart; answer me, Lord,
and I will obey your decrees.
146I call out to you; save me
and I will keep your statutes.
147I rise before dawn and cry for help;
I have put my hope in your word.
148My eyes stay open through the watches of the night,
that I may meditate on your promises.
149Hear my voice in accordance with your love;
preserve my life, Lord, according to your laws.
150Those who devise wicked schemes are near,
but they are far from your law.
151Yet you are near, Lord,
and all your commands are true.
152Long ago I learned from your statutes
that you established them to last forever.
ר Resh
153Look on my suffering and deliver me,
for I have not forgotten your law.
154Defend my cause and redeem me;
preserve my life according to your promise.
155Salvation is far from the wicked,
for they do not seek out your decrees.
156Your compassion, Lord, is great;
preserve my life according to your laws.
157Many are the foes who persecute me,
but I have not turned from your statutes.
158I look on the faithless with loathing,
for they do not obey your word.
159See how I love your precepts;
preserve my life, Lord, in accordance with your love.
160All your words are true;
all your righteous laws are eternal.
ש Sin and Shin
161Rulers persecute me without cause,
but my heart trembles at your word.
162I rejoice in your promise
like one who finds great spoil.
163I hate and detest falsehood
but I love your law.
164Seven times a day I praise you
for your righteous laws.
165Great peace have those who love your law,
and nothing can make them stumble.
166I wait for your salvation, Lord,
and I follow your commands.
167I obey your statutes,
for I love them greatly.
168I obey your precepts and your statutes,
for all my ways are known to you.
ת Taw
169May my cry come before you, Lord;
give me understanding according to your word.
170May my supplication come before you;
deliver me according to your promise.
171May my lips overflow with praise,
for you teach me your decrees.
172May my tongue sing of your word,
for all your commands are righteous.
173May your hand be ready to help me,
for I have chosen your precepts.
174I long for your salvation, Lord,
and your law gives me delight.
175Let me live that I may praise you,
and may your laws sustain me.
176I have strayed like a lost sheep.
Seek your servant,
for I have not forgotten your commands.