Masalimo 120 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 120:1-7

Salimo 120

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Ndimafuwulira kwa Yehova mʼmasautso anga,

ndipo Iye amandiyankha.

2Pulumutseni Yehova ku milomo yabodza,

ndi kwa anthu achinyengo.

3Kodi adzakuchitani chiyani,

ndipo adzawonjezerapo zotani, inu anthu achinyengo?

4Adzakulangani ndi mivi yakuthwa ya munthu wankhondo,

ndi makala oyaka a mtengo wa tsanya.

5Tsoka ine kuti ndimakhala ku Mesaki,

kuti ndimakhala pakati pa matenti a ku Kedara!

6Kwa nthawi yayitali ndakhala pakati

pa iwo amene amadana ndi mtendere.

7Ine ndine munthu wamtendere;

koma ndikamayankhula, iwo amafuna nkhondo.

New International Version

Psalms 120:1-7

Psalm 120

A song of ascents.

1I call on the Lord in my distress,

and he answers me.

2Save me, Lord,

from lying lips

and from deceitful tongues.

3What will he do to you,

and what more besides,

you deceitful tongue?

4He will punish you with a warrior’s sharp arrows,

with burning coals of the broom bush.

5Woe to me that I dwell in Meshek,

that I live among the tents of Kedar!

6Too long have I lived

among those who hate peace.

7I am for peace;

but when I speak, they are for war.