Salimo 111
1Tamandani Yehova.
Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse
mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;
onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,
ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;
amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,
kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;
malangizo ake onse ndi odalirika.
8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,
ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9Iyeyo amawombola anthu ake;
anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya
dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;
onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.
Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Psalm 111This psalm is an acrostic poem, the lines of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.
1Praise the Lord.111:1 Hebrew Hallelu Yah
I will extol the Lord with all my heart
in the council of the upright and in the assembly.
2Great are the works of the Lord;
they are pondered by all who delight in them.
3Glorious and majestic are his deeds,
and his righteousness endures forever.
4He has caused his wonders to be remembered;
the Lord is gracious and compassionate.
5He provides food for those who fear him;
he remembers his covenant forever.
6He has shown his people the power of his works,
giving them the lands of other nations.
7The works of his hands are faithful and just;
all his precepts are trustworthy.
8They are established for ever and ever,
enacted in faithfulness and uprightness.
9He provided redemption for his people;
he ordained his covenant forever—
holy and awesome is his name.
10The fear of the Lord is the beginning of wisdom;
all who follow his precepts have good understanding.
To him belongs eternal praise.