Masalimo 111 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 111:1-10

Salimo 111

1Tamandani Yehova.

Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse

mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.

2Ntchito za Yehova nʼzazikulu;

onse amene amakondwera nazo amazilingalira.

3Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu,

ndipo chilungamo chake ndi chosatha.

4Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike;

Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.

5Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye;

amakumbukira pangano lake kwamuyaya.

6Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake,

kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.

7Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama;

malangizo ake onse ndi odalirika.

8Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi,

ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.

9Iyeyo amawombola anthu ake;

anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya

dzina lake ndi loyera ndi loopsa.

10Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru;

onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu.

Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

New International Version

Psalms 111:1-10

Psalm 111This psalm is an acrostic poem, the lines of which begin with the successive letters of the Hebrew alphabet.

1Praise the Lord.111:1 Hebrew Hallelu Yah

I will extol the Lord with all my heart

in the council of the upright and in the assembly.

2Great are the works of the Lord;

they are pondered by all who delight in them.

3Glorious and majestic are his deeds,

and his righteousness endures forever.

4He has caused his wonders to be remembered;

the Lord is gracious and compassionate.

5He provides food for those who fear him;

he remembers his covenant forever.

6He has shown his people the power of his works,

giving them the lands of other nations.

7The works of his hands are faithful and just;

all his precepts are trustworthy.

8They are established for ever and ever,

enacted in faithfulness and uprightness.

9He provided redemption for his people;

he ordained his covenant forever—

holy and awesome is his name.

10The fear of the Lord is the beginning of wisdom;

all who follow his precepts have good understanding.

To him belongs eternal praise.