Masalimo 110 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 110:1-7

Salimo 110

Salimo la Davide.

1Yehova akuwuza Mbuye wanga kuti,

“Khala ku dzanja langa lamanja

mpaka nditasandutsa adani ako

kukhala chopondapo mapazi ako.”

2Yehova adzakuza ndodo yamphamvu ya ufumu wako kuchokera mʼZiyoni;

udzalamulira pakati pa adani ako.

3Ankhondo ako adzakhala odzipereka

pa tsiku lako la nkhondo.

Atavala chiyero chaulemerero,

kuchokera mʼmimba ya mʼbandakucha,

udzalandira mame a unyamata wako.

4Yehova walumbira

ndipo sadzasintha maganizo ake:

“Ndiwe wansembe mpaka muyaya

monga mwa unsembe wa Melikizedeki.”

5Ambuye ali kudzanja lako lamanja;

Iye adzaponda mafumu pa tsiku la ukali wake.

6Adzaweruza anthu a mitundu ina,

adzadzaza dziko lapansi ndi mitembo ndipo adzaphwanya olamulira a pa dziko lonse lapansi.

7Iye adzamwa mu mtsinje wa mʼmbali mwa njira;

choncho adzaweramutsa mutu wake.

New International Version

Psalms 110:1-7

Psalm 110

Of David. A psalm.

1The Lord says to my lord:110:1 Or Lord

“Sit at my right hand

until I make your enemies

a footstool for your feet.”

2The Lord will extend your mighty scepter from Zion, saying,

“Rule in the midst of your enemies!”

3Your troops will be willing

on your day of battle.

Arrayed in holy splendor,

your young men will come to you

like dew from the morning’s womb.110:3 The meaning of the Hebrew for this sentence is uncertain.

4The Lord has sworn

and will not change his mind:

“You are a priest forever,

in the order of Melchizedek.”

5The Lord is at your right hand110:5 Or My lord is at your right hand, Lord;

he will crush kings on the day of his wrath.

6He will judge the nations, heaping up the dead

and crushing the rulers of the whole earth.

7He will drink from a brook along the way,110:7 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.

and so he will lift his head high.