Masalimo 108 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 108:1-13

Salimo 108

Nyimbo. Salimo la Davide.

1Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu;

ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.

2Dzukani, zeze ndi pangwe!

Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.

3Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.

4Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba;

kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.

5Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba,

ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.

6Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

7Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.

8Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.

9Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo

ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu;

ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”

10Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

11Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana

ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?

12Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani,

pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.

13Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano,

ndipo adzapondereza pansi adani athu.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 108:1-14

Hjælp mod fjenden

1En sang af David.

2Jeg er fuld af tillid til dig, Gud,

jeg vil synge og spille til din ære.

3Jeg vil gribe min harpe og lyre,

når befrielsens sol står op.108,3 Mere ordret: „Rejs dig ved morgenrøden.” Da solens lys driver nattens mørke på flugt, er morgenrøden et billede på det øjeblik, befrielsen kommer.

4Jeg vil takke dig, Herre, blandt folkeslagene,

jeg vil synge din pris for de fremmede.

5Din trofasthed fylder universet,

din godhed når til skyerne.

6Herre, lad din storhed fylde himmelrummet,

lad din herlighed komme over hele jorden.

7Hør min bøn og gør brug af din magt,

så dit elskede folk kan blive reddet.

8Gud har talt fra sin helligdom:

„Med glæde vil jeg udstykke Sikem,

jeg vil udmåle Sukkots dal.

9Gilead tilhører mig,

Manasse er min ejendom.

Kongerne kommer fra Juda,

og dygtige krigere fra Efraim.

10Moabitterne skal tjene mig

og edomitterne være mine slaver.

Jeg vinder sejr over filistrene.”

11Hvem tager med os til den befæstede by?

Hvem vil gå med os mod Edom?

12Herre, har du forkastet os?

Hvorfor drager du ikke med os i krig?

13Hjælp os dog mod vore fjender,

for menneskers hjælp er intet værd.

14Med Guds hjælp vinder vi sejr,

for han vil trampe vore fjender ned.