Masalimo 107 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 107:1-43

BUKU LACHISANU

Masalimo 107–150

Salimo 107

1Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino;

pakuti chikondi chake ndi chosatha.

2Owomboledwa a Yehova anene zimenezi

amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,

3iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko,

kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.

4Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu,

osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.

5Iwo anamva njala ndi ludzu,

ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.

6Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

7Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka

kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.

8Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

9pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu

ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.

10Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu,

amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,

11pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu

ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.

12Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga;

anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.

13Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.

14Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu

ndipo anadula maunyolo awo.

15Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,

16pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa

ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.

17Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira,

ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.

18Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse

ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.

19Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.

20Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa;

anawalanditsa ku manda.

21Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

22Apereke nsembe yachiyamiko

ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.

23Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi;

Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.

24Anaona ntchito za Yehova,

machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.

25Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho

imene inabweretsa mafunde ataliatali.

26Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya;

pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.

27Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera;

anali pa mapeto a moyo wawo.

28Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo

ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.

29Yehova analetsa namondwe,

mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.

30Anali osangalala pamene kunakhala bata,

ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.

31Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha

ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.

32Akuze Iye mu msonkhano wa anthu

ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.

33Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu,

akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,

34ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere,

chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.

35Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi

ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;

36kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako,

ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.

37Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa

ndipo anakolola zipatso zochuluka;

38Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri,

ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.

39Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa

chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;

40Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka

anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.

41Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo

ngati magulu a nkhosa.

42Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala,

koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.

43Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi

ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 107:1-43

Herrens trofasthed mod sit folk

1Tak Herren, for han er god.

Hans trofasthed varer til evig tid.

2Det er, hvad Herrens folk bør sige,

dem, han befriede fra fjendens magt

3og bragte tilbage fra fjerne lande,

fra øst og vest og syd og nord.

4De måtte vandre længe gennem øde egne,

de ledte efter et sted at bo.

5De var udmattede af sult og tørst

og nær ved at give op.

6Men i deres nød råbte de til Herren,

og han reddede dem ud af problemerne.

7Han førte dem ad den rigtige vej

til en by, hvor de kunne bosætte sig.

8De bør takke Herren for hans trofasthed,

for de undere, han gør for menneskene.

9Han slukkede de udmattedes tørst,

og han mættede de sultne med gode gaver.

10De sad i et trøstesløst mørke

og led under deres fangenskab,

11fordi de havde gjort oprør mod Gud,

ringeagtet den Højestes bud.

12Han nedbrød deres stolthed gennem lidelser,

når de segnede, hjalp ingen dem op.

13Men i deres nød råbte de til Herren,

og han reddede dem ud af problemerne.

14Han førte dem ud af mørket

og rev deres lænker i stykker.

15De bør takke Herren for hans trofasthed,

for de undere, han gør for menneskene.

16Han sprængte porte af bronze

og huggede gennem slåer af jern.

17De blev mishandlet og betragtet som tåber

på grund af deres synd og oprør mod Gud.

18De mistede appetitten og fik kvalme af maden,

de var døden nær af sult.

19Men i deres nød råbte de til Herren,

og han reddede dem ud af problemerne.

20Han sagde blot et ord, og de blev reddet,

han rev dem ud af dødens gab.

21De bør takke Herren for hans trofasthed,

for de undere han gør for menneskene.

22Lad dem bringe ham ofre i taknemmelighed,

synge med glæde om hans vældige gerninger.

23Nogle stod til søs med deres skibe,

drev handel på det store hav.

24Også de fik Herrens gerninger at se,

de undere han udførte på havet.

25Han befalede stormvejret at bryde løs,

bølgerne rejste sig som bjerge.

26De steg mod himlen, sank atter ned i dybet.

Sømændene var ved at give op over for orkanen.

27De ravede rundt som fulde folk,

de kunne intet stille op.

28Men i deres nød råbte de til Herren,

og han reddede dem ud af problemerne.

29Stormen blev stille som en hvisken,

havets bølger faldt hurtigt til ro.

30Da fyldtes de af fred, åndede lettet op,

og han førte dem til deres rejses mål.

31De bør takke Herren for hans trofasthed,

for de undere, han gør for menneskene,

32ophøje ham offentligt i folkets forsamling

og for landets ledende råd.

33Han forvandlede floder til ødemark,

gjorde kildevand til ørkensand.

34Frugtbart land blev til saltsletter

på grund af beboernes ondskab.

35Men derefter gjorde han ørkenen til oase

og ødemarken til frugtbart land,

36så hans sultende folk kunne slå sig ned

og bygge byer, hvor de kunne bo,

37tilså deres marker, plante vingårde

og bringe en bugnende høst i hus.

38Han velsignede dem, de blev mange,

og der var ingen mangel på kvæg.

39Det oprørske folk blev ydmyget gennem sorg og ulykker,

mange døde, så de blev færre og færre.

40Gud måtte straffe de stolte, religiøse ledere,

lade dem flakke om i øde egne.

41Men de, der søgte hjælp hos Herren,

blev reddet ud af deres ulykke.

Han tog sig af dem,

så de trivedes og havde fremgang.

42De retskafne glæder sig over at se det,

men de onde holder skamfuldt deres mund.

43De vise vil lægge mærke til det

og anerkende Herrens trofasthed.