Masalimo 105 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 105:1-45

Salimo 105

1Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.

2Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo;

fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.

3Munyadire dzina lake loyera;

mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.

4Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi yonse.

5Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita,

zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,

6inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhika ake.

7Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.

8Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya,

mawu amene analamula kwa mibado yonse,

9pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu,

lumbiro limene analumbira kwa Isake.

10Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya:

11“Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani

ngati gawo la cholowa chako.”

12Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero,

ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,

13ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina,

kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.

14Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza;

anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:

15“Musakhudze odzozedwa anga;

musachitire choyipa aneneri anga.”

16Iye anabweretsa njala pa dziko

ndipo anawononga chakudya chonse;

17Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo,

Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.

18Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza,

khosi lake analiyika mʼzitsulo,

19mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa,

mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.

20Mfumu inatuma munthu kukamumasula,

wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.

21Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake,

wolamulira zonse zimene iye anali nazo,

22kulangiza ana a mfumu monga ankafunira

ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.

23Tsono Israeli analowa mu Igupto;

Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.

24Yehova anachulukitsa anthu ake;

ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;

25amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake,

kukonzera chiwembu atumiki ake.

26Yehova anatuma Mose mtumiki wake,

ndi Aaroni amene Iye anamusankha.

27Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo,

zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.

28Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima.

Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.

29Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi,

kuchititsa kuti nsomba zawo zife.

30Dziko lawo linadzaza ndi achule

amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.

31Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka

ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.

32Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala,

ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;

33Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu,

nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.

34Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera,

ziwala zosawerengeka;

35zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo,

zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.

36Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo,

zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.

37Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri,

ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.

38Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka,

pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.

39Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo,

ndi moto owawunikira usiku.

40Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri

ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.

41Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka;

ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.

42Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene

linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.

43Iye anatulutsa anthu ake akukondwera,

osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;

44Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina

ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,

45kuti iwo asunge malangizo ake

ndi kutsatira malamulo ake.

Tamandani Yehova.

New International Reader’s Version

Psalm 105:1-45

Psalm 105

1Give praise to the Lord and announce who he is.

Tell the nations what he has done.

2Sing to him, sing praise to him.

Tell about all the wonderful things he has done.

3Praise him, because his name is holy.

Let the hearts of those who trust in the Lord be glad.

4Seek the Lord and the strength he gives.

Always seek him.

5Remember the wonderful things he has done.

Remember his miracles and how he judged our enemies.

6Remember what he has done, you children of his servant Abraham.

Remember it, you people of Jacob, God’s chosen ones.

7He is the Lord our God.

He judges the whole earth.

8He will keep his covenant forever.

He will keep his promise for all time to come.

9He will keep the covenant he made with Abraham.

He will keep the promise he made to Isaac.

10He made it stand as a law for Jacob.

He made it stand as a covenant for Israel that will last forever.

11He said, “I will give you the land of Canaan.

It will belong to you.”

12At first there weren’t very many of God’s people.

There were only a few, and they were strangers in the land.

13They wandered from nation to nation.

They wandered from one kingdom to another.

14But God didn’t allow anyone to treat them badly.

To keep them safe, he gave a command to kings.

15He said to them, “Do not touch my anointed ones.

Do not harm my prophets.”

16He made the people in the land go hungry.

He destroyed all their food supplies.

17He sent a man ahead of them into Egypt.

That man was Joseph. He had been sold as a slave.

18The Egyptians put his feet in chains.

They put an iron collar around his neck.

19He was in prison until what he said would happen came true.

The word of the Lord proved that he was right.

20The king of Egypt sent for Joseph and let him out of prison.

The ruler of many nations set him free.

21He put Joseph in charge of his palace.

He made him ruler over everything he owned.

22Joseph was in charge of teaching the princes.

He taught the elders how to think and live wisely.

23Then the rest of Jacob’s family went to Egypt.

The people of Israel lived as outsiders in the land of Ham.

24The Lord gave his people so many children

that there were too many of them for their enemies.

25He made the Egyptians hate his people.

The Egyptians made evil plans against them.

26The Lord sent his servant Moses to the king of Egypt.

He sent Aaron, his chosen one, along with him.

27The Lord gave them the power to do signs among the Egyptians.

They did his wonders in the land of Ham.

28The Lord sent darkness over the land.

He did it because the Egyptians had refused to obey his words.

29He turned their rivers and streams into blood.

He caused the fish in them to die.

30Their land was covered with frogs.

Frogs even went into the bedrooms of the rulers.

31The Lord spoke, and large numbers of flies came.

Gnats filled the whole country.

32He turned their rain into hail.

Lightning flashed all through their land.

33He destroyed their vines and fig trees.

He broke down the trees in Egypt.

34He spoke, and the locusts came.

There were so many of them they couldn’t be counted.

35They ate up every green thing in the land.

They ate up what the land produced.

36Then he killed the oldest son of every family in Egypt.

He struck down the oldest of all their sons.

37He brought the people of Israel out of Egypt.

The Egyptians loaded them down with silver and gold.

From among the tribes of Israel no one got tired or fell down.

38The Egyptians were glad when the people of Israel left.

They were terrified because of Israel.

39The Lord spread out a cloud to cover his people.

He gave them a fire to light up the night.

40They asked for meat, and he brought them quail.

He fed them well with manna, the bread of heaven.

41He broke open a rock, and streams of water poured out.

They flowed like a river in the desert.

42He remembered the holy promise

he had made to his servant Abraham.

43His chosen people shouted for joy

as he brought them out of Egypt.

44He gave them the lands of other nations.

He let them take over what others had worked for.

45He did it so they might obey his rules

and follow his laws.

Praise the Lord.