Masalimo 104 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 104:1-35

Salimo 104

1Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.

Inu Yehova Mulungu wanga, ndinu wamkulu kwambiri;

mwavala ulemerero ndi ufumu.

2Iye wadzifunditsa kuwala ngati chovala;

watambasula miyamba ngati tenti

3ndipo wayika pa madzi mitanda ya chipinda chake.

Iye amasandutsa mitambo kukhala galeta lake,

ndi kuwuluka pa mapiko a mphepo.

4Amapanga mphepo kukhala amithenga ake,

malawi amoto kukhala atumiki ake.

5Anakhazikitsa dziko lapansi pa maziko ake;

silingasunthike.

6Munaliphimba ndi nyanja yozama ngati chovala;

madzi anayimirira pamwamba pa mapiri.

7Koma pakudzudzula kwanu madzi anathawa,

pa mkokomo wa bingu lanu iwo anamwazika;

8Inu munamiza mapiri,

iwo anatsikira ku zigwa

kumalo kumene munawakonzera.

9Inu munayika malire ndipo sangathe kudutsa,

iwo sadzamizanso dziko lapansi.

10Iye achititsa akasupe kutulutsa madzi kupita ku zigwa;

madziwo amayenda pakati pa mapiri.

11Iwo amapereka madzi kwa zirombo zonse zakuthengo;

abulu akuthengo amapha ludzu lawo.

12Mbalame zamlengalenga zimayika zisa mʼmbali mwa madzi;

zimayimba pakati pa thambo.

13Iye amathirira mapiri kuchokera ku zipinda zake zapamwamba;

dziko lapansi limakhutitsidwa ndi chipatso cha ntchito yake.

14Amameretsa udzu kuti ngʼombe zidye,

ndi zomera, kuti munthu azilima

kubweretsa chakudya kuchokera mʼdziko lapansi:

15vinyo amene amasangalatsa mtima wa munthu,

mafuta amene amachititsa nkhope yake kuwala,

ndi buledi amene amapereka mphamvu.

16Mitengo ya Yehova ndi yothiriridwa bwino,

mikungudza ya ku Lebanoni imene Iye anadzala.

17Mbalame zimamanga zisa zawo;

kakowa ali ndi malo ake mʼmikungudzamo.

18Mapiri ataliatali ndi a mbalale;

mʼmingʼalu ya miyala ndi mobisalamo mbira.

19Mwezi umasiyanitsa nyengo

ndipo dzuwa limadziwa nthawi yake yolowera.

20Inu mumabweretsa mdima nukhala usiku,

ndipo zirombo zonse za ku nkhalango zimatuluka.

21Mikango imabangula kufuna nyama,

ndi kufunafuna chakudya chawo kuchokera kwa Mulungu.

22Dzuwa limatuluka ndipo iyo imapita kukabisala;

imabwerera kukagona pansi mʼmapanga awo.

23Pamenepo munthu amapita ku ntchito yake,

kukagwira ntchito yake mpaka madzulo.

24Ntchito zanu ndi zochulukadi Inu Yehova!

Munazipanga zonse mwanzeru,

dziko lapansi ladzaza ndi zolengedwa zanu.

25Kuli nyanja yayikulu ndi yotambalala,

yodzaza ndi zolengedwa zosawerengeka,

zamoyo zanu zazikulu ndi zazingʼono zomwe.

26Kumeneko sitima zapamadzi zimayenda uku ndi uku,

ndiponso Leviyatani amene munamulenga kuti asewere kumeneko.

27Zonsezi zimayangʼana kwa Inu

kuti muzipatse chakudya chawo pa nthawi yake yoyenera.

28Mukazipatsa,

zimachisonkhanitsa pamodzi;

mukatsekula dzanja lanu,

izo zimakhutitsidwa ndi zinthu zabwino.

29Mukabisa nkhope yanu,

izo zimachita mantha aakulu;

mukachotsa mpweya wawo,

zimafa ndi kubwerera ku fumbi.

30Mukatumiza mzimu wanu,

izo zimalengedwa

ndipo mumakozanso maonekedwe a dziko lapansi.

31Ulemerero wa Yehova ukhalebe mpaka muyaya;

Yehova akondwere ndi ntchito ya manja ake;

32Iye amene amayangʼana dziko lapansi ndipo limanjenjemera,

amene amakhudza mapiri ndipo amatuluka utsi.

33Ine ndidzayimbira Yehova moyo wanga wonse;

ndidzayimbira matamando Mulungu wanga nthawi yonse imene ndili ndi moyo.

34Zolingalira zanga zikhale zomukomera Iye,

pamene ndikusangalala mwa Yehova.

35Koma anthu ochimwa awonongeke pa dziko lapansi

ndipo anthu oyipa asapezekenso.

Tamanda Yehova, Iwe moyo wanga.

Tamandani Yehova.

New International Reader’s Version

Psalm 104:1-35

Psalm 104

1I will praise the Lord.

Lord my God, you are very great.

You are dressed in glory and majesty.

2The Lord wraps himself in light as if it were a robe.

He spreads out the heavens like a tent.

3He builds his palace high in the heavens.

He makes the clouds serve as his chariot.

He rides on the wings of the wind.

4He makes the winds serve as his messengers.

He makes flashes of lightning serve him.

5He placed the earth on its foundations.

It can never be moved.

6You, Lord, covered it with the oceans like a blanket.

The waters covered the mountains.

7But you commanded the waters, and they ran away.

At the sound of your thunder they rushed off.

8They flowed down the mountains.

They went into the valleys.

They went to the place you appointed for them.

9You drew a line they can’t cross.

They will never cover the earth again.

10The Lord makes springs pour water into the valleys.

It flows between the mountains.

11The springs give water to all the wild animals.

The wild donkeys satisfy their thirst.

12The birds in the sky build nests by the waters.

They sing among the branches.

13The Lord waters the mountains from his palace high in the clouds.

The earth is filled with the things he has made.

14He makes grass grow for the cattle

and plants for people to take care of.

That’s how they get food from the earth.

15There is wine to make people glad.

There is olive oil to make their skin glow.

And there is bread to make them strong.

16The cedar trees of Lebanon belong to the Lord.

He planted them and gave them plenty of water.

17There the birds make their nests.

The stork has its home in the juniper trees.

18The high mountains belong to the wild goats.

The cliffs are a safe place for the rock badgers.

19The Lord made the moon to mark off the seasons.

The sun knows when to go down.

20You, Lord, bring darkness, and it becomes night.

Then all the animals of the forest prowl around.

21The lions roar while they hunt.

All their food comes from God.

22The sun rises, and they slip away.

They return to their dens and lie down.

23Then people get up and go to work.

They keep working until evening.

24Lord, you have made so many things!

How wise you were when you made all of them!

The earth is full of your creatures.

25Look at the ocean, so big and wide!

It is filled with more creatures than people can count.

It is filled with living things, from the largest to the smallest.

26Ships sail back and forth on it.

Leviathan, the sea monster you made, plays in it.

27All creatures depend on you

to give them their food when they need it.

28When you give it to them,

they eat it.

When you open your hand,

they are satisfied with good things.

29When you turn your face away from them,

they are terrified.

When you take away their breath,

they die and turn back into dust.

30When you send your Spirit,

you create them.

You give new life to the ground.

31May the glory of the Lord continue forever.

May the Lord be happy with what he has made.

32When he looks at the earth, it trembles.

When he touches the mountains, they pour out smoke.

33I will sing to the Lord all my life.

I will sing praise to my God as long as I live.

34May these thoughts of mine please him.

I find my joy in the Lord.

35But may sinners be gone from the earth.

May evil people disappear.

I will praise the Lord.

Praise the Lord.