Marko 9 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 9:1-50

1Ndipo anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti ena amene ayimirira pano sadzafa asanaone ufumu wa Mulungu ukubwera mwa mphamvu.”

Maonekedwe a Ulemerero wa Yesu pa Phiri

2Patatha masiku asanu ndi limodzi Yesu anatenga Petro, Yakobo ndi Yohane nawatsogolera kupita ku phiri lalitali, kumene anali okhaokha. Kumeneko maonekedwe ake anasinthika pamaso pawo. 3Zovala zake zinawala monyezimira kwambiri, kotero kuti palibe sopo wina aliyense amene angaziyeretse monyezimira chotere pa dziko la pansi. 4Ndipo anaonekera Eliya ndi Mose pamaso pawo, amene ankayankhulana ndi Yesu.

5Petro anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, ndi kwabwino kuti ife tili pano. Tiyeni timange misasa itatu; umodzi wanu, wina wa Mose ndi wina wa Eliya.” 6(Iye sanadziwe choti anene, anali ndi mantha akulu).

7Pamenepo mtambo unaoneka ndi kuwaphimba, ndipo mawu anamveka kuchokera mu mtambo kuti, “Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa. Mvereni Iye!”

8Mwadzidzidzi, atayangʼanayangʼana, sanaonenso wina aliyense ali ndi iwo kupatula Yesu.

9Pamene ankatsika kuchokera ku phiri, Yesu anawalamulira kuti asawuze aliyense zimene anaona mpaka Mwana wa Munthu atauka kwa akufa. 10Iwo anayisunga nkhaniyo nakambirana za tanthauzo lake la “Kuuka kwa akufa.”

11Ndipo anamufunsa Iye kuti, “Nʼchifukwa chiyani aphunzitsi amalamulo amati Eliya ayenera kuyamba wabwera?”

12Yesu anayankha kuti, “Kunena motsimikiza, Eliya ayeneradi kuyamba kubwera kudzakonzanso zinthu zonse. Nʼchifukwa chiyani tsono zinalembedwa, kuti Mwana wa Munthu ayenera kuvutika kwambiri ndi kukanidwa? 13Koma ndikuwuzani, kuti Eliya wabweradi, ndipo amuchitira iye zonse zimene iwo anafuna, monga momwe zalembedwera za iye.”

Kuchiritsidwa kwa Mnyamata Wogwidwa ndi Mzimu Woyipa

14Atafika kwa ophunzira ena aja, anaona gulu lalikulu la anthu litawazungulira ndi aphunzitsi amalamulo akutsutsana nawo. 15Nthawi yomweyo anthu onse atamuona, anadabwa kwambiri ndipo anathamanga kukamulonjera.

16Iye anafunsa kuti, “Mukukangana nawo chiyani iwowa?”

17Munthu wina mʼgululo anayankha kuti, “Aphunzitsi, ndinakubweretserani mwana wanga wamwamuna, amene ndi ogwidwa ndi mzimu umene umamulepheretsa kuyankhula. 18Nthawi iliyonse ukamugwira umamugwetsa pansi. Amatuluka thovu kukamwa, amakukuta mano ake ndipo amawuma. Ndinapempha ophunzira anu kuti awutulutse mzimuwo, koma sanathe.”

19Yesu anayankha kuti, “Haa! Mʼbado osakhulupirira, kodi ndidzakhala nanu mpaka liti? Mubweretseni kwa Ine mnyamatayo.”

20Ndipo anamubweretsa kwa Iye. Mzimu woyipawo utaona Yesu, nthawi yomweyo unamukomola mnyamatayo. Anagwa pansi ndi kumagubuduka, ndi kuchita thovu kukamwa.

21Yesu anafunsa abambo a mnyamatayo kuti, “Kodi wakhala chotere nthawi yayitali bwanji?”

Iye anayankha kuti, “Kuyambira ali wamngʼono, 22wakhala ukumuponya pa moto kapena mʼmadzi kuti umuphe. Koma ngati mungathe kuchita kanthu, tichitireni chifundo ndipo mutithandize.”

23Yesu anati, “ ‘Ngati mungathe!’ Zinthu zonse ndi zotheka kwa iye amene akhulupirira.”

24Nthawi yomweyo abambo a mwanayo anafuwula kuti, “Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga!”

25Yesu ataona kuti gulu la anthu likuthamangira kumalowo, anadzudzula mzimu woyipawo kuti, “Iwe mzimu wolepheretsa kuyankhula ndi kumva, ndikulamulira tuluka mwa iye ndipo usadzalowenso.”

26Mzimuwo unafuwula ndi kumugubuduza kwambiri ndipo unatuluka. Mnyamatayo anaoneka ngati mtembo ndipo ambiri anati, “Wafa.” 27Koma Yesu anamugwira dzanja ndipo anamuyimiritsa, ndipo anayimirira.

28Yesu atalowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa ali pa okha kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani ife sitinathe kutulutsa chiwandacho?”

29Iye anayankha kuti, “Mtundu uwu umatuluka pokhapokha mwapemphera ndi kusala kudya.”

Yesu aneneratu za Imfa yake Kachiwiri

30Anachoka malo amenewo nadutsa ku Galileya. Yesu sanafune kuti wina aliyense adziwe kumene anali, 31chifukwa amaphunzitsa ophunzira ake. Anati kwa iwo, “Mwana wa Munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu. Adzamupha, ndipo patatha masiku atatu adzauka.” 32Koma sanazindikire chimene amatanthauza, ndipo anachita mantha kuti amufunse.

Wamkulu Ndani mu Ufumu wa Mulungu?

33Anafika ku Kaperenawo. Pamene anali mʼnyumba, anawafunsa kuti, “Kodi mumatsutsana chiyani mʼnjira muja?” 34Koma anakhala chete chifukwa ali mʼnjira amatsutsana za kuti wamkulu kuposa onse ndani.

35Atakhala pansi, Yesu anayitana khumi ndi awiriwo nati, “Ngati wina aliyense afuna kukhala woyamba, ayenera kukhala wotsiriza ndi wotumikira onse.”

36Anatenga kamwana nakayimiritsa pakati pawo ndipo anawawuza kuti, 37“Aliyense wolandira mmodzi wa ana angʼono awa mʼdzina langa alandira Ine; ndipo aliyense wolandira Ine salandira Ine koma amene anandituma.”

Wosatsutsana Nafe Athandizana Nafe

38Yohane anati, “Aphunzitsi, tinaona munthu akutulutsa ziwanda mʼdzina lanu ndipo ife tinamuwuza kuti aleke, chifukwa sanali mmodzi wa ife.”

39Yesu anati, “Musamuletse, palibe amene amachita chodabwitsa mʼdzina langa ndipo kenaka nanena zoyipa za Ine, 40pakuti aliyense amene satsutsana nafe ali mbali yathu. 41Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene akupatsani chikho cha madzi mʼdzina langa chifukwa ndinu ake a Khristu, sadzataya konse mphotho yake.”

Zochimwitsa Ena

42“Ndipo ngati wina aliyense achimwitsa mmodzi wa ana angʼono awa amene akhulupirira Ine, kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala waukulu mʼkhosi mwake. 43Ngati dzanja lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo ndi dzanja limodzi kusiyana ndi kukhala ndi manja awiri ndi kupita ku gehena, kumene moto wake suzima. 44(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 45Ndipo ngati phazi lako likuchimwitsa, lidule. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa mʼmoyo olumala kusiyana ndi kukhala ndi mapazi awiri ndi kuponyedwa mu gehena. 46(Kumene mphutsi zake sizifa ndipo moto wake suzima). 47Ndipo ngati diso lako likuchimwitsa, likolowole. Ndi kwabwino kwa iwe kulowa ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi, kusiyana ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa mu gehena, 48kumene

“ ‘mphutsi zake sizifa

ndipo moto wake suzima.’

49Aliyense adzayesedwa ndi moto.

50“Mchere ndi wabwino, koma ngati utasukuluka, mungawukoleretsenso bwanji? Mukhale nawo mchere mwa inu nokha, ndipo mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.”

Słowo Życia

Marka 9:1-50

1—Zapewniam was: Niektórzy z obecnych tu—mówił dalej do uczniów—jeszcze za swojego życia ujrzą potęgę nadchodzącego królestwa Bożego!

Przemienienie

2Sześć dni później Jezus wziął ze sobą na szczyt pewnej góry Piotra, Jakuba i Jana. Poza nimi nie było tam nikogo. Nagle, na ich oczach, przemienił się: 3Jego płaszcz zalśnił taką nieziemską bielą, jakiej nie zdołałby osiągnąć żaden farbiarz. 4Potem zjawili się Eliasz i Mojżesz, którzy zaczęli z Nim rozmawiać.

5—Nauczycielu, jak dobrze, że tu jesteśmy!—wykrzyknął Piotr do Jezusa. —Jeśli chcesz, zbuduję trzy szałasy: dla Ciebie, dla Mojżesza i dla Eliasza.

6Powiedział tak, gdyż—podobnie jak pozostali—był sparaliżowany strachem i nie wiedział, co mówić. 7Ale zanim skończył, otoczył ich jasny obłok, z którego rozległ się głos:

—Oto mój ukochany Syn. Słuchajcie Go!

8Po chwili, gdy się rozejrzeli, stwierdzili, że poza Jezusem nie ma już nikogo. 9Schodząc z góry, Jezus nakazał im, aby do czasu Jego zmartwychwstania nikomu nie opowiadali o tym, co widzieli. 10Zatrzymali to więc dla siebie, ale często rozmawiali o tym we własnym gronie i zastanawiali się, co Jezus miał na myśli, mówiąc o zmartwychwstaniu. 11Zapytali Go też, dlaczego przywódcy religijni twierdzą, że przed przyjściem Mesjasza musi pojawić się Eliasz.

12—Mają rację—odparł Jezus. —Eliasz musi przyjść i wszystko przygotować. A co prorocy napisali o Mnie, Synu Człowieczym? Mam cierpieć i być odrzucony! 13Mówię wam: Eliasz już przyszedł, ale—zgodnie z tym, co przepowiedzieli prorocy—został haniebnie potraktowany!

Uzdrowienie chłopca zniewolonego przez demona

14U podnóża góry zastali ogromny tłum, otaczający pozostałych dziewięciu uczniów, żywo dyskutujących z przywódcami religijnymi. 15Ludzie, uradowani widokiem Jezusa, przybiegli Go powitać.

16—O co chodzi?—zapytał.

17—Nauczycielu!—odezwał się ktoś z tłumu. —Przyprowadziłem tu mojego syna, żebyś go uzdrowił. Opanował go zły duch i nie może mówić. 18Gdy go napada, chłopiec rzuca się na ziemię z pianą na ustach, zgrzyta zębami i sztywnieje. Prosiłem Twoich uczniów, żeby wypędzili demona, lecz oni nie potrafili.

19—Dlaczego wciąż brakuje wam wiary?—zwrócił się do nich Jezus. —Jak długo jeszcze muszę być z wami, żebyście wreszcie uwierzyli? Jak długo mam was znosić? Przyprowadźcie tu chłopca!

20Ujrzawszy Jezusa, demon rzucił chłopca na ziemię tak gwałtownie, że ten wił się w konwulsjach, z pianą na ustach.

21—Jak długo na to cierpi?—zapytał Jezus ojca.

—Od dzieciństwa. 22Zły duch często usiłuje go zabić, rzucając go w ogień lub wodę. Zmiłuj się nad nami i jeśli możesz, zrób coś!

23—„Jeśli możesz”?—powtórzył Jezus. —Dla tego, kto wierzy, wszystko jest możliwe!

24—Wierzę!—gorąco zapewnił ojciec. —Ale, proszę, pomóż mi wierzyć jeszcze mocniej!

25A ponieważ tłum gęstniał coraz bardziej, Jezus zwrócił się do demona:

—Duchu niemy i głuchy! Rozkazuję ci: Opuść to dziecko raz na zawsze!

26Demon przeraźliwie krzyknął, targnął chłopcem i wyszedł z niego, pozostawiając go leżącego nieruchomo i bezwładnie, jak gdyby był martwy. Przez tłum przebiegł szmer:

—Nie żyje…

27Lecz Jezus wziął go za rękę i podniósł. Chłopiec był całkowicie uzdrowiony!

28Później, gdy Jezus znalazł się w domu sam na sam z uczniami, zapytali Go:

—Dlaczego my nie mogliśmy wypędzić tego demona?

29—Takiego rodzaju złych duchów nie uda się wypędzić bez modlitwy—odpowiedział.

30Gdy opuścili to miejsce, przemierzali dalej Galileę, lecz Jezus unikał tłumów. Chciał bowiem poświęcić czas przygotowaniu uczniów na to, co miało nastąpić. 31Mówił im:

—Ja, Syn Człowieczy, zostanę wkrótce wydany w ręce ludzi, którzy Mnie zabiją, ale trzeciego dnia zmartwychwstanę.

32Uczniowie nie rozumieli tego, lecz bali się prosić Go o wyjaśnienie.

Kto jest największy?

33Tak doszli do Kafarnaum. Gdy rozgościli się w domu, gdzie ich przyjęto, Jezus zapytał:

—O czym to dyskutowaliście w drodze?

34Lecz oni wstydzili się odpowiedzieć, ponieważ spierali się o to, który z nich jest najważniejszy. 35Wtedy Jezus usiadł, zebrał Dwunastu wokół siebie i rzekł:

—Kto chce być największy, musi stać się sługą wszystkich!

36Postawił wśród nich dziecko i obejmując je ramieniem powiedział:

37—Każdy, kto ze względu na Mnie przyjmie nawet takie małe dziecko, Mnie przyjmie; a kto Mnie przyjmie—przyjmie samego Ojca, który Mnie posłał.

Kto nie jest przeciwko nam, jest z nami

38Niedługo potem Jan—jeden z uczniów—zwrócił się do Jezusa:

—Nauczycielu, spotkaliśmy człowieka, który w Twoim imieniu wypędza demony, i zabroniliśmy mu działać. Nie należy bowiem do naszego grona.

39—Nie zabraniajcie mu—odparł Jezus. —Kto w moim imieniu czyni cuda, nieprędko wystąpi przeciwko Mnie. 40Każdy, kto nie jest nam przeciwny, jest naszym sprzymierzeńcem. 41Zapewniam was, że jeśli ktoś poda wam choćby kubek wody—dlatego, że należycie do Mnie—nie ominie go nagroda!

Powód do grzechu

42Lecz jeśli z czyjegoś powodu upadnie choćby jeden z najmniejszych moich uczniów, to lepiej byłoby, aby takiemu człowiekowi przywiązano do szyi kamień młyński i wrzucono go do morza. 43-44Jeśli więc twoja własna ręka skłania cię do grzechu—odetnij ją; lepiej bowiem wejść do nieba z jedną ręką, niż mając dwie znaleźć się w ogniu piekielnym, który nigdy nie gaśnie. 45-46Podobnie, jeśli twoja noga skłania cię do grzechu—odetnij ją; lepiej jest dla ciebie kalekim wejść do nieba, niż z obiema nogami zostać wrzuconym do piekła. 47Jeśli twoje oko skłania cię do grzechu—wyłup je; lepiej bowiem wejść do królestwa Bożego z jednym okiem, niż z dwojgiem oczu być wrzuconym do piekła, 48gdzie udręka się nie kończy i ogień nigdy nie gaśnie. 49Tam wszyscy zostaną „posoleni” ogniem cierpień.

50Sól jest dobra; lecz jeśli utraci swój smak, staje się bezwartościowa. Nie utraćcie więc i wy swoich właściwości, ale zachowajcie pokój między sobą.