Luka 1 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 1:1-80

Mawu Oyamba

1Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu, 2monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu. 3Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo, 4kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.

Aneneratu za Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

5Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni. 6Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse. 7Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.

8Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu, 9Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani. 10Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.

11Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira. 12Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha. 13Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane. 14Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake, 15chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa. 16Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo. 17Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”

18Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”

19Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu. 20Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”

21Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu. 22Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.

23Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo. 24Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu. 25Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”

Aneneratu za Kubadwa kwa Yesu

26Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya, 27kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya. 28Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”

29Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere. 30Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu. 31Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu. 32Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide, 33ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.”

34Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”

35Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu. 36Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi. 37Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”

38Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”

Mariya Acheza kwa Elizabeti

39Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya, 40kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti. 41Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera. 42Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke! 43Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine? 44Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe. 45Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”

Nyimbo ya Mariya

46Ndipo Mariya anati:

“Moyo wanga ulemekeza Ambuye.

47Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,

48pakuti wakumbukira

kudzichepetsa kwa mtumiki wake.

Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,

49pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu,

dzina lake ndi loyera.

50Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye

kufikira mibadomibado.

51Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake;

Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.

52Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu,

koma wakweza odzichepetsa.

53Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino

koma anachotsa olemera wopanda kanthu.

54Iye anathandiza mtumiki wake Israeli,

pokumbukira chifundo chake.

55Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse

monga ananena kwa makolo athu.”

56Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.

Kubadwa kwa Yohane Mʼbatizi

57Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna. 58Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.

59Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya, 60koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”

61Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”

62Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo. 63Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.” 64Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu. 65Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi. 66Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.

Nyimbo ya Zakariya

67Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,

68“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli

chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.

69Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife

mu nyumba ya mtumiki wake Davide.

70(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera),

71chipulumutso kuchoka kwa adani athu

ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,

72kuonetsa chifundo kwa makolo athu

ndi kukumbukira pangano lake loyera,

73lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:

74kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu,

ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,

75mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.

76“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba;

pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,

77kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso

kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,

78chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu,

ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,

79kuwalira iwo okhala mu mdima

ndi mu mthunzi wa imfa,

kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”

80Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.

Słowo Życia

Łukasza 1:1-80

Wprowadzenie

1Dostojny Teofilu! Wielu już starało się uporządkować wydarzenia z życia Chrystusa, 2zgodnie z tym, co przekazali naoczni świadkowie i pierwsi głosiciele słowa. 3Ja również uznałem za słuszne przestudiować je, od pierwszego do ostatniego, i dokładnie opisać wszystko po kolei, 4abyś był pewien tego, czego się nauczyłeś.

Zapowiedź narodzenia Jana Chrzciciela

5Zacznę od historii o pewnym kapłanie, Zachariaszu, który żył w Judei za panowania króla Heroda. Należał on do kapłańskiej grupy Abiasza. Z kapłańskiego rodu Aarona pochodziła również jego żona, Elżbieta. 6Byli to ludzie prawi w oczach Boga, żyjący w zgodzie zarówno z duchem, jak i z literą całego Bożego Prawa. 7Oboje dożyli sędziwego wieku, ale nie mieli dzieci, gdyż Elżbieta była bezpłodna.

8Pewnego dnia, grupa Zachariasza pełniła służbę w świątyni, jemu zaś w drodze losowania 9przypadł zaszczyt wejścia do miejsca świętego i złożenia Panu ofiary z kadzidła. 10W tym czasie na dziedzińcu znajdowało się wielu modlących się ludzi.

11Będąc w świątyni, Zachariasz ujrzał nagle anioła Bożego stojącego po prawej stronie ołtarza kadzenia. 12Ogarnęły go zdumienie i strach. 13Lecz anioł powiedział:

—Nie bój się, Zachariaszu! Przyszedłem ci oznajmić, że Bóg wysłuchał twojej modlitwy: Elżbieta, twoja żona, urodzi syna. Daj mu na imię Jan. 14Stanie się on przyczyną radości nie tylko dla was, ale także dla wielu innych ludzi. 15Będzie wielki w oczach Pana. Nie będzie pił wina ani innych tego rodzaju napojów i już w łonie matki zostanie napełniony Duchem Świętym. 16Przekona on wielu potomków Izraela, aby powrócili do Pana, swojego Boga. 17Będzie się odznaczał nieugiętym duchem i mocą proroka Eliasza. To on poprzedzi nadejście Mesjasza i przygotuje ludzi dla Pana, nauczając ich prawości. Pogodzi również rodziców z dziećmi.

18—To chyba niemożliwe?—odpowiedział Zachariasz aniołowi. —Jestem już przecież stary, a moja żona również jest w podeszłym wieku.

19—Ja jestem Gabriel—rzekł wtedy anioł. —Przebywam w najbliższym otoczeniu Boga. To On posłał mnie do ciebie z tą dobrą nowiną. 20Ponieważ mi jednak nie uwierzyłeś, staniesz się niemy aż do czasu spełnienia się wszystkiego, co zapowiedziałem.

21Tymczasem ludzie na dziedzińcu czekali na Zachariasza i dziwili się, dlaczego jeszcze nie wychodzi. 22Gdy się wreszcie ukazał, nie był w stanie wypowiedzieć ani słowa. Po jego gestach zebrani zorientowali się, że właśnie widział anioła. 23Zachariasz pozostał w świątyni jeszcze kilka dni i dopiero po zakończeniu swojej kapłańskiej służby powrócił do domu. 24Wkrótce jego żona zaszła w ciążę i przez pięć następnych miesięcy żyła w odosobnieniu.

25—Jakże dobry jest Pan!—cieszyła się. —Zdjął ze mnie hańbę bezdzietności.

Zapowiedź narodzenia Jezusa

26Gdy Elżbieta była w szóstym miesiącu ciąży, Bóg posłał anioła Gabriela do galilejskiego miasteczka Nazaret, 27do pewnej panny o imieniu Maria, która była narzeczoną Józefa, potomka króla Dawida. 28Gabriel, stanąwszy przed nią, powiedział:

—Witaj! Pan jest z tobą i obdarzył cię szczególną łaską!

29Oszołomiona Maria zastanawiała się, co miałoby oznaczać takie powitanie.

30—Nie bój się, Mario!—rzekł wtedy anioł. —Bóg zechciał ci okazać wyjątkową łaskę! 31Wkrótce poczniesz i urodzisz syna, któremu dasz na imię Jezus. 32Będzie On wielki i nazwą Go Synem Najwyższego. Bóg da Mu tron Jego przodka, króla Dawida. 33Będzie wiecznie panował nad Izraelem, a Jego królestwo nie będzie miało końca!

34—Ale jak to się stanie?—zapytała Maria. —Jestem jeszcze dziewicą!

35—Zstąpi na ciebie Duch Święty i osłoni cię moc Boga. Dlatego dziecko, które urodzisz, będzie świętym Synem Boga. 36Sześć miesięcy temu twoja krewna Elżbieta, uważana za bezpłodną, również zaszła w ciążę, mimo podeszłego wieku. 37Dla Boga bowiem wszystko jest możliwe.

38—Chcę służyć mojemu Panu—rzekła Maria—i jestem gotowa na wszystko, co się Jemu podoba. Niech się stanie tak, jak powiedziałeś.

Wtedy anioł odszedł.

Maria odwiedza Elżbietę

39Maria szybko udała się do rodzinnego miasta Zachariasza, położonego w górzystej krainie Judei, 40aby odwiedzić Elżbietę. 41Gdy tylko wypowiedziała słowa pozdrowienia, na dźwięk jej głosu poruszyło się w łonie Elżbiety dziecko, a ona sama została napełniona Duchem Świętym. 42Zawołała z radości i powiedziała do Marii:

—Jak bardzo Bóg wyróżnił cię spośród wszystkich kobiet i jak szczęśliwe jest twoje dziecko! 43To dla mnie zaszczyt, że odwiedziła mnie matka mojego Pana! 44Gdy tylko usłyszałam twoje pozdrowienie, z radości poruszyło się we mnie dzieciątko! 45Naprawdę Bóg obdarzył cię wyjątkowym szczęściem, bo uwierzyłaś, że spełnią się Jego słowa.

Pieśń Marii

Maria powiedziała wtedy:

46—Z całej duszy wielbię Pana,

47mojego Boga i Zbawiciela!

Obdarzył mnie bowiem wielką radością

48i dostrzegł swoją pokorną służebnicę!

Dlatego od tej pory wszystkie pokolenia

będą mnie nazywać szczęśliwą.

49Wszechmocny i Święty

dokonał bowiem w moim życiu

wspaniałych rzeczy.

50On w każdym pokoleniu okazuje miłość tym,

którzy są Mu posłuszni.

51Jego moc jest niezwyciężona!

Rozproszył ludzi dumnych i wyniosłych.

52Zrzucił z tronu władców,

a wywyższył pokornych.

53Nakarmił głodnych,

a bogatych odesłał z pustymi rękami.

54Pomógł swojemu słudze, Izraelowi

i nie zapomniał o miłości,

55którą na zawsze przyrzekł Abrahamowi

oraz jego dzieciom, naszym przodkom.

56Maria przebywała u Elżbiety około trzech miesięcy, po czym wróciła do domu.

Narodzenie Jana Chrzciciela

57Gdy nadszedł czas, Elżbieta urodziła syna. 58Wiadomość o łasce, okazanej jej przez Pana, dotarła wkrótce do krewnych i znajomych i wszyscy bardzo się ucieszyli. 59Ósmego dnia po urodzeniu zeszli się na uroczystość obrzezania. Chcieli, aby dziecko otrzymało imię ojca—Zachariasza, 60ale Elżbieta sprzeciwiła się temu:

—Nie! Damy mu na imię Jan—rzekła.

61—Dlaczego? Przecież w całej twojej rodzinie nie ma ani jednej osoby o takim imieniu!

62Zwrócili się więc do Zachariasza, ojca dziecka. 63On zaś gestem poprosił, aby mu podano tabliczkę, i ku zdziwieniu obecnych napisał: „Niech się nazywa Jan”. 64W tej samej chwili odzyskał mowę i zaczął wielbić Boga.

65Wszystkich zebranych ogarnął lęk i podziw, a wiadomość o tym zdarzeniu szybko rozeszła się po całej okolicy 66i zastanawiano się:

—Kim będzie to dziecko? Widać, że Bóg naprawdę nad nim czuwa.

Pieśń Zachariasza

67Wielbiąc Boga, Zachariasz został napełniony Duchem Świętym i zaczął prorokować:

68—Chwała Panu, Bogu Izraela!

Przyszedł bowiem, aby uratować swój lud.

69-70Tak, jak niegdyś obiecał

przez swoich świętych proroków,

posłał potężnego Zbawiciela

z rodu króla Dawida, swojego sługi.

71On nas wybawi z rąk naszych wrogów

i tych, którzy nas nienawidzą.

72Bóg zmiłował się nad naszymi przodkami,

pamiętając o swoim świętym przymierzu.

73I dotrzymał przysięgi,

którą złożył Abrahamowi, naszemu przodkowi,

74-75że uwolni nas od wrogów i pozwoli,

abyśmy bez lęku, w świętości i prawości,

mogli służyć Mu aż do końca naszych dni.

76A ty, synku, zostaniesz prorokiem Najwyższego.

Pójdziesz przed Panem i przygotujesz Mu drogę.

77I pokażesz ludziom Boże zbawienie,

dokonujące się przez odpuszczenie grzechów,

78dzięki łasce naszego Boga.

Ona to zabłyśnie jak niebiańska światłość,

79i oświeci pogrążonych w ciemności i mroku śmierci.

Ona też wprowadzi nas na drogę pokoju!

80Czas upływał, a chłopiec rozwijał się i wzmacniał duchowo. Gdy dorósł, zamieszkał samotnie na pustyni i przebywał tam aż do chwili rozpoczęcia swojej publicznej działalności w Izraelu.