Marko 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Marko 7:1-37

Miyambo ya Makolo ya Ayuda

1Afarisi ndi ena mwa aphunzitsi amalamulo omwe anachokera ku Yerusalemu anasonkhana momuzungulira Yesu ndipo 2iwo anaona ophunzira ake akudya chakudya ndi mʼmanja mwakuda kapena kuti mʼmanja mosasamba. 3(Afarisi ndi Ayuda onse sadya pokhapokha atasamba mʼmanja, kusunga mwambo wa makolo awo. 4Akabwera kuchokera ku msika samadya pokhapokha atasamba. Ndipo amasunga miyambo ina yambiri monga, kutsuka zikho, mitsuko ndi maketulo).

5Choncho Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anafunsa Yesu kuti, “Nʼchifukwa chiyani ophunzira anu satsatira mwambo wa makolo, mʼmalo mwake amangodya chakudya ndi mʼmanja mwakuda?”

6Iye anayankha kuti, “Yesaya ananena zoona pamene ananenera za inu achiphamaso; monga kunalembedwa kuti:

“Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

7Amandilambira Ine kwachabe;

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.

8Mwasiya malamulo a Mulungu ndipo mwagwiritsitsa miyambo ya anthu.”

9Ndipo anawawuzanso kuti, “Inu muli ndi njira yabwino yokankhira kumbali malamulo a Mulungu kuti mukatsatire miyambo yanuyo! 10Pakuti Mose anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako,’ ndipo, ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 11Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukanayenera kulandira kuchokera kwa ine ndi Korobani’ (kutanthauza kuti, mphatso yoperekedwa kwa Mulungu), 12pamenepo inu simumalola kuti achitire kanthu kalikonse abambo kapena amayi ake. 13Potero mumachepetsa mawu a Mulungu kukhala wopanda mphamvu ndi miyambo yanu imene mumapatsirana. Ndipo mumachita zinthu zina zambiri monga zimenezi.”

14Yesu anayitananso gulu la anthu ndipo anati, “Tandimverani nonsenu, ndipo zindikirani izi. 15Palibe kanthu kunja kwa munthu kamene kakalowa mwa iye kangamusandutse wodetsedwa. Koma zimene zituluka mwa munthu ndizo zimupanga kukhala wodetsedwa.” 16(Ngati wina ali ndi makutu akumva amve).

17Atalisiya gulu la anthu ndi kulowa mʼnyumba, ophunzira ake anamufunsa za fanizoli 18Iye anawafunsa kuti, “Kodi nanunso simumvetsetsa? Kodi simukuona kuti palibe kanthu kamene kakalowa mwa munthu kochokera kunja kakhoza kumudetsa? 19Pakuti sikalowa mu mtima wake koma mʼmimba mwake, ndipo kenaka kamatuluka kunja.” (Ndi mawu amenewa, Yesu anayeretsa zakudya zonse).

20Anapitiriza kuti, “Chimene chichokera mwa munthu ndi chomwe chimamudetsa. 21Pakuti kuchokera mʼkati mwa mitima ya anthu, mumatuluka maganizo oyipa, chiwerewere, kuba, kupha, chigololo, 22dyera, nkhwidzi, chinyengo, machitidwe onyansa, kaduka, chipongwe, kudzikuza ndi kupusa. 23Zoyipa zonsezi zimatuluka mʼkati ndipo zimadetsa munthu.”

Chikhulupiriro cha Mayi wa ku Siriya Fonisia

24Yesu anachoka kumalo amenewo napita ku madera a Turo. Iye analowa mʼnyumba ndipo sanafune wina kuti adziwe zimenezi; komabe sanathe kudzibisa. 25Kunena zoona, amayi amene kamwana kawo kakakazi kanali kogwidwa ndi mzimu woyipa, atangomva za Iye, anabwera nagwada pa mapazi ake. 26Mayiyu anali Mhelene, wobadwira ku Fonisia wa ku Siriya. Anamupempha Yesu kuti atulutse chiwanda mwa mwana wake.

27Iye anamuwuza kuti, “Choyamba asiye ana adye zimene akuzifuna, pakuti si kwabwino kutenga buledi wa ana ndi kuponyera agalu awo.”

28Mayiyo anayankha kuti, “Inde Ambuye, koma ngakhale agalu amadya zomwe zimagwa pansi kuchokera pa tebulo la ana.”

29Ndipo Iye anamuwuza kuti, “Chifukwa cha yankholi, ukhoza kupita; chiwanda chachoka mwa mwana wako wamkazi.”

30Atapita kwawo anakapeza mwana wake aligone pa bedi, chiwanda chitatuluka.

Kuchiritsidwa kwa Munthu Wosamva ndi Wosayankhula

31Ndipo Yesu anachoka ku dera la Turo nadutsa pakati pa Sidoni, kutsikira ku nyanja ya Galileya kupita ku dera la Dekapoli. 32Kumeneko anthu ena anabweretsa kwa Iye munthu amene anali wosamva ndi wosayankhula, ndipo anamupempha kuti asanjike dzanja pa iye.

33Atamutengera iye pambali, patali ndi gulu la anthu, Yesu analowetsa zala zake mʼmakutu a munthuyo. Kenaka anapaka malovu pachala ndi kukhudza lilime la munthuyo. 34Iye anayangʼana kumwamba ndipo ndi mawu otsitsa moyo, anati kwa iye, “Efataa!” (Kutanthauza kuti, “Tsekuka!”) 35Atachita izi, makutu a munthuyo anatsekuka komanso lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula momveka bwino.

36Yesu anawalamula kuti asawuze wina aliyense. Koma pamene anapitiriza kuwaletsa, iwo anapitiriza kuyankhula za izi. 37Anthu anadabwa kwambiri. Iwo anati, “Wachita zonse bwino, ngakhale Iyenso atsekula makutu a osamva ndi osayankhula kuti ayankhule.”

New Russian Translation

Марка 7:1-37

Иисус говорит о внутренней чистоте

(Мат. 15:1-20)

1Однажды собрались вокруг Него фарисеи и некоторые учители Закона из Иерусалима. 2Они обратили внимание, что некоторые ученики Иисуса принимали пищу ритуально нечистыми, то есть неомытыми руками. 3Фарисеи, и вообще иудеи, строго следуя обычаям своих предков7:3 Духовные учители иудеев разработали целую систему обрядового очищения, намного превосходящую по своим требованиям то, что Бог предписал в Законе. Эти установления передавались из поколения в поколение в устной форме., не садятся есть, не помыв установленным образом руки. 4Они не едят ничего, принесенного с рынка, пока не совершат ритуального омовения. Ими соблюдается также и множество других установлений, как, например, о мытье чаш, кувшинов и медной посуды. 5Поэтому фарисеи и учители Закона спросили Иисуса:

– Почему Твои ученики нарушают обычаи наших предков? Почему они едят нечистыми руками?

6Иисус ответил им:

– Прав был Исаия, когда пророчествовал о вас, лицемерах:

«Этот народ чтит Меня губами,

но сердца их далеки от Меня.

7Они поклоняются Мне впустую,

и их учение состоит из человеческих предписаний»7:6-7 Ис. 29:13..

8Оставив Божью заповедь, вы соблюдаете человеческое предание. 9Вы ловко умеете подменять заповедь Божью вашими собственными традициями. 10Ведь Моисей сказал: «Почитай отца и мать»7:10 Исх. 20:12; Втор. 5:16. и «Кто злословит отца или мать, тот должен быть предан смерти»7:10 Исх. 21:17; Лев. 20:9.. 11Вы же говорите, что если человек скажет отцу или матери: «То, чем я мог бы тебе помочь, – Корбан» (то есть дар Богу), 12то вы уже позволяете ему ничего не делать для своего отца или матери7:11-12 Произнеся эти слова, человек, по мнению духовных учителей, освобождался от обязанности помогать своим нуждающимся родителям. И в данном случае никого не интересовало, будут ли эти средства потрачены на нужды храма или нет.. 13Вы отменяете Божье слово собственным преданием, которое вы установили, и многое, подобное этому, вы делаете.

14Иисус снова подозвал к Себе народ и сказал:

– Выслушайте Меня все и постарайтесь понять. 15Ничто из того, что входит в человека извне, не может сделать его нечистым; нечистым человека делает то, что исходит из него. 16Если у кого есть уши, чтобы слышать, пусть слышит7:16 Ст. 16 отсутствует в древнейших рукописях Евангелия от Марка..

17Когда Иисус оставил толпу и вошел в дом, ученики спросили Его об этой притче.

18– Так и вы тоже не понимаете? – сказал Он им. – Неужели вы не понимаете, что все, что входит в человека извне, не может осквернить его? 19Оно входит не в сердце человека, а в его желудок, а потом выходит вон. (Так Он объявил чистой любую пищу.) 20Но то, что исходит из человека, – продолжал Он, – вот это и оскверняет его. 21Потому что изнутри, из сердца человека, исходят злые мысли, разврат, воровство, убийство, 22супружеская неверность, жадность, злоба, коварство, распутство, зависть7:22 Букв.: «дурной глаз» – на языке иудеев это выражение было фразеологическим оборотом, обозначающим жадного или завистливого человека (см. Мат. 20:15)., клевета, надменность и безрассудство. 23Все это зло исходит изнутри, и именно оно оскверняет человека.

Вера язычницы

(Мат. 15:21-28)

24Оттуда Иисус отправился в окрестности Тира. Он остановился в одном доме и не хотел, чтобы кто-либо знал о Его приходе, но Ему все равно не удалось сохранить это в тайне. 25О приходе Иисуса узнала одна женщина, маленькая дочь которой была одержима нечистым духом. Эта женщина пришла и пала к Его ногам, 26а она была язычницей, сирофиникиянкой. И она попросила Иисуса, чтобы Он изгнал демона из ее дочери.

27Иисус сказал ей:

– Пусть сначала наедятся дети7:27 То есть иудеи., ведь нехорошо будет забрать хлеб у детей и бросить собачкам7:27 Для иудеев собака считалась нечистым животным. Израильтяне часто называли язычников собаками, но в данном случае Иисус не желал кого-либо обидеть, Он просто приводит иллюстрацию из жизни..

28– Господи, – ответила женщина, – но ведь и собачки едят под столом крошки, которые роняют дети.

29– За твой ответ, – сказал ей Иисус, – иди, демон вышел из твоей дочери.

30Она пошла домой и увидела, что ее дочь лежит в постели, а демон из нее вышел.

Иисус исцеляет глухого и косноязычного человека

(Мат. 15:29-31)

31Возвращаясь из окрестностей Тира, Иисус через Сидон вышел к Галилейскому озеру в области Десятиградия. 32Там к Иисусу привели глухого и косноязычного человека и попросили возложить на него руку. 33Иисус отвел его в сторону, вложил Свои пальцы ему в уши, затем сплюнул Себе на пальцы и прикоснулся к языку человека. 34Потом Он поднял глаза к небу, тяжело вздохнул и сказал:

– Эффата!

Это означает: «Откройся!»

35К человеку тотчас же вернулся слух, скованный язык стал двигаться, и он начал говорить ясно. 36Иисус запретил людям рассказывать об этом исцелении. Однако чем больше Он запрещал, тем больше они рассказывали. 37Их удивлению не было предела.

– Все, что Он делает – хорошо, – говорили люди. – У Него и глухие начинают слышать, и немые – говорить!