Maliro 5 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Maliro 5:1-22

1Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira;

yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.

2Apereka cholowa chathu kwa obwera,

nyumba zathu kwa alendo.

3Takhala amasiye ndi wopanda abambo,

amayi athu ali ngati akazi amasiye.

4Tiyenera kugula madzi amene timamwa,

nkhuni zathunso nʼzogula.

5Otilondola atigwira pakhosi;

tafowoka ndipo sakutilola kupumula.

6Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya

kuti tipeze chakudya.

7Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale,

koma chilango chawo chili pa ife.

8Akapolo akutilamulira,

ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.

9Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe

chifukwa cha lupanga mʼchipululu.

10Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo,

chifukwa cha kuwawa kwa njala.

11Amayi agwiriridwa mu Ziyoni,

ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.

12Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo,

akuluakulu sakuwalemekeza.

13Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu;

anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.

14Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda;

achinyamata aleka nyimbo zawo.

15Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu;

kuvina kwathu kwasanduka maliro.

16Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu.

Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!

17Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi,

chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,

18pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja,

nkhandwe zikungoyendayendapo.

19Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya;

mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.

20Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse?

Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?

21Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere;

mukonzenso masiku athu akhale monga akale,

22pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu,

ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米哀歌 5:1-22

求耶和华怜悯

1耶和华啊,求你顾念我们的遭遇,

看看我们所受的耻辱!

2我们的土地被陌生人侵占,

我们的房屋落入外族人手中。

3我们成了丧父的孤儿,

我们的母亲成了寡妇。

4我们喝水要付钱,

烧的柴要用钱买。

5敌人紧追不舍,

我们疲惫不堪,不得安歇。

6为了得到食物,

我们向埃及亚述卑躬屈膝。

7我们的祖先犯了罪,

已经逝去,

我们却要承担他们的罪责。

8奴仆做了我们的主人,

无人从他们手中解救我们。

9旷野中杀机四伏,

我们冒着生命危险才得到粮食。

10我们因饥饿而发热,

皮肤热如烤炉。

11妇女在锡安遭强暴,

少女在犹大被奸污。

12首领双手被吊起来,

老人得不到尊敬。

13青年被迫推磨,

孩童肩背柴捆,步履蹒跚。

14老人不再坐在城门口,

青年不再弹琴奏乐。

15我们心中的快乐消失,

我们的舞蹈变成了哀哭。

16荣耀的冠冕从我们头上落下。

我们犯了罪,我们有祸了!

17此情此景使我们黯然神伤,

泪眼模糊。

18锡安山一片荒凉,

豺狼四处游荡。

19耶和华啊,你永远掌权,

你的宝座世代长存。

20你为何永远忘记我们?

为何如此长久地弃绝我们?

21耶和华啊,求你使我们回到你身边,

让我们归向你,

恢复我们昔日的繁荣!

22难道你完全弃绝了我们,

仍然向我们大发烈怒吗?